< 2 Samuelova 11 >

1 U početku slijedeće godine, u doba kad kraljevi izlaze u rat, posla David Joaba i s njim svoje ljude i svega Izraela: oni pobiše Amonce i podsjedoše Rabu. A David osta u Jeruzalemu.
Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Davide anatumiza Yowabu ndi ankhondo a mfumu pamodzi ndi gulu lonse lankhondo la Aisraeli. Iwo anawononga Aamoni ndi kuzungulira mzinda wa Raba. Koma Davide anatsala ku Yerusalemu.
2 A jednoga dana predveče usta David sa svoje postelje i prošeta se po krovu svoje palače. Opazi s krova ženu gdje se kupa. Ta žena bijaše izvanredno lijepa.
Tsiku lina cha kumadzulo Davide anadzuka pa bedi lake ndipo ankayenda pamwamba pa nyumba yake. Ali pa dengapo anaona mkazi akusamba. Mkaziyo anali wokongola kwambiri.
3 David se propita za tu ženu i rekoše mu: “Pa to je Bat-Šeba, kći Eliamova i žena Urije Hetita!”
Ndipo Davide anatuma munthu wina kuti akafufuze za iye. Munthuyo anati, “Kodi uyu si Batiseba, mwana wa Eliamu, mkazi wa Uriya Mhiti?”
4 Nato David posla glasnika da je dovedu k njemu. Kad je došla, leže on s njom, upravo kad se bila očistila od svoje nečistoće. Zatim se ona vrati svojoj kući.
Ndipo Davide anatumiza amithenga kwa iye kukamuyitana. Batiseba anabwera kwa Davide ndipo anagona naye. (Nʼkuti mkaziyu atayeretsedwa ku masiku ake osamba). Kenaka anabwerera ku nyumba yake.
5 Žena zatrudnje te poruči Davidu: “Trudna sam!”
Mkaziyo anakhala woyembekezera ndipo anatumiza mawu kwa Davide kunena kuti, “Ine ndine woyembekezera.”
6 Tada David posla poruku Joabu: “Pošalji k meni Uriju Hetita!” I Joab posla Uriju k Davidu.
Ndipo Davide anatumiza mawu awa kwa Yowabu: “Nditumizire Uriya Mhiti.” Ndipo Yowabu anamutumiza kwa Davide.
7 Kad je Urija došao k njemu, zapita ga David kako je Joab, kako je vojska i kako napreduje rat.
Uriya atafika kwa Davide, Davide anamufunsa za momwe analili Yowabu, za asilikali ndi momwe nkhondo inkayendera.
8 Potom David reče Uriji: “Siđi u svoju kuću i operi svoje noge!” Urija iziđe iz kraljeva dvora, a za njim ponesoše dar s kraljeva stola.
Kenaka Davide anati kwa Uriya, “Pita ku nyumba yako ukapumule.” Choncho Uriya anachoka ku nyumba yaufumu, ndipo mfumuyo inatumiza mphatso kwa Uriya.
9 Ali Urija osta da spava pred vratima kraljeva dvora sa stražarima svoga gospodara i ne ode svojoj kući.
Koma Uriya anagona pa chipata cha nyumba yaufumu pamodzi ndi antchito onse a mbuye wake ndipo sanapite ku nyumba yake.
10 Javiše to Davidu govoreći: “Urija nije otišao svojoj kući!” Tada David upita Uriju: “Zar nisi došao s puta? Zašto ne ideš svojoj kući?”
Davide atawuzidwa kuti, “Uriya sanapite ku nyumba yake.” Iye anafunsa kuti, “Kodi iwe sunachokera kutali? Nʼchifukwa chiyani sunapite ku nyumba yako?”
11 A Urija odgovori Davidu: “Kovčeg, Izrael i Juda borave pod šatorima, moj gospodar Joab i straža moga gospodara borave na otvorenu polju, a ja da uđem u svoju kuću da jedem i da pijem i da spavam sa svojom ženom? Živoga mi Jahve, i tako mi tvoga života, zaista neću učiniti nešto takvo!”
Uriya anayankha Davide kuti, “Bokosi la Chipangano ndi Israeli ndiponso Yuda akukhala mʼmatenti, ndipo mbuye wanga Yowabu ndi ankhondo anu mbuye wanga amanga misasa pa mtetete. Ine ndingapite bwanji ku nyumba yanga kukadya ndi kumwa ndiponso kugona ndi mkazi wanga? Pali inu wamoyo, ine sindidzachita chinthu chimenechi.”
12 Tada David reče Uriji: “Ostani još danas ovdje, a sutra ću te otpustiti.” Tako Urija osta u Jeruzalemu onaj dan.
Ndipo Davide anati kwa iye, “Ukhale konkuno tsiku lina limodzi, ndipo mawa ndikulola kuti upite.” Kotero Uriya anakhala mu Yerusalemu tsiku limenelo ndi tsiku linalo.
13 Sutradan David pozva Uriju da jede i da pije pred njim i on ga opi. A uvečer Urija iziđe i leže na svoju postelju sa stražama svoga gospodara, ali svojoj kući nije otišao.
Davide anayitana Uriya nadya ndi kumwa naye, ndipo Davide anamuledzeretsa. Koma madzulo Uriya anapita kukagona pa mphasa pamodzi ndi antchito a mbuye wake. Iye sanapite ku nyumba yake.
