< Ezekiel 5 >

1 A ti, sine čovječji, uzmi mač naoštren, uzmi ga kao britvu brijačku i obrij glavu i bradu. Zatim uzmi mjerice i porazdijeli.
Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
2 Trećinu spali posred grada ognjem kad se navrše dani tvoje opsade; trećinu uzmi i sasijeci mačem oko grada; trećinu baci u vjetar - i svoj ću mač trgnuti na njih.
Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
3 Uzmi malo i zaveži u skute haljine.
Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
4 Od toga opet nešto uzmi, baci u vatru i spali: odatle će se razgorjeti vatra svemu domu Izraelovu!”
Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
5 Ovako govori Jahve Gospod: “Ovo je Jeruzalem! Postavih ga u središte naroda, okružih ga zemljama!
Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
6 Ali se on odupro mojim naredbama većma nego pogani, zakonima mojim većma nego zemlje koje ga okružuju.”
Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
7 Stoga ovako govori Jahve Gospod: “Buntovniji ste od naroda koji vas okružuju, ne hodite po mojim zakonima i ne vršite ni mojih naredaba ni naredaba okolnih naroda.”
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
8 Zato ovako govori Jahve Gospod: “Evo i mene protiv tebe! Izvršit ću sud svoj nad tobom na oči svih naroda.
“Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
9 Zbog tvojih gadosti učinit ću s tobom što još ne učinih nikada nit ću ikad učiniti:
Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
10 posred tebe očevi će jesti sinove, a sinovi očeve; izvršit ću sud svoj nad tobom i sav ostatak tvoj predati svim vjetrovima!
Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
11 Života mi moga! - riječ je Jahve Gospoda - svakojakim grozotama i gadostima ti uistinu oskvrnu moje Svetište. I ja ću sada brijati i oko se moje neće sažaliti i neću se smilovati:
Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
12 trećina će tvojih žitelja posred tebe od kuge skončati i od gladi umrijeti; trećina će oko tebe od mača pasti; trećinu ću predati vjetrovima - i mač ću svoj trgnuti na njih!
Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
13 Tako ću iskaliti gnjev svoj i smirit će se jarost moja kad im se osvetim. I kad iskalim jarost svoju nad njima, spoznat će da sam to ja, Jahve, u ljubomori svojoj bio rekao.
“Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
14 Opustošit ću te, izvrgnut ću te ruglu naroda koji te okružuju, na oči svim prolaznicima.
“Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
15 Da, bit ćeš na ruglo i sramotu, opomena i užas okolnim narodima kad izvršim protiv tebe sve svoje sudove kažnjavajući gnjevno, jarosno. Ja, Jahve, rekoh!
Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
16 I kad na vas pustim ljute strijele gladi što zatiru, koje ću pustiti na vas da vas uništim i glađu zatrem - uništit ću vam i posljednju pričuvu kruha.
Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
17 A povrh gladi pustit ću na vas i divlje zvijeri koje će ti djecu rastrgati; kuga će te i krv preplaviti: pod mač ću te svoj okrenuti. Ja, Jahve, rekoh!”
Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”

< Ezekiel 5 >