< Jeremija 16 >
1 I dođe mi riječ Jahvina i reče:
Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
2 “Ne uzimaj sebi žene; i nemaj ni sinova ni kćeri na ovome mjestu.
“Usadzakwatire ndi kubereka ana aamuna kapena aakazi malo ano
3 Jer ovako govori Jahve o kćerima i sinovima koji će se roditi na ovome mjestu i o majkama koje će ih rađati i o očevima koji će ih imati u ovoj zemlji:
pakuti ana aamuna ndi ana aakazi obadwira mʼdziko muno, komanso amayi awo ndi abambo awo amene anabereka anawo mʼdziko muno,
4 Oni će umrijeti smrću prebolnom, nitko ih neće oplakivati, niti će ih sahraniti. Pretvorit će se u gnoj za oranice, izginut će od mača i gladi, a njihova će trupla biti hrana pticama nebeskim i zvijerima zemaljskim.”
adzafa ndi nthenda zoopsa. Sadzawalira maliro kapena kuyikidwa mʼmanda koma adzakhala ngati ndowe zotayikira pansi. Ena adzaphedwa ku nkhondo ndipo ena adzafa ndi njala. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo.”
5 Da, ovako govori Jahve: “Ne smiješ ući u kuću žalosti, ne idi naricati niti ih sažaljevati. Jer ja sam tom narodu uskratio mir svoj - riječ je Jahvina - ljubav i samilost.
Yehova akuti, “Usalowe mʼnyumba ya maliro; usapite kukalira maliro kapena kukapepesa, chifukwa Ine ndawachotsera madalitso anga, chikondi changa ndi chifundo changa.”
6 Pomrijet će veliko i malo u ovoj zemlji i nitko ih neće pokopati. Nitko neće naricati nad njima, niti će zbog njih praviti ureza, niti kose šišati.
Akuluakulu ndi angʼonoangʼono omwe adzafa mʼdziko muno. Sadzayikidwa mʼmanda kapena kuliridwa, ndipo palibe amene adzaonetse chisoni podzichekacheka kapena kumeta tsitsi lake chifukwa cha iwo.
7 Za onog u žalosti neće kruh lomiti, da ga utješe zbog pokojnika, nitiće mu tko pružiti pehar utjehe zbog smrti njegova oca ili majke njegove.
Palibe amene adzapereka chakudya kutonthoza amene akulira maliro, ngakhale kuti womwalirayo ndi abambo ake kapena amayi ake.
8 Ne ulazi u kuću slavlja da s njima sjediš i gostiš se.”
“Ndipo usalowe mʼnyumba mmene muli madyerero, nʼkukhala pansi ndi kudya ndi kumwa nawo.
9 Jer ovako govori Jahve nad Vojskama, Bog Izraelov: “Evo, učinit ću da s ovog mjesta i pred vašim očima i u ovim danima iščeznu poklici radosti i veselja i glasovi zaručnika i zaručnice.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Pa nthawi yanu, inu mukuona ndidzathetsa mawu achimwemwe ndi achisangalalo ndiponso mawu a mkwati ndi mkwatibwi pa malo ano.’
10 A kad objaviš tom narodu sve ove riječi, pa te upitaju: 'Zašto nam Jahve zaprijeti svom ovom golemom nesrećom; u čemu je zločinstvo naše i u čemu su grijesi naši što ih počinismo protiv Jahve, Boga našega?' -
“Ukawawuza anthu awa zinthu zonsezi akakufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wanena kuti tsoka lalikulu lotere lidzatigwere? Kodi talakwa chiyani? Kodi tamuchimwira tchimo lotani Yehova Mulungu wathu?’
11 onda im odgovori: 'U tom što me ostaviše oci vaši - riječ je Jahvina - i trčaše za tuđim bogovima da im služe i da im se klanjaju, a mene ostaviše i Zakona se moga ne držaše.
Pamenepo ukawawuze kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti makolo anu anandisiya Ine,’ akutero Yehova, ‘ndi kutsatira milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Iwo anandisiya Ine ndipo sanasunge lamulo langa.
