< Job 3 >
1 Napokon otvori Job usta i prokle dan svoj;
Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
2 poče svoju besjedu i reče:
Ndipo Yobu anati:
3 “O, ne bilo dana kad sam se rodio i noći što javi: 'Začeo se dječak!'
“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
4 U crnu tminu dan taj nek se prometne! S visina se njega Bog ne spominjao, svjetlost sunčeva ne svijetlila mu više!
Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
5 Mrak i sjena smrtna o nj se otimali, posvema ga tmina gusta prekrila, pomrčine dnevne stravom ga morile!
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
6 O, da bi ga tama svega presvojila, nek' se ne dodaje danima godine, nek' ne ulazi u brojenje mjeseci!
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
7 A noć ona bila žalosna dovijeka, ne čulo se u njoj radosno klicanje!
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
8 Prokleli je oni štono dan proklinju i Levijatana probudit' su kadri!
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
9 Pomrčale zvijezde njezina svanuća, zaludu se ona vidjelu nadala, i zorinih vjeđa ne gledala nigda!
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 Što mi od utrobe ne zatvori vrata da sakrije muku od mojih očiju!
Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
11 Što nisam mrtav od krila materina, što ne izdahnuh izlazeć' iz utrobe?
“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 Čemu su me dva koljena prihvatila i dojke dvije da me nejaka podoje?
Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 U miru bih vječnom počivao sada, spavao bih, pokoj svoj bih uživao
Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 s kraljevima i savjetnicima zemlje koji su sebi pogradili grobnice,
pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 ili s knezovima, zlatom bogatima, što su kuće svoje srebrom napunili.
pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 Ne bih bio - k'o nedonošče zakopano, k'o novorođenče što svjetla ne vidje.
Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 Zlikovci se više ne obijeste ondje, iznemogli tamo nalaze počinka.
Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 Sužnjeve na miru tamo ostavljaju: ne slušaju više poviku stražara.
A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 Malen ondje leži zajedno s velikim, rob je slobodan od gospodara svoga.
Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
20 Čemu darovati svjetlo nesretniku i život ljudima zagorčene duše
“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 koji smrt ištu, a ona ne dolazi, i kao za blagom za njome kopaju?
kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 Grobnom bi se humku oni radovali, klicali od sreće kad bi grob svoj našli.
amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
23 Što će to čovjeku kom je put sakriven, koga je Bog sa svih strana zapriječio?
Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 Zato videć' hranu, uzdahnuti moram, k'o voda se moji razlijevaju krici.
Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 Obistinjuje se moje strahovanje, snalazi me, evo, čega god se bojah.
Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 Pokoja ni mira meni više nema, u mukama mojim nikad mi počinka.”
Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”