< Jevrejima 6 >

1 Stoga mimoiđimo početnički nauk o Kristu i uzdignimo se k savršenome ne postavljajući iznovice temelja: obraćenje od mrtvih djela i vjera u Boga,
Tsono tiyeni tisangoyima pa maphunziro oyambirira enieni a Khristu koma tipitirire kuti mukule msinkhu. Tisaphunzitsenso zinthu zomwe zili ngati maziko, monga za kutembenuka mtima kusiya ntchito zosapindulitsa pa moyo wosatha, za kukhulupirira Mulungu,
2 naučavanje o krštenjima i polaganje ruku, uskrsnuće mrtvih i vječni sud. (aiōnios g166)
za maubatizo, za kusanjika manja, za kuuka kwa akufa ndi za chiweruzo chotsiriza. (aiōnios g166)
3 To ćemo pak učiniti, dakako, ako Bog da.
Ndipo Mulungu akalola, tidzaterodi.
4 Zaista, onima koji su jednom prosvijetljeni, i okusili dar nebeski, i postali dionici Duha Svetoga,
Nʼkosatheka kuwabwezanso anthu amene nthawi ina anawunikiridwa. Iwowa analawapo mphatso yochokera kumwamba, nʼkulandira nawo Mzimu Woyera.
5 i okusili Lijepu riječ Božju i snage budućega svijeta, (aiōn g165)
Analawa kukoma kwa mawu a Mulungu ndi mphamvu za nthawi ikubwera. (aiōn g165)
6 pa otpali, nemoguće je opet se obnoviti na obraćenje kad oni sami ponovno razapinju Sina Božjega i ruglu ga izvrgavaju.
Popeza anabwerera mʼmbuyo, nʼkosatheka kuti atembenukenso mtima chifukwa akupachikanso Mwana wa Mulungu ndi kumunyozetsa poyera.
7 Jer zemlja koja se napije kiše što na nju često pada i rađa raslinjem korisnim onima za koje se i obrađuje, prima blagoslov od Boga;
Nthaka yolandira mvula kawirikawiri nʼkubala mbewu zopindulitsa oyilima, Mulungu amayidalitsa.
8 ona pak koja donosi trnje i drač, odbačena je, blizu prokletstvu a svršetak joj je: “U oganj!”
Koma nthaka yobereka minga ndi nthula ndi yopanda phindu ndipo ili pafupi kutembereredwa. Matsiriziro ake idzatenthedwa mʼmoto.
9 A uvjereni smo, ljubljeni, sve ako tako i govorimo, da je s vama dobro i da ste na putu spasenja.
Okondedwa anga, ngakhale tikuyankhula zimenezi, ife tikudziwa kuti muli nazo zinthu zabwino zomwe zimabwera pamodzi ndi chipulumutso.
10 Ta Bog nije nepravedan da bi zaboravio vaše djelo i ljubav što je iskazaste njegovu imenu posluživši i poslužujući svetima.
Mulungu ndi wolungama, sangayiwale ntchito zanu ndi chikondi chanu chimene munamuonetsa pothandiza anthu ake monga mmene mukuchitirabe tsopano.
11 Želimo ipak da svatko od vas sve do svršetka pokazuje tu istu gorljivost za ispunjenje nade
Ife tikufuna kuti aliyense wa inu aonetse changu chomwechi mpaka kumapeto, kuti zichitikedi zomwe mukuyembekezera.
12 te ne omlitavite, nego budete nasljedovatelji onih koji po vjeri i strpljivosti baštine obećano.
Ife sitikufuna kuti inu mukhale aulesi, koma mutsatire anthu amene, pokhulupirira ndi kupirira, akulandira zimene zinalonjezedwa.
13 Doista, kad je Bog Abrahamu davao obećanje, jer se nije imao kime većim zakleti, zakle se samim sobom:
Pamene Mulungu ankamulonjeza Abrahamu, popeza panalibe wamkulu womuposa, amene akanamutchula ndikulumbira mwa Iye, analumbira mwa Iye yekha kuti,
14 Uistinu, blagosloviti, blagoslovit ću te i umnožiti, umnožit ću te.
“Ine ndidzakudalitsa ndithu, ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
15 I tako Abraham, strpljiv, postiže obećano.
Ndipo Abrahamu atayembekezera mofatsa, analandira zimene anamulonjezazo.
16 Ljudi se doista kunu onim tko je veći i zakletva im je, kao potkrepa, kraj svake raspre.
Anthu amalumbira mʼdzina la wina amene akuwaposa, ndipo lumbiro lotere limatsimikizira zomwe zayankhulidwa ndi kuthetsa mikangano yonse.
17 Tako i Bog: htio je baštinicima obećanja obilatije pokazati nepromjenljivost svoje odluke pa zato zajamči zakletvom
Momwemonso Mulungu pofuna kutsimikizira anthu amene adzalandire lonjezo, kuti Iye sangasinthe maganizo, anatsimikiza lonjezo lakelo ndi lumbiro.
18 da bismo po dva nepromjenljiva čina - u kojima je nemoguće da bi Bog prevario - mi pribjeglice imali snažno ohrabrenje da se držimo ponuđene nade.
Mulungu anachita zinthu ziwiri, lonjezo ndi lumbiro, zimene sizingathe kusintha ndipo Mulungu sangathe kunama. Choncho Mulungu akutilimbikitsa mtima ife amene tinathawira kwa Iye kuti tichigwiritsitse chiyembekezo chimene tinalandira.
19 Ona nam je kao pouzdano i čvrsto sidro duše što ulazi u unutrašnjost iza zavjese,
Chiyembekezo chimenechi tili nacho ngati nangula wa moyo wathu. Nʼchokhazikika ndi chosagwedezeka ndipo chimalowa mʼkatikati mwa malo opatulika, kuseri kwa chinsalu chotchinga.
20 kamo je kao preteča za nas ušao Isus postavši zauvijek Veliki svećenik po redu Melkisedekovu. (aiōn g165)
Yesu anatitsogolera kupita kumeneko, nalowako mʼmalo mwathu. Iye anasanduka Mkulu wa ansembe onse wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki. (aiōn g165)

< Jevrejima 6 >