12 A vi još gore učiniste nego oci vaši, jer evo, svaki se povodi za okorjelošću zloga srca svoga, a mene ne sluša.
Komanso inu munachimwa kwambiri kupambana makolo anu. Aliyense wa inu akutsatira zoyipa ndi mtima wake wokanikawo mʼmalo mondimvera Ine.
13 Zato ću vas istjerati iz ove zemlje u zemlju koja vam je neznana, kao što bijaše i ocima vašim. Ondje ćete služiti tuđim bogovima danju i noću: jer neću vam se više smilovati!'”
Choncho Ine ndidzakubalalitsani mʼdziko muno ndi kukulowetsani mʼdziko limene inu ndi makolo anu simunalidziwe. Kumeneko mukatumikira milungu ina usana ndi usiku, ndipo sadzakuchitirani chifundo.’”
14 “Zato, evo, dolaze dani - riječ je Jahvina - kad se više neće govoriti: 'Živoga mi Jahve koji sinove Izraelove izvede iz Egipta',
Yehova akuti, “Komabe masiku akubwera pamene anthu polumbira sadzatinso, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto,’
15 nego: 'Živoga mi Jahve koji sinove Izraelove izvede iz zemlje sjeverne i iz svih zemalja kamo ih bijaše prognao.' Vratit ću ih u zemlju njihovu koju dadoh ocima njihovim.
koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku dziko lakumpoto, ndi ku mayiko onse kumene anawabalalitsirako.’ Pakuti ndidzawabwezera ku dziko limene ndinalipereka kwa makolo awo.”
16 Evo, poslat ću mnoga ribara - riječ je Jahvina - koji će ih uloviti. A zatim ću dovesti mnoge lovce koji će ih goniti sa svih gora, i sa svih brežuljaka, i iz svih pećinskih rasjeklina.
Yehova akuti, “Koma tsopano ndidzayitana adani okhala ngati asodzi ambiri, ndipo adzawagwira ngati nsomba. Izi zitatha adani enanso okhala ngati alenje ambiri, adzawasaka pa phiri lililonse, pa chitunda chilichonse ndiponso mʼmapanga onse a mʼmatanthwe.
17 Jer moje oči prate sve njihove putove: neće mi izmaći, niti se bezakonje njihovo može sakriti od očiju mojih.
Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa.
18 Dvostruko ću naplatiti njihovo bezakonje i grijehe njihove, jer su truplima svojih grozota oskvrnuli moju zemlju i moju baštinu ispunili gnusobama.”
Ndidzawalanga mowirikiza chifukwa cha kuyipa kwawo ndi tchimo lawo. Ndidzatero chifukwa ayipitsa dziko langa ndi mafano awo amene ali ngati mitembo, ndiponso adzaza cholowa changa ndi mafano awo onyansa.”
19 Jahve, snago moja i moja utvrdo, utočište moje u danima nevolje! K tebi će doći narodi s krajeva zemlje. I govorit će: Samu nam laž oci namriješe, Ništavost i Nemoć.
Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga ndi linga langa, pothawirapo panga nthawi ya masautso, anthu a mitundu yonse adzabwera kwa Inu kuchokera ku mathero onse a dziko lapansi ndipo adzanena kuti, “Makolo anthu anali ndi milungu yonama, anali ndi mafano achabechabe amene sanawathandize.
20 TÓa stvara li čovjek sam sebi bogove, to nikako nisu bogovi.
Kodi anthu nʼkudzipangira milungu? Atati atero ndiye kuti imeneyo ikhala milungu yachabechabe.”
21 Učinit ću, evo, da osjete, da ovaj put zaista oćute moju ruku i snagu moju, i znat će da mi je ime Jahve.
“Choncho Ine ndidzawaphunzitsa, kokha kano kuti adziwe za mphamvu yanga ndi za nyonga zanga. Pamenepo adzadziwa kuti dzina langa ndi Yehova.