< Ponovljeni zakon 16 >
1 Drži mjesec Abib i slavi Pashu u čast Jahvi, Bogu svome, jer te Jahve, Bog tvoj, u mjesecu Abibu izveo noću iz Egipta.
Samalirani mwezi wa Abibu ndi kukondwerera Paska wa Yehova Mulungu wanu, chifukwa pa mwezi wa Abibu, usiku, Iye anakutulutsani mu Igupto.
2 Kao pashu u čast Jahvi, Bogu svome, žrtvuj ovce i goveda u mjestu koje Jahve odabere da u njemu nastani ime svoje.
Mumuphere Yehova Mulungu wanu nsembe ya Paska, chiweto chochokera pa nkhosa zanu kapena ngʼombe zanu kumalo kumene Yehova adzasankha kuti akhazikeko dzina lake.
3 Ništa ukvasano nemoj s njome jesti; nego sedam dana jedi beskvasan kruh - kruh nevoljnički - budući da si u žurbi izišao iz zemlje egipatske: da se svega svog vijeka sjećaš dana kad si izišao iz zemlje egipatske.
Musadyere pamodzi ndi buledi wopanga ndi yisiti, koma kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti, buledi wa masautso, chifukwa munachoka ku Igupto mwamsangamsanga kuti pa masiku onse a moyo wanu muzikumbukira nthawi imene munanyamukira ku Igupto.
4 Neka se sedam dana u tebe ne vidi kvasac na svemu tvome području i ništa od mesa žrtve što je zakolješ navečer prvoga dana ne smije ostati preko noći do jutra.
Yisiti asapezeke kwa masiku asanu ndi awiri pa katundu wanu mʼdziko lanu lonse. Ndipo musasunge nyama imene mwapereka nsembe madzulo a tsiku loyamba mpaka mmawa.
5 Nije ti dopušteno žrtvovati pashu u bilo kojem gradu što ti ga dadne Jahve, Bog tvoj,
Musamangopereka nsembe ya Paska mu mzinda wina uliwonse umene Yehova Mulungu wanu wakupatsani,
6 nego u mjestu koje odabere Jahve, Bog tvoj, da ondje nastani ime svoje; samo tu žrtvuj pashu u predvečerje, o zalasku sunca, jer u to si vrijeme izišao iz Egipta.
koma ku malo wokhawo amene Iye adzawasankhe kukhazikitsako Dzina lake. Kumeneko ndiye muzikapereka nsembe ya Paska madzulo, pamene dzuwa likulowa, pa tsiku lokumbukira kutuluka mu Igupto.
7 Skuhaj je i pojedi na mjestu koje odabere Jahve, Bog tvoj. Ujutro se onda okreni i zaputi svojim šatorima.
Muyiwotche ndi kuyidya pa malo pamene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. Kenaka mmawa mubwerere ku matenti anu.
8 Šest dana jedi beskvasan kruh, a sedmoga dana neka bude svečani zbor u čast Jahvi, Bogu tvome. Posla nikakva ne radi!
Kwa masiku asanu ndi limodzi muzidya buledi wopanda yisiti ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wa Yehova Mulungu wanu ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
9 Nabroj sedam tjedana; a tih sedam tjedana uzmi brojiti kad srp počne žeti klasje.
Muziwerenga masabata asanu ndi awiri kuyambira pamene mwatenga chikwakwa ndi kuyamba kumweta tirigu wachilili.
10 Tada drži Blagdan sedmica u čast Jahvi, Bogu svome, prinoseći dragovoljni prinos iz svoje ruke, kako te već Jahve, Bog tvoj, bude blagoslovio.
Pamenepo muzichita Chikondwerero cha Masabata pamaso pa Yehova Mulungu wanu popereka chopereka chaufulu mofanana ndi madalitso amene Yehova Mulungu wakupatsani
11 I proveseli se tada u nazočnosti Jahve, Boga svoga - na mjestu što ga Jahve, Bog tvoj, odabere da ondje nastani ime svoje - ti, sin tvoj i kći tvoja, sluga tvoj i sluškinja tvoja, levit koji bude u tvome gradu, došljak, sirota i udovica što budu kod tebe.
