< 2 Kraljevima 9 >

1 Prorok Elizej pozva jednoga od proročkih sinova i reče mu: “Opaši se, uzmi sa sobom ovu posudu s uljem pa idi u Ramot Gilead.
Mneneri Elisa anayitanitsa mmodzi mwa ana a aneneri, namuwuza kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga botolo la mafuta mʼdzanja lako ndipo upite ku Ramoti Giliyadi.
2 Kad onamo stigneš, potraži Jehua, sina Jošafatova, sina Nimšijeva. Kad ga nađeš, izvedi ga između njegovih drugova i uvedi ga u pokrajnju sobu.
Ukakafika kumeneko, ukafunefune Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi. Ukapite kwa iye, ukamuchotse pakati pa anzake ndi kukamulowetsa mʼchipinda chamʼkati.
3 I uzmi posudu s uljem, izlij mu je na glavu i reci: 'Ovako veli Jahve: Pomazao sam te za kralja izraelskoga.' Zatim otvori vrata i bježi, ne oklijevaj.”
Ndipo ukatenge botololi ndi kuthira mafuta pa mutu wake ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’ Kenaka ukatsekule chitseko ndi kuthawa ndipo usakachedwe!”
4 Tada mladi prorok ode u Ramot Gilead.
Choncho mneneri wachinyamatayo anapita ku Ramoti Giliyadi.
5 Kad je stigao, zapovjednici vojske upravo su sjedili na okupu. On reče: “Imam ti riječ reći, zapovjedniče!” Jehu upita: “Komu od nas?” On odgovori: “Tebi, zapovjedniče!”
Atafika ku Giliyadiko anapeza atsogoleri a ankhondo ali pa msonkhano. Iye anati, “Mtsogoleri, ine ndili ndi uthenga wanu.” Ndipo Yehu anafunsa kuti, “Uthengawo ndi wa yani pakati pathu?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndi wa inuyo, mtsogoleri.”
6 Jehu tada ustade i uđe u kuću. Mladi mu čovjek izli ulje na glavu i reče mu: “Ovako veli Jahve, Bog Izraelov: 'Pomazao sam te za kralja nad Jahvinim narodom, nad Izraelom.
Yehu anayimirira nakalowa mʼnyumba. Pamenepo mneneriyo anakhuthulira mafuta pamutu pa Yehu ndipo ananena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndikukudzoza kukhala mfumu ya Israeli, anthu a Yehova.
7 Ti ćeš pobiti obitelj Ahaba, gospodara tvoga, a ja ću osvetiti krv svojih slugu proroka i krv sviju službenika Jahvinih na Izebeli
Uyenera kuwononga nyumba ya mbuye wako Ahabu ndipo ndidzabwezera imfa ya atumiki anga, aneneri ndiponso imfa ya atumiki ena onse a Yehova amene anaphedwa ndi Yezebeli.
8 i na svoj obitelji Ahabovoj. Iskorijenit ću Ahabu sve što mokri uza zid, robove i slobodnjake u Izraelu.
Banja lonse la Ahabu lidzatheratu. Ndidzachotsa munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu kaya ndi kapolo kapena mfulu.
9 Učinit ću s domom Ahabovim kao s domom Jeroboama, sina Nebatova, i kao s domom Baše, sina Ahijina.
Ndidzachititsa kuti banja la Ahabu lifanane ndi banja la Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati banja la Baasa mwana wa Ahiya.
10 A Izebelu će proždrijeti psi na polju jizreelskom i nitko je neće pokopati.'” - Zatim otvori vrata i pobježe.
Kunena za Yezebeli, agalu adzamudya ku dera la Yezireeli ndipo palibe amene adzamuyike mʼmanda.’” Kenaka mneneriyo anatsekula chitseko nʼkuthawa.
11 Jehu iziđe k časnicima svoga gospodara. Oni ga upitaše: “Je li sve u miru? Zašto je ta budala dolazila k tebi?” On im odgovori: “Znate čovjeka i besjedu njegovu.”
Yehu atatuluka kupita kumene kunali atsogoleri anzake, mmodzi mwa iwo anamufunsa kuti, “Kodi zonse zili bwino? Kodi munthu wamisala uja anabwera kudzatani kwa iwe?” Yehu anayankha kuti, “Iwe ukumudziwa munthu uja ndiponso ukudziwa zomwe amayankhula.”
12 Oni rekoše: “Ne znamo! Kazuj nam!” On im reče: “Govorio mi je tako i tako i rekao mi: 'Ovako veli Jahve: Pomazao sam te za kralja nad Izraelom.'”
Atsogoleri aja anati, “Ukunama! Tiwuze.” Yehu anati, “Zimene wandiwuza ndi izi: ‘Yehova akuti: Ine ndakudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’”
13 Odmah oni uzeše svoje ogrtače i prostriješe ih pred njim po stepenicama, zatrubiše u rogove i povikaše: “Jehu je kralj!”
