< Izlazak 32 >
1 A narod, videći gdje Mojsije dugo ne silazi s brda, okupi se oko Arona pa mu rekne: “Ustaj! Napravi nam boga, pa neka on pred nama ide! Ne znamo što se dogodi s tim čovjekom Mojsijem koji nas izvede iz zemlje egipatske.”
Anthu ataona kuti Mose akuchedwa kutsika mʼphiri, anasonkhana kwa Aaroni ndipo anati, “Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.”
2 “Poskidajte zlatne naušnice što vise o ušima vaših žena, vaših sinova i vaših kćeri”, odgovori im Aron, “pa ih meni donesite.”
Aaroni anawayankha kuti, “Vulani ndolo zagolide zimene avala akazi anu, ana anu aamuna ndi aakazi ndipo muzibweretse kwa ine.”
3 Sav svijet skine zlatne naušnice što ih je o ušima imao i donese Aronu.
Kotero anthu onse anavula ndolo zagolide ndi kubwera nazo kwa Aaroni.
4 Primivši zlato iz njihovih ruku, rastopi kovinu u kalupu i načini saliveno tele. A oni poviču: “Ovo je tvoj bog, Izraele, koji te izveo iz zemlje egipatske.”
Choncho Aaroni analandira golideyo ndipo anamuwumba ndi chikombole ndi kupanga fano la mwana wangʼombe. Kenaka anthu aja anati, “Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.”
5 Vidjevši to Aron, sagradi pred njim žrtvenik a onda najavi: “Sutra neka se priredi svečanost u čast Jahvi!”
Aaroni ataona izi, anamanga guwa lansembe patsogolo pa mwana wangʼombeyo ndipo analengeza kuti, “Mawa kudzakhala chikondwerero cha Yehova.”
6 Sutradan rano ustanu i prinesu žrtve paljenice i donesu žrtve pričesnice. Onda svijet posjeda da jede i pije. Poslije toga ustade da se zabavlja.
Kotero tsiku linalo anthu anadzuka mmamawa ndithu ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Atatha kupereka nsembezo, anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.
7 “Požuri se dolje!” - progovori Jahve Mojsiju. “Narod tvoj, koji si izveo iz zemlje egipatske, pošao je naopako.
Pamenepo Yehova anati kwa Mose, “Tsika msanga, chifukwa anthu ako amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto aja adziyipitsa kwambiri.
8 Brzo su zašli s puta koji sam im odredio. Napravili su sebi tele od rastopljene kovine, preda nj pali ničice i žrtve mu prinijeli uz poklike: 'Ovo je tvoj bog, Izraele, koji te izveo iz zemlje egipatske!'
Iwo apatuka mwamsanga kuleka kutsatira zimene ndinawalamula. Ndiye adzipangira fano la mwana wangʼombe. Aligwadira ndi kuliperekera nsembe nʼkumati, ‘Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.’”
9 Dobro vidim”, reče dalje Jahve Mojsiju, “da je ovaj narod tvrde šije.
Yehova anati kwa Mose, “Ine ndikuwadziwa anthu amenewa. Iwowa ndi ankhutukumve.
10 Pusti sada neka se moj gnjev na njih raspali da ih istrijebim. Onda ću od tebe razviti velik narod.”
Chifukwa chake undileke kuti mkwiyo wanga uyake pa iwo ndi kuwawononga. Ndipo Ine ndidzakusandutsa kuti ukhale mtundu waukulu.”
11 Mojsije pak zapomagao pred Jahvom, Bogom svojim, i govorio: “O Jahve! Čemu da gnjevom plamtiš na svoj narod koji si izbavio iz zemlje egipatske silom velikom i rukom jakom!
Koma Mose anapempha chifundo cha Mulungu wake ndipo anati, “Chonde Yehova, chifukwa chiyani mwakwiyira anthu awa amene munawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
12 Zašto bi Egipćani morali reći: 'U zloj ih je namjeri i odveo, tako da ih smakne u brdinama i izbriše s lica zemlje!' Smiri svoj gnjev i ljutinu; odustani od zla svome narodu!
