< Jeremija 46 >
1 Riječ koju Jahve uputi proroku Jeremiji protiv naroda.
Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.
2 Još o Egiptu. Protiv vojske faraona Neka, kralja egipatskoga, što bijaše kod rijeke Eufrata, u Karkemišu, i kralj Nabukodonozor ga potuče, četvrte godine Jojakima, sina Jošijina, kralja judejskoga.
Kunena za Igupto: Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,
3 Pripremite štitove i oklope! Naprijed, u boj!
anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo, ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!
4 Upregnite konje! Na kola, vozači! Postavite se pod kacigama! Naperite koplja! Navucite oklope!
Mangani akavalo, ndipo kwerani inu okwerapo! Khalani pa mzere mutavala zipewa! Nolani mikondo yanu, valani malaya anu ankhondo!
5 Što vidim? Zaprepašteni, uzmiču? Junaci njihovi, poraženi, u bijeg udariše glavom bez obzira! Užas odasvud - riječ je Jahvina.
Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani? Achita mantha akubwerera, ankhondo awo agonjetsedwa. Akuthawa mofulumirapo osayangʼananso mʼmbuyo, ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,” akutero Yehova.
6 Ni najbrži ne umače, ni najhrabriji ne uteče! Na sjeveru, na obali Eufrata, posrću i padaju.
Waliwiro sangathe kuthawa ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka. Akunka napunthwa ndi kugwa kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.
7 Tko se to diže poput Nila, čije vode šume, k'o brzaci nabujaše?
“Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo, ngati mtsinje wa madzi amkokomo?
8 To Egipat se diže poput Nila, k'o brzaci vode mu nabujaše. I govori: dići ću se, poplaviti zemlju, opustošiti gradove i pučanstvo!
Igupto akusefukira ngati Nailo, ngati mitsinje ya madzi amkokomo. Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi; ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’
9 Konji, naprijed! Poletite, kola bojna! Navalite, ratnici! Kušiti, Putijci, štitom zaštićeni, i Ludijci, što lukom strijeljate!
Tiyeni, inu akavalo! Thamangani inu magaleta! Tulukani, inu ankhondo, ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango, ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.
10 Ovo je dan Jahve nad Vojskama - dan osvete da se dušmanima svojim osveti: mač će se nažderati, nasititi, glad utoliti krvlju njihovom! Jer Gospod, Jahve nad Vojskama, ima žrtveno klanje u sjevernoj zemlji uz obalu Eufrata.
Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse; tsiku lolipsira, lolipsira adani ake. Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi, lidzaledzera ndi magazi. Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
11 Popni se na Gilead, balzama potraži, djevice, kćeri egipatska! Uzalud lijekovi mnogi: nema tebi ozdravljenja!
“Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala iwe namwali Igupto. Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira; palibe mankhwala okuchiritsa.
12 Narodi čuše za tvoju sramotu, vapaji tvoji napuniše zemlju. Jer se junak o junaka spotiče i obojica padaju.
Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako; kulira kwako kwadzaza dziko lapansi. Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana, onse awiri agwa pansi limodzi.”
13 Riječ koju Jahve uputi proroku Jeremiji kad Nabukodonozor, kralj babilonski, dođe da udari na zemlju egipatsku.
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:
14 Navijestite Egiptu, objavite u Migdolu, obznanite u Memfisu: “Svrstaj se! Spremi se! Jer mač već ždere sve oko tebe!
“Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli. Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi. Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza, chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’
15 Što? Zar Apis pobježe? Tvoj se Bik ne odrva?” Da, Jahve ga obori!
Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa? Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.
16 On učini te mnogi posrnuše, popadaše jedan na drugoga. I gle, govore: “Na noge! Vratimo se svom narodu, rodnoj grudi svojoj, pred mačem koljačkim!”
Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa. Aliyense akuwuza mnzake kuti, ‘Tiyeni tibwerere kwathu, ku dziko kumene tinabadwira, tithawe lupanga la adani athu.’
17 Faraonu, kralju egipatskom, ime nadjenite: “Graja što pravi čas promaši.”
Kumeneku iwo adzafuwula kuti, ‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti, Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’
18 “Tako, života mi moga” - govori Kralj, komu je ime Jahve nad Vojskama - “ono će doći kao Tabor posred gora, kao Karmel iznad mora.
“Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse, “wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena, ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.
19 Spremi izgnanički zavežljaj, udomljena kćeri egipatska, jer Memfis će biti u pustoš pretvoren, poharan i nenastanjen.
Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo inu anthu a ku Igupto, pakuti Mefisi adzasanduka chipululu ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.
20 Egipat bijaše lijepa junica, ali ide, ide na nju obad sa Sjevera.
“Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola, koma chimphanga chikubwera kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.
21 A i plaćenici egipatski što k'o gojna telad usred nje življahu, i oni se okrenuše, u bijeg udariše, ne mogu se odhrvati jer ih stiže Dan propasti, dođe vrijeme da se kazne.
Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye ali ngati ana angʼombe onenepa. Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi. Palibe amene wachirimika. Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira; ndiyo nthawi yowalanga.
22 Slušaj! K'o da zmija sikće, sa svom silom dolaze, sjekirama na nju navaljuju, baš k'o drvosječe.
Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa pamene adani abwera ndi zida zawo, abwera ndi nkhwangwa ngati anthu odula mitengo.
23 Posjeći će šumu - riječ je Jahvina - iako je neprohodna. Više ih je nego skakavaca, broja njima nema.
Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,” akutero Yehova, “ngakhale kuti ndi yowirira. Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe, moti sangatheke kuwerengeka.
24 Osramoćena je zemlja egipatska, predana je narodu Sjevera.”
Anthu a ku Igupto achita manyazi atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”
25 Govori Jahve nad Vojskama, kralj Izraelov: “Evo, kaznit ću Amona Tebskoga, faraona i Egipat, i sve njegove bogove, kraljeve, faraona i sve koji se u nj uzdaju.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira.
26 Predat ću ih u ruke onima što im rade o glavi, u ruke Nabukodonozora, kralja babilonskoga, i u ruke slugu njegovih. A poslije će Egipat biti opet naseljen, kao u stara vremena” - riječ je Jahvina.
Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.
27 “Ne boj se, Jakove, slugo moja, ne plaši se, Izraele! Jer, evo, spasit ću te izdaleka i potomstvo tvoje iz zemlje izgnanstva. Jakov će se opet smiriti, spokojno će živjet' i nitko ga neće plašiti.
“Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha; usataye mtima, iwe Israeli. Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali, ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere, ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.
28 Ne boj se, Jakove, slugo moja - riječ je Jahvina - jer ja sam s tobom. Zatrt ću narode među koje te prognah, a tebe neću sasvim uništiti: ali ću te kaznit' po pravici, ne smijem te pustit' nekažnjena.”
Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova. “Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu a ku mayiko kumene ndakupirikitsira, Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu. Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera; sindidzakulekerera osakulanga.”