Atsogoleri aja mofulumira anatenga zofunda zawo naziyala pansi pa makwerero kuti Yehu akhalepo. Kenaka analiza lipenga, nafuwula kuti, “Yehu ndiye mfumu!”
14 Tako Jehu, sin Jošafata, sina Nimšijeva, skova urotu protiv Jorama - Joram je tada branio Ramot Gilead sa svim Izraelcima protiv Hazaela, aramejskog kralja.
Choncho Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi, anachitira chiwembu Yoramu. (Nthawi imeneyi nʼkuti Yoramu ndi Aisraeli onse akuteteza Ramoti Giliyadi kwa Hazaeli mfumu ya ku Aramu,
15 Ali se kralj Joram vratio u Jizreel da liječi rane koje su mu zadali Aramejci u boju s Hazaelom, aramejskim kraljem. - I reče Jehu: “Ako vam je po volji, neka nitko ne utekne iz grada da odnese vijest u Jizreel.”
koma nʼkuti Yoramu atabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene Aaramu anamuvulaza pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya ku Aramu.) Yehu anati, “Ngati mukugwirizana nazo zimenezi, wina aliyense asatuluke mu mzinda muno kupita kukafotokoza nkhaniyi ku Yezireeli.”
16 Jehu se tada pope na kola i ode prema Jizreelu, jer je Joram ondje bolovao, i Ahazja, kralj judejski, došao ga posjetiti.
Pamenepo Yehu anakwera galeta lake, napita ku Yezireeli, chifukwa Yoramu anali akupumula kumeneko ndipo Ahaziya, mfumu ya ku Yuda, nʼkuti ali komweko kudzamuona.
17 Stražar koji je stajao na kuli u Jizreelu, videći da dolazi Jehuova četa, javi: “Vidim nekakvu četu.” Joram naredi: “Uzmi konjanika i pošalji ga pred njih da upita: je li sve s mirom.”
Mlonda amene ankayimirira pa nsanja yolondera mzinda wa Yezireeli ataona gulu lankhondo la Yehu likuyandikira, anafuwula kuti, “Ndikuona gulu lankhondo likubwera.” Yoramu analamula kuti, “Peza munthu wokwera kavalo, mutume kuti akakumane nawo ndi kuwafunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’”
18 Ode konjanik preda nj i reče: “Ovako veli kralj: je li sve s mirom?” - Jehu odgovori: “Što te briga je li s mirom! Hajde za mnom.” Stražar javi: “Glasnik je stigao do njih, ali se ne vraća.”
Choncho munthu wokwera kavalo anapita kukakumana ndi Yehu ndipo anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.” Mlonda uja anakafotokoza kwa mfumu kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwerera.”
19 Kralj posla drugoga konjanika. Taj dođe k njima i upita: “Ovako veli kralj: je li sve s mirom?” - Jehu mu odgovori: “Što te briga je li s mirom! Hajde za mnom.”
Choncho mfumu inatumanso munthu wina wachiwiri wokwera kavalo. Atafika kwa anthuwo iye anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.”
20 Stražar opet javi: “Došao je do njih, ali se ne vraća. A vožnja je kao vožnja Jehua, sina Nimšijeva: vozi kao mahnit!”
Mlonda uja anakanenanso kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwereranso. Kuyendako kukukhala ngati kwa Yehu mwana wa Nimisi, iye amayenda ngati munthu wamisala.”
21 Joram reče: “Preži!” I upregoše u njegova kola. Joram, kralj Izraela, i judejski kralj Ahazja iziđoše, svaki u svojim kolima, u susret Jehuu. Susretoše ga u polju Nabota Jizreelca.
Yoramu analamula kuti, “Konzani galeta langa.” Ndipo atakonza galeta lake, Yoramu mfumu ya Israeli ndi Ahaziya mfumu ya ku Yuda anakwera nʼkutuluka mu mzindamo, aliyense atakwera galeta lake, kukakumana ndi Yehu. Iwo anakumana ndi Yehu pa munda umene unali wa Naboti, wa ku Yezireeli.
22 Kad Joram ugleda Jehua, upita ga: “Je li sve u miru, Jehu?” Ovaj odgovori: “Kakvu miru dok traju bludništva tvoje majke Izebele i njena mnoga čaranja!”
Yoramu ataona Yehu anafunsa kuti, “Yehu, kodi wabwera mwamtendere?” Yehu anayankha kuti, “Pangakhale bwanji mtendere pamene zopembedza mafano zonse zilipo ndiponso ufiti wa amayi ako Yezebeli uli ponseponse?”
23 Joram okrenu i udari u bijeg govoreći Ahazji: “Izdaja, Ahazja!”
Yoramu anatembenuka, nathawa akufuwula kwa Ahaziya kuti, “Ahaziya, anthuwa atiwukira!”
