< Izlazak 31 >
Ndipo Yehova anati kwa Mose,
2 “Pozvao sam, gledaj, po imenu Besalela, sina Urijeva, od koljena Hurova iz plemena Judina.
“Taona, ndasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda.
3 Napunio sam ga duhom Božjim koji mu je dao umješnost, razumijevanje i sposobnost za svakovrsne poslove:
Ndipo ndamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
4 da zamišlja nacrte za radove od zlata, srebra i tuča;
Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
5 za rezanje dragulja, za umetanje; za rezbarije u drvu i poslove svakakve.
kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
6 Dodao sam još Oholiaba, sina Ahisamakova iz Danova plemena; vještinom sam obdario sve sposobne ljude da mognu napraviti sve što sam ti naredio:
Ndasankhanso Oholiabu mwana wa Ahisamaki wa fuko la Dani. Ndiponso ndapereka nzeru kwa anthu aluso motero adzagwira ntchito zonse zimene ndakulamulira kuti zichitike monga izi:
7 Šator sastanka, Kovčeg Svjedočanstva, povrh njega Pomirilište i sav namještaj Šatora;
Kupanga tenti ya msonkhano, bokosi laumboni pamodzi ndi chophimbira chake, ndiponso zonse za mu tenti,
8 stol i sav njegov pribor, čisti svijećnjak sa svim njegovim priborom;
tebulo ndi zida zake, choyikapo nyale cha golide wabwino kwambiri ndi ziwiya zake zonse, guwa lofukizirapo lubani,
9 kadioni žrtvenik, žrtvenik za žrtve paljenice i njegov pribor, onda umivaonik i njegovo podnožje;
guwa lansembe yopsereza ndi ziwiya zake zonse, beseni ndi nsichi yake,
10 odijela za službu, posvećena odijela za svećenika Arona i odijela za njegove sinove, za njihovu svećeničku službu;
ndiponso zovala zonse zolukidwa, zovala zopatulika za Aaroni wansembe pamodzi ndi za ana ake, zovala pamene akutumikira monga ansembe,
11 pa ulje za pomazanje i miomirisni tamjan za Svetište. Sve neka načine kako sam ti naredio.”
ndiponso mafuta odzozera ndi lubani wonunkhira wa ku malo opatulika. Iwo azipanga monga momwe Ine ndinakulamulira.”
12 Jahve opet reče Mojsiju:
Ndipo Yehova anati kwa Mose,
13 “Reci Izraelcima: Subote moje morate održavati, jer subota je znak između mene i vas od naraštaja do naraštaja, da budete svjesni da vas ja, Jahve, posvećujem.
“Uza ana a Israeli kuti azisunga Masabata anga. Ichi chidzakhala chizindikiro pakati pa inu ndi Ine pamodzi ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo, chosonyeza kuti Ine ndine amene ndimakuyeretsani.
14 Držite, dakle, subotu, jer je ona za vas sveta. Tko je oskvrne neka se pogubi; tko bude u njoj radio ikakav posao neka se odstrani iz svoga naroda.
“Motero muzisunga tsiku la Sabata chifukwa ndi loyera kwa inu. Aliyense amene adetsa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
15 Šest dana neka se vrše poslovi, ali sedmi dan neka bude dan posvemašnjeg odmora, Jahvi posvećen. Tko bi u dan subotni obavljao kakav posao neka se pogubi.
Mugwire ntchito kwa masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, lopuma, tsiku lopatulika la Yehova. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa.
16 Stoga neka Izraelci drže subotu - svetkujući je od naraštaja do naraštaja - kao vječni savez.
Aisraeli onse komanso zidzukulu zawo mʼtsogolo azidzasunga tsiku la Sabata ngati pangano lamuyaya.
17 Neka je ona znak, zauvijek, između mene i Izraelaca. TÓa Jahve je za šest dana sazdao nebo i zemlju, a sedmoga je dana prestao raditi i odahnuo.”
Tsiku la Sabata lidzakhala chizindikiro chamuyaya pakati pa Ine ndi Aisraeli chosonyeza kuti Yehova analenga za kumwamba ndi dziko lapansi kwa masiku asanu ndi limodzi ndi kuti pa tsiku lachisanu ndi chiwiri analeka kugwira ntchito napumula.”
18 Kad Jahve svrši svoj razgovor s Mojsijem na Sinajskom brdu, dade mu dvije ploče Svjedočanstva, ploče kamene, ispisane prstom Božjim.
Yehova atamaliza kuyankhula ndi Mose pa phiri la Sinai, anamupatsa Mose miyala iwiri yaumboni, imene Mulungu analembapo ndi chala chake.