14 Ujutro David napisa pismo Joabu i posla ga po Uriji.
Mmawa Davide analemba kalata kwa Yowabu ndipo anayitumiza ndi Uriya.
15 A u tom pismu pisao je ovako: “Postavite Uriju naprijed, gdje je najžešći boj, pa uzmaknite iza njega: neka bude pogođen i neka pogine!”
Mʼkalatayo analembamo kuti, “Uriya mumuyike patsogolo penipeni, pamene pali nkhondo yoopsa. Ndipo mumusiye yekha kuti akanthidwe ndi kufa.”
16 Zato Joab, opsjedajući grad, postavi Uriju na mjesto gdje je znao da stoje najhrabriji ratnici.
Kotero Yowabu atawuzinga mzindawo, anamuyika Uriya pamalo pamene amadziwa kuti pali asilikali amphamvu.
17 Kad su onda građani provalili van i pobili se s Joabom, pade nekoliko od njegove vojske, od Davidovih ljudi, a pogibe i Urija Hetit.
Ankhondo a mu mzindawo atabwera kudzamenyana ndi Yowabu, anthu ena a gulu la ankhondo la Davide anaphedwa ndipo Uriya Mhiti uja anaphedwanso.
18 Potom Joab posla čovjeka i javi Davidu sve što se dogodilo u boju.
Yowabu anatumiza wamthenga kwa Davide kukafotokoza mwatsatanetsatane za nkhondoyo.
19 I zapovjedi glasniku ovako: “Kad pripovjediš kralju sve što se dogodilo u boju,
Iye anamulangiza wa mthengayo kuti, “Pamene ukatsiriza kufotokozera mfumu za ku nkhondozi,
20 možda će se kralj razljutiti pa ti kazati: 'Zašto ste se primakli tako blizu gradu da navalite? Zar niste znali da se obično izmeću strijele sa zida?
mfumu ikapsa mtima, ndipo akakakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani munapita pafupi ndi mzindawo kukamenya nkhondo? Inu simunadziwe kuti atha kukuponyerani mivi kuchokera pa khoma?
21 Tko je ubio Abimeleka, sina Jerubaalova? Nije li jedna žena bacila na njega mlinski kamen, ozgo sa zida, te je poginuo u Tebesu? Zašto ste se primakli tako blizu zidu?' Ako ti tako kaže, a ti mu reci: 'Poginuo je i tvoj sluga Urija Hetit.'”
Kodi anapha Abimeleki mwana wa Yerubeseti ndani? Kodi mkazi sanamuponyere mphero kuchokera pa khoma? Kotero kuti anakafera ku Tebezi. Nʼchifukwa chiyani munafika pafupi ndi khoma?’ Ngati iye akafunsa zimenezi, iwe ukanene kwa iye kuti, ‘Mtumiki wanunso Uriya Mhiti wafa.’”
22 Glasnik krenu na put, dođe k Davidu i pripovjedi mu sve što mu je naložio Joab. A David planu gnjevom na Joaba i reče glasniku: “Zašto ste se primakli tako blizu zidu? Tko je ubio Abimeleka, sina Jerubaalova? Nije li jedna žena bacila na njega mlinski kamen, ozgo sa zida, te je poginuo u Tebesu? Zašto ste se primakli tako blizu zidu?”
Mthengayo ananyamuka, ndipo atafika anamuwuza Davide zonse zimene Yowabu anamutuma kuti akanene.
23 Glasnik odgovori Davidu: “Ti su ljudi silovito udarali na nas i izašli su protiv nas na otvoreno polje. Mi smo ih potisnuli natrag do gradskih vrata,
Mthengayo anati kwa Davide, “Anthuwo anatiposa mphamvu ndipo anabwera kudzalimbana nafe poyera, koma ife tinawabwezera ku chipata cha mzindawo.
24 ali su strijelci sa zida stali izmetati strijele na tvoje ljude te ih je poginulo nekoliko između kraljevih slugu; tako je poginuo i tvoj sluga Urija Hetit.”
Ndipo anthu oponya mivi anatiponyera kuchokera pa khoma, anthu ena a mfumu afa. Kuwonjezera apo, mtumiki wanu Uriya Mhiti wafanso.”
25 Tada David reče glasniku: “Ovako reci Joabu: 'Nemoj to uzimati toliko k srcu, jer mač proždire sad ovoga, sad onoga. Udaraj još jače na grad i obori ga!' Tako ćeš mu vratiti srčanost!”
Davide anamuwuza mthengayo kuti, “Ukanene izi kwa Yowabu: ‘Zimenezi zisakukhumudwitse; lupanga limapha wina nthawi zinanso wina. Limbikitsa nkhondo pa mzindawo ndipo uwuwononge!’ Ukanene zimenezi pomulimbikitsa Yowabu.”
26 Kad je Urijina žena čula da je poginuo njezin muž Urija, žalila je za svojim mužem.
Mkazi wa Uriya atamva kuti mwamuna wake wafa, analira maliro.
27 A kad je prošlo vrijeme žalosti, posla David po nju i uze je u svoj dvor, i ona mu posta ženom. I rodi mu sina. Ali djelo koje učini David bijaše zlo u očima Jahvinim.
Nthawi yolira maliro itatha, Davide anamubweretsa ku nyumba yake, ndipo anakhala mkazi wake nabala mwana wamwamuna. Koma Yehova sanakondwe ndi zimene Davide anachitazo.

< 2 Samuelova 11 >