Kodi mukufuna kuti Aigupto azinena kuti, ‘Munali ndi cholinga choyipa chofuna kuwaphera ku mapiri kuno ndi kuwawonongeratu pa dziko lapansi pamene munkawatulutsa ku Igupto kuja?’ Ayi, chonde mkwiyo wanu woyaka ngati motowu ubwezeni ndipo sinthani maganizo ofunira zoyipa anthu anu.
13 Sjeti se Abrahama, Izaka i Izraela, slugu svojih, kojima si se samim sobom zakleo i obećao im: 'Razmnožit ću vaše potomstvo kao zvijezde na nebu i svu zemlju ovu što sam obećao dat ću vašem potomstvu i ona će zavazda biti njihova baština.'”
Kumbukirani atumiki anu, Abrahamu, Isake, Israeli ndi zija munawalonjeza polumbira pa dzina lanu kuti, ‘Ine ndidzachulukitsa zidzukulu zanu ndipo zidzakhala zambiri ngati nyenyezi zakumwamba. Zidzukulu zanuzo ndidzazipatsa dziko lonseli limene ndinalonjeza. Dziko limeneli lidzakhala lawo nthawi zonse.’”
14 I Jahve odustane da na svoj narod svali nesreću kojom mu bijaše zaprijetio.
Choncho Yehova analeka ndipo sanawachitire choyipa anthu ake monga anaopsezera.
15 Mojsije se okrene i siđe s brda. U rukama su mu bile dvije ploče Svjedočanstva, ploče ispisane na objema plohama; ispisane i s jedne i s druge strane.
Mose anatembenuka ndi kutsika phiri miyala iwiri ya pangano ili mʼmanja mwake. Miyalayi inalembedwa mbali zonse, kutsogolo ndi kumbuyo komwe.
16 Ploče su bile djelo Božje; pismo je bilo pismo Božje u pločama urezano.
Miyalayi anayikonza ndi Mulungu. Malembawo analemba ndi Mulungu mozokota pa miyalapo.
17 A Jošua ču viku naroda koji je bučio pa reče Mojsiju: “Bojna vika u taboru!”
Pamene Yoswa anamva phokoso la anthu anati kwa Mose, “Ku msasa kuli phokoso la nkhondo.”
18 Mojsije mu odgovori: “Niti viču pobjednici, niti tuže pobijeđeni: tu ja samo pjesmu čujem.”
Mose anayankha kuti, “Phokoso limeneli sindikulimva ngati phokoso la opambana nkhondo, kapena kulira kwa ongonjetsedwa pa nkhondo. Koma ndikulimva ngati phokoso la anthu amene akuyimba.”
19 Čim se približi taboru te opazi tele i kako igraju, razgnjevi se Mojsije. Baci iz ruku ploče i razbije ih na podnožju brda.
Mose atayandikira msasa ndi kuona mwana wangʼombe ndiponso kuvina, anakwiya kwambiri ndipo anaponya pansi miyala imene inali mʼmanja mwake, ndi kuyiphwanya pa tsinde la phiri.
20 Pograbi tele koje bijahu napravili, spali ga ognjem i u prah satre. Onda prah razbaca po vodi i natjera Izraelce da je piju.
Ndipo iye anatenga mwana wangʼombe amene anthu anapanga uja ndi kumuwotcha pa moto ndi kumuperapera ndikukhala ngati fumbi. Kenaka anawaza fumbilo mʼmadzi ndi kuwamwetsa Aisraeli madziwo.
21 “Što ti je ovaj puk učinio”, reče Mojsije Aronu, “da si tako velik grijeh na nj svalio?”
Tsono Mose anafunsa Aaroni kuti, “Kodi anthu awa anakuchita chiyani kuti uwachimwitse koopsa chotere?”
22 “Neka se moj gospodar srdžbom ne raspaljuje”, odgovori Aron. “Sam dobro znaš kako je ovaj narod na zlo sklon.
Aaroni anayankha kuti, “Musakwiye mbuye wanga. Inu mukudziwa kuti anthu awa ndi ovuta.
23 Rekoše mi: 'Napravi nam boga pa neka pred nama ide! Ne znamo što se dogodi s tim čovjekom Mojsijem koji nas izbavi iz zemlje egipatske.'
Iwo anati kwa ine, ‘Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa ife mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.’
