< 2 Timoteju 2 >
1 Ti se dakle, dijete moje, jačaj milošću u Kristu Isusu
Tsono iwe, mwana wanga, limbika mʼchisomo chimene chili mwa Khristu Yesu.
2 i što si od mene po mnogim svjedocima čuo, to predaj vjernim ljudima koji će biti podobni i druge poučiti.
Ndipo zinthu zimene unamva ine ndikuziyankhula pamaso pa mboni zambiri, uziphunzitse kwa anthu odalirika amene akaphunzitsenso ena.
3 S njima se zlopati kao dobar vojnik Krista Isusa.
Umve nane zowawa, monga msilikali wa Khristu Yesu.
4 Tko vojuje, ne zapleće se u svagdanje poslove kako bi se vojskovođi svidio.
Palibe msilikali amene ali pa ntchito amagwiranso ntchito za anthu wamba, iye amafuna kukondweretsa bwana wolamulira.
5 I natječe li se tko, ne ovjenčava se ako se zakonito ne natječe.
Chimodzimodzinso, munthu amene ali pa mpikisano waliwiro, salandira mphotho ya wopambana pokhapokha atatsiriza monga mwa malamulo a mpikisanowo.
6 Ratar koji se trudi treba da prvi primi od uroda.
Mlimi wolimbika ndi amene amayembekezereka kukhala woyambirira kulandira gawo la zokolola.
7 Shvati što govorim! Ta dat će ti Gospodin razum u svemu.
Lingalira zimene ndikunenazi, pakuti Ambuye adzakuzindikiritsa zonsezi.
8 Spominji se Isusa Krista, uskrsla od mrtvih, od potomstva Davidova - po mojem evanđelju.
Kumbukira Yesu Khristu wochokera ku mtundu wa Davide kuti anauka kwa akufa. Uwu ndiye uthenga wanga wabwino
9 Za nj se ja zlopatim sve do okova, kao zločinac. Ali riječ Božja nije okovana!
umene ndikuwuvutikira choterewu mpaka kumangidwa ndi maunyolo ngati wakuba. Koma mawu a Mulungu sanamangidwe ndi maunyolo.
10 Stoga sve podnosim radi izabranih, da i oni postignu spasenje, spasenje u Kristu Isusu, zajedno s vječnom slavom. (aiōnios )
Choncho ndikupirira chilichonse chifukwa cha osankhidwa, kuti nawonso apulumutsidwe ndi Khristu Yesu ndi kulandira ulemerero wosatha. (aiōnios )
11 Vjerodostojna je riječ: Ako s njime umrijesmo, s njime ćemo i živjeti.
Mawu oyenera kuwadalira ndi awa: Ngati ife tinafa naye pamodzi, tidzakhalanso moyo pamodzi naye.
12 Ako ustrajemo, s njime ćemo i kraljevati. Ako ga zaniječemo, i on će zanijekati nas.
Ngati tinapirira, tidzalamuliranso naye pamodzi. Ngati ife timukana, Iye adzatikananso.
13 Ako ne budemo vjerni, on vjeran ostaje. Ta ne može sebe zanijekati!
Ngati ndife osakhulupirika, Iye adzakhalabe wokhulupirika popeza sangathe kudzikana.
14 Na to podsjećaj zaklinjući pred Bogom neka ne bude rječoborstva: ničemu ne koristi, a na propast je onima koji slušaju.
Uziwakumbutsa anthu a Mulungu zinthu izi. Uwachenjeze pamaso pa Mulungu kuti asamakangane pa za mawu. Zimenezi nʼzopanda phindu ndipo zimangowononga amene akumvawo.
15 Uznastoj da kao prokušan staneš pred Boga kao radnik koji se nema čega stidjeti, koji ispravno reže riječ istine.
Uyesetse kukhala wovomerezeka pamaso pa Mulungu monga wantchito wopanda chifukwa chochitira manyazi amene amalalikira mawu achoonadi molondola.
16 Svjetovnih se pak praznorječja kloni: sve će više provaljivati prema bezbožnosti
Upewe nkhani zopanda pake, zosalemekeza Mulungu, chifukwa anthu oyankhula zotere amanka napotokerapotokera.
17 i riječ će njihova kao rak-rana izgrizati. Od njih su Himenej i Filet,
Chiphunzitso chawo chidzafalikira ngati chilonda. Mwa anthuwa muli Humenayo ndi Fileto.
18 koji zastraniše od istine tvrdeći da je uskrsnuće već bilo te nekima prevraćaju vjeru.
Iwowa apatuka pa choonadi. Iwo amaphunzitsa kuti kuuka kwa akufa kunachitika kale, motero amawononga chikhulupiriro cha anthu ena.
19 Ipak čvrsti temelj Božji stoji - pod ovim je pečatom: Poznaje Gospodin one koji su njegovi i neka se kloni zloće tko god imenuje ime Gospodnje.
Komabe maziko olimba, amene Mulungu anawayika ngokhazikika, ndipo mawu olembedwapo ndi awa: “Yehova amadziwa amene ndi ake,” ndiponso, “Aliyense amene amavomereza dzina la Ambuye ayenera kusiya zoyipa.”
20 Pa u velikoj kući ima posuda ne samo zlatnih i srebrnih, nego i drvenih i glinenih; i jedne su časne, druge pak nečasne.
Mʼnyumba yayikulu simukhala ziwiya zagolide ndi zasiliva zokha, koma mumakhalanso zamtengo ndi zadothi. Zina zimakhala za ntchito yapamwamba, zina za ntchito wamba.
21 Očisti li se dakle tko od toga, bit će posuda časna, posvećena, korisna Gospodaru, za svako dobro djelo prikladna.
Munthu akadziyeretsa nʼkusiya ntchito za wambazi, adzakhala chiwiya cha ntchito yapamwamba, woyeretsedwa, ndi waphindu kwa Ambuye wake, wokonzeka kugwira ntchito iliyonse yabwino.
22 A mladenačkih se strastvenosti kloni! Teži za pravednošću, vjerom, ljubavlju, mirom sa svima koji iz čista srca prizivlju Gospodina.
Thawa zilakolako zoyipa zachinyamata. Funafuna chilungamo, chikhulupiriro, chikondi ndi mtendere pamodzi ndi amene akuyitanira pa dzina la Ambuye ndi mtima osadetsedwa.
23 Lude pak i neobuzdane raspre odbijaj znajući da rađaju svađama.
Ukane matsutsano oyipa ndi opusa, chifukwa amayambitsa mikangano.
24 A sluga Gospodnji treba da se ne svađa, nego da bude nježan prema svima, sposoban poučavati, zlo podnositi,
Ndiponso mtumiki wa Ambuye asamakangane ndi anthu, koma azikhala wachifundo kwa aliyense, wodziwa kuphunzitsa, osati wokalipakalipa.
25 da s blagošću preodgaja protivnike, ne bi li ih Bog podario obraćenjem te spoznaju istinu
Otsutsana naye awalangize mofatsa, mwina Mulungu adzawapatsa mwayi woti asinthike ndi kuzindikira choonadi.
26 i ponovno budu trijezni izvan zamke đavla koji ih drži robljem svoje volje.
Motero nzeru zawo zidzabweramo, ndipo adzathawa msampha wa mdierekezi, amene anawagwira ukapolo kuti azichita zofuna zake.