< Ezra 1 >
1 Prve godine perzijskoga kralja Kira, da bi se ispunila riječ Jahvina objavljena na Jeremijina usta, nadahnu Jahve perzijskoga kralja Kira te on objavi po svemu svojem kraljevstvu, usmeno i pismeno:
Mʼchaka choyamba cha ufumu wa Koresi mfumu ya Perisiya, pofuna kukwaniritsa zimene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anayika maganizo mu mtima mwa Koresi mfumu ya Perisiya kuti alengeze mʼdziko lake lonse ndi mawu apakamwa ngakhalenso ochita kulemba.
2 “Ovako veli perzijski kralj Kir: 'Sva zemaljska kraljevstva dade mi Jahve, Bog nebeski. On mi naloži da mu sagradim Dom u Jeruzalemu, u Judeji.
Iye anati, “Koresi mfumu ya Perisiya ikunena kuti, “‘Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa maufumu onse a dziko lapansi, ndipo wandipatsa udindo woti ndimumangire Nyumba ku Yerusalemu mʼdziko la Yuda.
3 Tko je god među vama od svega njegova naroda, Bog njegov bio s njim! Neka ide u Jeruzalem u Judeji i neka gradi Dom Jahvi, Bogu Izraelovu, Bogu koji stoluje u Jeruzalemu.
Aliyense wa inu amene ali wa Yehova, Mulungu wakeyo akhale naye. Tsono aliyense wa inu apite ku Yerusalemu, mʼdziko la Yuda kuti akamange Nyumba ya Yehova, Mulungu wa Israeli. Iyeyu ndi Mulungu amene ali mu Yerusalemu.
4 I gdje god se još zadržao ostatak toga naroda, neka ga stanovništvo mjesta u kojima boravi podupre srebrom i zlatom, imanjem i stokom i dragovoljnim prinosima za Dom Božji u Jeruzalemu.'”
Ndipo kumalo kulikonse kumene otsalawo akukhala, athandizidwe ndi eni dzikolo powapatsa siliva, golide, katundu ndi ziweto ndi zopereka za ufulu zoti akapereke ku Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.’”
5 Tada ustadoše glavari obitelji Jude i Benjamina, svećenici i leviti, i svi kojima je Bog potaknuo duh i krenuše graditi Dom Jahvin u Jeruzalemu.
Choncho atsogoleri a mabanja afuko la Yuda ndi la Benjamini komanso ansembe ndi Alevi, aliyense amene Mulungu anawutsa mtima wake, anayamba kukonzeka kupita kukamanga Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.
6 I svi su im susjedi pomagali: srebrom, zlatom, darovima u naravi, stokom, dragocjenostima mnogim, osim svega što su dragovoljno prilagali.
Onse oyandikana nawo anawathandiza powapatsa ziwiya za siliva ndi zagolide, kuphatikizaponso katundu ndi ziweto, ndiponso mphatso zamtengo wapatali, kuwonjezera pa zopereka zaufulu zija.
7 Kralj Kir iznese posuđe Jahvina Doma koje Nabukodonozor bijaše odnio iz Jeruzalema i stavio u hram svoga boga.
Nayenso mfumu Koresi anatulutsa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara anazitenga kuzichotsa ku Yerusalemu ndi kuziyika mʼnyumba ya milungu yake.
8 Kir, kralj perzijski, uruči ga Mitredatu, rizničaru, koji ga izbroji judejskom knezu Šešbasaru.
Koresi, mfumu ya ku Perisiya inatulutsa ziwiyazi ndi kuzipereka kwa Miteridati, msungichuma amene anaziwerenga pamaso pa Sesibazara nduna yayikulu ya dziko la Yuda.
9 Evo njegova popisa. Zlatnih zdjela: trideset; srebrnih zdjela: tisuću i dvadeset devet;
Chiwerengerochi chinali motere: Mabeseni agolide 30 mabeseni asiliva 1,000 a zopereka 29
10 zlatnih čaša: trideset; srebrnih čaša: četiri stotine i deset; ostalog posuđa: tisuću.
timiphika tagolide 230 timiphika tasiliva 410 ziwiya zina 1,000.
11 Svega zlatnog i srebrnog posuđa: pet tisuća i četiri stotine. Sve je to odnio Šešbasar kada se sužnji vraćahu iz Babilona u Jeruzalem.
Ziwiya zonse zagolide ndi siliva pamodzi zinalipo 5,400. Zonsezi ndi zimene Sezi-Bazara anabwera nazo pamene otengedwa ukapolo aja ankabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku Babuloni.