< Job 36 >

1 Elihu nastavi i reče:
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 “Strpi se malo, pa ću te poučit', jer još nisam sve rekao za Boga.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 Izdaleka ću svoje iznijet' znanje da Stvoritelja svojega opravdam.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 Zaista, za laž ne znaju mi riječi, uza te je čovjek znanjem savršen.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 Gle, Bog je silan, ali ne prezire, silan je snagom razuma svojega.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 Opakome on živjeti ne daje, nevoljnicima pravicu pribavlja.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 S pravednika on očiju ne skida, na prijestolje ih diže uz kraljeve da bi dovijeka bili uzvišeni.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 Ako su negvam' oni okovani i užetima nevolje sputani,
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 djela njihova on im napominje, kazuje im grijeh njine oholosti.
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 Tad im otvara uho k opomeni i poziva ih da se zla okane.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 Poslušaju li te mu se pokore, dani im završavaju u sreći, u užicima godine njihove.
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 Ne slušaju li, od koplja umiru, zaglave, sami ne znajući kako.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 A srca opaka mržnju njeguju, ne ištu pomoć kad ih on okuje;
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 u cvatu svoga dječaštva umiru i venu poput hramskih milosnika.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Nevoljnog on bijedom njegovom spasava i u nesreći otvara mu oči:
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 izbavit će te iz ždrijela tjeskobe k prostranstvima bezgraničnim izvesti, k prepunu stolu mesa pretiloga.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Ako sudio nisi opakima, ako si pravo krnjio siroti,
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 nek' te obilje odsad ne zavede i nek' te dar prebogat ne iskvari.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Nek' ti je gavan k'o čovjek bez zlata, a čovjek jake ruke poput slaba.
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Ne goni one koji su ti tuđi da rodbinu na njino mjesto staviš.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Pazi se da u nepravdu ne skreneš, jer zbog nje snađe tebe iskušenje.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 Gle, uzvišen je Bog u svojoj snazi! Zar učitelja ima poput njega?
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Tko je njemu put njegov odredio? Tko će mu reći: 'Radio si krivo'?
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Spomeni se veličati mu djelo što ga pjesmama ljudi opjevaše.
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 S udivljenjem svijet čitav ga promatra, divi se čovjek, pa ma izdaleka.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 Veći je Bog no što pojmit' možemo, nedokučiv je broj ljeta njegovih!
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 U visini on skuplja kapi vode te dažd u paru i maglu pretvara.
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 Pljuskovi tada pljušte iz oblaka, po mnoštvu ljudskom dažde obilato.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 Tko li će shvatit' širenje oblaka, tutnjavu strašnu njegovih šatora?
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Gle, on nad sobom razastire svjetlost i dno morsko on vodama pokriva.
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 Pomoću njih on podiže narode, u izobilju hranom ih dariva.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 On munju drži objema rukama i kazuje joj kamo će zgoditi.
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Glasom gromovnim sebe navješćuje, stiže s gnjevom da zgromi opačinu.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

< Job 36 >