< Izaija 59 >
1 Ne, nije ruka Jahvina prekratka da spasi, niti mu je uho otvrdlo da ne bi čuo,
Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa, kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
2 nego su opačine vaše jaz otvorile između vas i Boga vašega. Vaši su grijesi lice njegovo zastrli, i on vas više ne sluša.
Koma zoyipa zanu zakulekanitsani ndi Mulungu wanu; ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu, kotero Iye sadzamva.
3 Jer ruke su vaše u krvi ogrezle, a vaši prsti u zločinima. Usne vam izgovaraju laž, a jezik podlost mrmlja.
Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi. Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu. Pakamwa panu payankhula zabodza, ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
4 Nitko s pravom tužbu ne podiže, niti koga sude po istini. U ništavilo se uzdaju, laž kazuju, začinju zloću, a rađaju bezakonje.
Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama, palibe amene akupita ku mlandu moona mtima. Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza; amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
5 Legu jaja gujina, tkaju mrežu paukovu; pojede li tko njihovo jaje, umire, razbije li ga, iz njega ljutica izlazi.
Iwo amayikira mazira a mamba ndipo amaluka ukonde wakangawude. Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa, ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
6 Njihovim tkanjem nemoguće se odjenuti, ne možeš se pokriti njihovom rukotvorinom. Rukotvorine su njihove djela zločinačka, rukama svojim čine nasilje.
Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala; ndipo chimene apangacho sangachifunde. Ntchito zawo ndi zoyipa, ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
7 Noge njihove u zlo hitaju i brze su da krv nevinu proliju. Misli su im misli zločinačke, pustoš i propast na njinim su putima.
Amathamangira kukachita zoyipa; sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo awo ndi maganizo oyipa; kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
8 Put mira oni ne poznaju, na stazama njihovim nema pravice. Iskrivili su svoje putove, tko njima kreće mira ne poznaje.
Iwo sadziwa kuchita za mtendere; zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo. Njira zawo zonse nʼzokhotakhota; aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
9 Stog' se pravo od nas udaljilo, zato pravda ne dopire do nas. Nadasmo se svjetlosti, a ono tama; i vidjelu, a ono u tmini hodimo.
Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira; ndipo chipulumutso sichitifikira. Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha; tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
10 Pipamo kao slijepci duž zida, tapkamo kao bez očiju. Spotičemo se u podne k'o u sumraku, sasvim zdravi, kao da smo mrtvi.
Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona, kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso. Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku; timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
11 Svi mumljamo kao medvjedi i gučemo tužno kao golubovi. Očekivasmo Sud, a njega nema, i spasenje - od nas je daleko.
Tonse timabangula ngati zimbalangondo: Timalira modandaula ngati nkhunda. Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza. Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
12 Jer mnogo je naših opačina pred tobom i grijesi naši protiv nas svjedoče. Doista, prijestupi su naši pred nama, mi znademo svoju krivicu;
Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu, ndipo machimo athu akutsutsana nafe. Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse ndipo tikuvomereza machimo athu:
13 pobunili smo se i zanijekali Jahvu, odmetnuli se od Boga svojega, govorili podlo, odmetnički, mrmljali u srcu riječi lažljive.
Tawukira ndi kumukana Yehova. Tafulatira Mulungu wathu, pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova, ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
14 Tako je potisnuto pravo, i pravda mora stajati daleko. Jer na trgu posrnu istina i poštenju nema više pristupa.
Motero kuweruza kolungama kwalekeka ndipo choonadi chili kutali ndi ife; kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu, ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
15 Vjernosti je ponestalo, a tko izbjegava zlo, bude opljačkan. Jahve vidje, i ne bi mu milo što nema pravice.
Choonadi sichikupezeka kumeneko, ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto. Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa kuti panalibe chiweruzo cholungama.
16 Vidje da nema čovjeka, začudi se što nema posrednika. Tad mu pomože njegova mišica i njegova ga pravda poduprije.
Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe, Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera; Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza, ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
17 Pravednost je obukao k'o oklop, stavio na glavu kacigu spasenja. Osvetom se odjenuo k'o haljom, ogrnu se revnošću kao plaštem.
Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa, ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso; anavala kulipsira ngati chovala ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
18 Vratit će svakome po njegovim djelima: gnjev svojim protivnicima, odmazdu dušmanima.
Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake molingana ndi zimene anachita, adzaonetsa ukali kwa adani ake ndi kubwezera chilango odana naye. Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
19 Sa zapada vidjet će ime Jahvino i Slavu njegovu s istoka sunčanog. Jer doći će kao uska rijeka koju goni dah Jahvin.
Choncho akadzabwera ngati madzi oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho. Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
20 Ali doći će Otkupitelj Sionu, i onima od sinova Jakovljevih koji se obrate od svog otpadništva, riječ je Jahvina.
“Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,” akutero Yehova.
21 “A ovo je moj Savez s njima,” govori Jahve. “Duh moj koji je na tebi i riječi moje koje stavih u tvoja usta neće izići iz usta tvojih ni usta tvojega potomstva, ni iz usta potomstva tvojih potomaka, od sada pa dovijeka,” veli Jahve.
Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,” akutero Yehova.