Ndipo inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi a mʼmizinda mwanu, alendo, ana ndi akazi amasiye okhala pakati panu, mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku malo amene adzawasankhe kukhazikitsako dzina lake.
12 Sjećaj se da si i sam bio rob u Egiptu. Zato drži i vrši ove uredbe.
Kumbukirani kuti inunso munali akapolo ku Igupto, ndiye muzitsatira malangizo awa mosamalitsa.
13 Blagdan sjenica slavi sedam dana pošto pokupiš plodove sa svoga gumna i iz svoga badnja.
Mukatha kukolola tirigu wanu ndi kupsinya vinyo wanu, muzikhala ndi Chikondwerero cha Misasa kwa masiku asanu ndi awiri.
14 Proveseli se na svoj blagdan ti, sin tvoj, kći tvoja, sluga tvoj, sluškinja tvoja, levit i došljak, sirota i udovica što se nađe u tvome gradu.
Musangalale pa chikondwerero chanu, inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi, alendo, ana ndi akazi amasiye amene ali mʼmizinda yanu.
15 Svetkuj u čast Jahvi, Bogu svome, sedam dana na mjestu koje odabere Jahve, jer će te Jahve, Bog tvoj, blagoslovom obasipati u svim tvojim žetvama, u svakom poslu ruku tvojih, da budeš potpuno veseo.
Kwa masiku asanu ndi awiri muzichita chikondwererochi kwa Yehova Mulungu wanu kumalo kumene Yehova adzasankhe. Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani inu pa zokolola zanu ndi pa ntchito za manja anu, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.
16 Triput u godini neka se pokažu svi tvoji muškarci pred Jahvom, Bogom tvojim, na mjestu koje on odabere: na Blagdan beskvasnog kruha, na Blagdan sedmica i na Blagdan sjenica. Ali neka nitko ne dođe pred Jahvu praznih ruku,
Amuna onse azionekera pamaso pa Yehova Mulungu katatu pa chaka ku malo amene Iye adzasankha. Pa Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti, pa Chikondwerero cha Masabata ndi pa Chikondwerero cha Misasa. Munthu aliyense asadzapite pamaso pa Yehova wopanda kanthu mʼmanja mwake.
17 nego neka svatko prinese što može, prema blagoslovu koji ti je udijelio Jahve, Bog tvoj.
Aliyense wa inu adzabweretse mphatso molingana ndi momwe Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
18 U svakom gradu koji ti dade Jahve, Bog tvoj, postavi suce i nadglednike za svoja plemena da narodom pravedno upravljaju.
Musankhe oweruza ndi akuluakulu a fuko lanu lililonse mu mzinda uliwonse umene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, ndipo adzaweruza anthuwa mwachilungamo.
19 Ne iskrivljuj pravde; ne budi pristran; ne primaj mita, jer mito zasljepljuje oči mudrih, a ugrožava stvar pravednih.
Musamakhotetse chiweruzo kapena kukondera. Musamalandire chiphuphu pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu a nzeru ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.
20 Teži za samom pravdom, da dugo živiš i zaposjedneš zemlju koju ti Jahve, Bog tvoj, daje.
Tsatani chilungamo chokhachokha basi kuti mukhale ndi moyo ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
21 Ne postavljaj ašere ni od kakva drveta oko žrtvenika Jahve, Boga svoga, koji podigneš;
Musazike mtengo wina uliwonse wa mafano a Asera pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu,
22 i ne podiži stupova, jer su na zazor Jahvi, Bogu tvome.
ndipo musayimike mwala wachipembedzo pakuti Yehova Mulungu wanu amadana nazo zimenezi.