< Job 19 >

1 Job progovori i reče:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “TÓa dokle ćete mučit' dušu moju, dokle ćete me riječima satirat'?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 Već deseti put pogrdiste mene i stid vas nije što me zlostavljate.
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 Pa ako sam zastranio doista, na meni moja zabluda ostaje.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 Mislite li da ste me nadjačali i krivnju moju da ste dokazali?
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 Znajte: Bog je to mene pritisnuo i svojom me je on stegnuo mrežom.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 Vičem: 'Nasilje!' - nema odgovora; vapijem - ali za me pravde nema.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 Sa svih strana put mi je zagradio, sve staze moje u tminu zavio.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 Slavu je moju sa mene skinuo, sa moje glave strgnuo je krunu.
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 Podsijeca me odasvud te nestajem; k'o drvo, nadu mi je iščupao.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 Raspalio se gnjev njegov na mene i svojim me drži neprijateljem.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 U bojnom redu pristižu mu čete, putove proti meni nasipaju, odasvud moj opkoljavaju šator.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 Od mene su se udaljila braća, otuđili se moji poznanici.
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 Nestade bližnjih mojih i znanaca, gosti doma mog zaboraviše me.
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 Sluškinjama sam svojim kao stranac, neznanac sam u njihovim očima.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 Slugu zovnem, a on ne odgovara i za milost ga moram zaklinjati.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 Mojoj je ženi dah moj omrznuo, gadim se djeci vlastite utrobe.
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 I deranima na prezir tek služim, ako se dignem, rugaju se meni.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 Pouzdanicima sam svojim mrzak, protiv mene su oni koje ljubljah.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 Kosti mi se za kožu prilijepiše, osta mi jedva koža oko zuba.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Smilujte mi se, prijatelji moji, jer Božja me je ruka udarila.
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Zašto da me k'o Bog sam progonite, zar se niste moga nasitili mesa?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 O, kad bi se riječi moje zapisale i kad bi se u mjed tvrdu urezale;
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 kad bi se željeznim dlijetom i olovom u spomen vječan u stijenu uklesale!
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 Ja znadem dobro: moj Izbavitelj živi i posljednji će on nad zemljom ustati.
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 A kad se probudim, k sebi će me dići: iz svoje ću puti tad vidjeti Boga.
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Njega ja ću kao svojega gledati, i očima mojim neće biti stranac: za njime srce mi čezne u grudima.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 Kad kažete: 'Kako ćemo ga goniti? Koji ćemo razlog protiv njega naći?',
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 mača tad se bojte: grijehu mač je kazna. Saznat ćete tada da imade suda!”
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”

< Job 19 >