24 Na to im ja rekoh: 'Tko ima zlata, neka ga skine!' Tako mi ga dadoše, a ja ga bacih u vatru te izađe ovo tele.”
Choncho ine ndinawawuza kuti, ‘Aliyense amene ali ndi zokometsera zagolide azivule.’ Choncho iwo anandipatsa golide, ndipo ndinamuponya pa moto ndi kupanga fano la mwana wangʼombeyu.”
25 Kad je Mojsije vidio kako je narod postao razuzdan - tÓa Aron ih je pustio da padnu u idolopoklonstvo među svojim neprijateljima -
Mose anaona kuti anthuwo anali osokonezekadi chifukwa Aaroni anawalekerera mpaka kusanduka anthu osekedwa pakati pa adani awo.
26 stade na taborskim vratima i povika: “Tko je za Jahvu, k meni!” Svi se sinovi Levijevi okupe oko njega.
Choncho iye anayima pa chipata cholowera mu msasa ndipo anati, “Aliyense amene ali mbali ya Yehova abwere kwa ine.” Ndipo Alevi onse anapita mbali yake.
27 On im reče: “Ovako govori Jahve, Bog Izraela: 'Neka svatko pripaše mač o bedro i pođe taborom od vrata do vrata pa neka ubije tko svoga brata, tko svoga prijatelja, tko svoga susjeda.'”
Ndipo iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena, ‘Pitani ku misasa konse, mulowe ku zipata zonse ndipo aliyense akaphe mʼbale wake, kapena mnzake kapena mnansi wake.’”
28 Sinovi Levijevi izvršiše Mojsijev nalog, i toga dana pade naroda oko tri tisuće ljudi.
Alevi anachita zomwe Mose analamula, ndipo tsiku limenelo panafa anthu pafupifupi 3,000.
29 “Danas ste se posvetili Jahvi za službu”, reče Mojsije, “tko uz cijenu svoga sina, tko uz cijenu svoga brata, tako da vam danas daje blagoslov.”
Kenaka Mose anati, “Lero mwadzipatula nokha kukhala ansembe otumikira Yehova. Mwachita izi popeza aliyense wa inu wapha mwana wake kapena mʼbale wake. Tsono lero Yehova wakudalitsani.”
30 Sutradan reče Mojsije narodu: “Težak ste grijeh počinili. Ipak ću se Jahvi popeti. Možda za vaš grijeh oproštenje pribavim.”
Mmawa mwake Mose anati kwa anthu onse, “Inu mwachita tchimo lalikulu. Koma tsopano ine ndipita ku phiri kwa Yehova mwina ndikatha kukupepeserani chifukwa cha tchimo lanu.”
31 Mojsije se vrati Jahvi pa reče: “Jao! Narod onaj težak je grijeh počinio napravivši sebi boga od zlata.
Kotero Mose anabwereranso kwa Yehova ndipo anati, “Aa! Anthu awa achita tchimo lalikulu! Iwo adzipangira milungu yagolide.
32 Ipak im taj grijeh oprosti... Ako nećeš, onda i mene izbriši iz svoje knjige koju si napisao.”
Koma tsopano, chonde akhululukireni tchimo lawo. Ngati simutero, ndiye mundifute ine mʼbuku limene mwalemba.”
33 Nato Jahve odgovori Mojsiju: “Onoga koji je protiv mene sagriješio izbrisat ću iz svoje knjige.
Yehova anamuyankha Mose kuti, “Ndidzafuta mʼbuku aliyense amene wandichimwira.
34 Nego, idi sad! Povedi narod kamo sam ti rekao. Anđeo će moj pred tobom ići. Ali u dan kad ih pohodim, zbog njihova ću ih grijeha kazniti.”
Tsopano pita ukawatsogolere anthu kumalo kumene ine ndinanena, ndipo mngelo wanga adzakutsogolerani. Komabe, nthawi yanga ikadzafika kuti ndiwalange, ndidzawalanga chifukwa cha tchimo lawo.”
35 Udari Jahve po narodu pomorom zbog teleta što im ga Aron načini.
Ndipo Yehova anawakantha anthuwo ndi mliri chifukwa anawumiriza Aaroni kuti awapangire fano la mwana wangʼombe.