< Estera 6 >
1 Te noći kralj ne mogaše usnuti. Zato naredi da mu donesu i čitaju knjigu znamenitih događaja, Ljetopise.
Usiku umenewo mfumu inalephera kugona tulo; Choncho inayitanitsa buku limene amalembamo mbiri ya zamakedzana kuti amuwerengere.
2 Tu se nađe zapisano kako je Mordokaj prokazao Bigtanu i Tereša, dva dvoranina kraljeva, čuvare praga, koji su se spremali da podignu ruke na kralja Ahasvera.
Anapeza kuti mʼbukumo munalembedwa zoti Mordekai anawulula kuti Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa a mfumu amene ankalondera pa khomo la chipinda cha mfumu ndiwo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.
3 Kralj upita: "Kakva je čast i kakvo je odlikovanje zapalo Mordokaja za sve to?" Kraljeve sluge, dvorani koji ga slušahu, odgovoriše: "Ništa nije učinjeno za nj."
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi Mordekai anamupatsa ulemu ndi ukulu wotani chifukwa cha chinthu chimene anachitachi?” Atumiki ake anamuyankha kuti, “Palibe chimene chinachitika kwa iye.”
4 Kralj onda zapita: "Tko je u predvorju?" A to u vanjsko predvorje kraljevske palače bijaše stigao Haman da traži od kralja neka objese Mordokaja na vješalima koja su već bila podignuta za nj.
Mfumu inati, “Kodi ndani ali mʼbwalomo?” Tsono Hamani anali atangolowa kumene mʼbwalo lakunja la nyumba yaufumu kuti akawuze mfumu zomukhomera Mordekai pa mtanda umene anamukonzera.
5 Službenici kraljevi odgovoriše: "Eno se u predvorju nalazi Haman." "Neka uđe!" - naredi kralj.
Atumiki ake anamuyankha kuti, “Hamani ndiye wayima mu bwalo.” “Mulowetseni,” Mfumu inalamulira.
6 Kako Haman uđe, kralj ga upita: "Što treba učiniti čovjeku koga kralj hoće da počasti?" Haman reče u sebi: "Koga ako ne mene kralj želi počastiti?"
Hamani atalowa, mfumu inamufunsa kuti, “Kodi timuchitire ulemu otani munthu amene mfumu ikondweretsedwa naye?” Tsono Hamani anaganiza mu mtima kuti, “Kodi palinso ndani amene mfumu ingamulemekeze kuposa ine?”
7 Zato odgovori kralju: "Za čovjeka koga kralj želi počastiti
Choncho Hamani anayankha mfumuyo kuti, “Munthu amene mfumu ifuna kumuchitira ulemu, imuchitire izi:
8 treba donijeti kraljevske haljine koje kralj sam oblači i dovesti konja kojega kralj jaše i položiti mu na glavu kraljevsku krunu.
Anthu abwere ndi chovala cha ufumu ndi kavalo amene mfumu imakwerapo wokhala ndi chizindikiro chaufumu pamutu pake.
9 Haljine i konja neka kralj preda jednome od najuglednijih kneževa kraljevih da bi taj obukao onoga koga kralj želi počastiti i na konju ga odveo na gradski trg uzvikujući pred njim: 'Tako biva onome koga kralj hoće da počasti!'"
Ndipo mupereke chovala cha ufumucho ndi kavalo kwa mmodzi wa akalonga a mfumu a ulemu kwambiri. Ameneyu amuveke chovalacho munthu amene mfumu yakondweretsedwa naye. Akavekedwa chovalachi amuyendetse mʼmisewu yonse ya mzinda atakwera pa kavalo wa mfumu. Kalongayu azifuwula patsogolo pa munthuyu kuti ‘Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!’”
10 Kralj nato naredi Hamanu: "Uzmi odmah haljine i konja, kako si rekao, pa učini tako Mordokaju Židovu koji sjedi na kraljevim vratima i ne propusti ništa od onoga što si rekao!"
Mfumu inalamulira Hamani kuti, “Pita msanga, katenge chovala cha ufumu ndi kavalo ndipo uchite monga wanenera kwa Mordekai Myuda, amene amakhala pa chipata cha mfumu. Usasiyeko china chilichonse chimene wanena.”
11 Haman uze haljine i konja: obuče u haljine Mordokaja i provede ga na konju po trgu grada vičući pred njim: "Tako biva onome koga kralj hoće da počasti!"
Choncho Hamani anatenga chovala ndi kavalo. Anamuveka Mordekai chovalacho ndipo anamuyendetsa mʼmisewu yonse ya mu mzinda atakwera pa kavalo, akufuwula kuti, “Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!”
12 Malo zatim Mordokaj se vrati k vratima kraljevim, a Haman, tužan i zastrte glave, ode žurno kući
Pambuyo pake Mordekai anabwerera ku chipata cha mfumu. Koma Hamani anapita msanga ku nyumba kwake, akulira, atafundira mutu wake.
13 te ispriča Zareši, ženi svojoj, i svima prijateljima svojim što se dogodilo. Njegovi mu savjetnici i žena Zareša rekoše: "Ako Mordokaj, pred kojim si počeo posrtati, pripada židovskom rodu, nećeš ga nadjačati, nego će te on zacijelo oboriti."
Hamani anawuza Zeresi mkazi wake ndi abwenzi ake onse zonse zinamuchitikira. Anthu ake anzeru ndi mkazi wake Zeresi anamuwuza kuti, “Popeza kuti Mordekai ndi Myuda amene mwayamba kale kugonja pamaso pake, ndiye kuti palibe chimene mungachitepo. Mudzagwa ndithu pamaso pake.”
14 Još su o tom razgovarali, kad eto kraljevih dvorana. Došli su tražiti Hamana da ga žurno odvedu na gozbu koju je priredila Estera.
Pamene anthuwa amayankhula nayebe, adindo a mfumu ofulidwa anabwera kudzamutenga Hamani mofulumira kupita naye ku phwando limene Estere anakonza.