24 Jehu se lati luka, ustrijeli Jorama među pleća: strijela mu prođe posred srca te se on sruši u kola.
Pamenepo Yehu anakoka uta wake ndipo analasa Yoramu kumsana pakati pa mapewa. Muviwo unakalasa mtima wake ndipo anagwa pansi mʼgaleta lakelo.
25 Jehu reče svome dvorjaniku Bidkaru: “Digni ga i baci na njivu Nabota Jizreelca. Sjeti se: kad smo ja i ti jahali za njegovim ocem Ahabom, kako Jahve izreče protiv njega:
Yehu anawuza Bidikara, mtsogoleri wa galeta lake kuti, “Munyamule ndipo ukamuponye mʼmunda umene unali wa Naboti wa ku Yezireeli, chifukwa kumbukira mmene iwe ndi ine tinkayenda pambuyo pa Ahabu abambo ake, kuti Yehova ananeneratu za iye kuti,
26 'Kunem se: kako sinoć vidjeh krv Nabotovu i krv njegovih sinova,' riječ je Jahvina, 'tako ću ti vratiti isto na ovome polju,' riječ je Jahvina. Digni ga, dakle, i baci ga na to polje, prema riječi Jahvinoj.”
‘Zoonadi dzulo ndinaona magazi a Naboti ndi magazi a ana ake, akutero Yehova, ndipo Ine ndidzakubwezera ndithu choyipa chimenechi pa munda womwe uno, akutero Yehova.’ Tsono munyamule ndipo ukamuponye mʼmundamo, potsatira zimene Yehova ananena.”
27 Kada je to vidio judejski kralj Ahazja, pobježe prema Bet Haganu, ali ga je Jehu gonio i naredio: “Ubijte i njega!” Ranili su ga u kolima na brdu Guru, koje se nalazi kod Jibleama. Ali je umakao u Megido i ondje umrije.
Ahaziya mfumu ya ku Yuda ataona zimene zinachitika, anathawira ku Beti Hagani. Yehu anamuthamangitsa, uku akufuwula kuti, “Mupheninso!” Iwo anamuvulaza ali mʼgaleta lakelo pa njira yopita ku Guri pafupi ndi Ibuleamu, koma iye anathawira ku Megido ndipo anakafera kumeneko.
28 Njegove su ga sluge u kolima prenijele u Jeruzalem i sahranile ga u grobnici kraj njegovih otaca, u Davidovu gradu.
Antchito ake anamunyamulira mʼgaleta kupita naye ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide.
29 Jedanaeste godine kraljevanja Jorama, sina Ahabova, Ahazja postade kralj nad Judejom.
(Mʼchaka cha khumi ndi chimodzi cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu, Ahaziya anakhala mfumu ya ku Yuda).
30 A Jehu bijaše ušao u Jizreel. Kad je to čula Izebela, namaza oči, uresi glavu i pogleda s prozora.
Kenaka Yehu anapita ku Yezireeli. Yezebeli atamva zimene zinachitika, anapaka zodzikometsera mʼmaso, naluka tsitsi lake, namasuzumira pa zenera.
31 I kad je Jehu ulazio na vrata, ona reče: “Kako je, Zimri, ubojico svoga gospodara?”
Pamene Yehu ankalowa pa chipata iye anafunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere, iwe Zimuri, munthu wopha mbuye wako?”
32 Jehu okrenu lice prema prozoru i reče: “Tko je sa mnom, tko?” I dva-tri dvoranina pogledaše prema njemu.
Yehu anakweza maso nayangʼana pa zenera, ndipo anafuwula kuti, “Kodi ndani ali mbali yanga? Ndani?” Anthu ofulidwa awiri kapena atatu anayangʼana Yehu pansipo.
33 On reče: “Bacite je dolje.” I oni je baciše. Njena je krv poprskala zidove i konje, koji je pogaziše.
Yehu anawawuza kuti, “Muponyeni pansi!” Motero anamuponya pansi ndipo magazi ake ena anafalikira pa khoma ndi pa akavalo pamene ankamupondaponda.
34 Ušao je on, jeo i pio, a zatim naredio: “Pogledajte onu prokletnicu i sahranite je, jer je bila kraljevska kći.”
Yehu analowa mʼnyumba yaufumu ndipo anadya ndi kumwa. Kenaka iye anati, “Kamutoleni mkazi wotembereredwayo, ndipo kamuyikeni mʼmanda, popeza ndi mwana wa mfumu.”
35 I odoše da je sahrane, ali ne nađoše ništa od nje, osim lubanje, nogu i ruku.
Koma atapita kuti akamuyike mʼmanda, sanapeze kanthu kupatula chibade cha mutu wokha, mapazi ake ndi manja ake.
36 Vratiše se i javiše, a Jehu reče: “To je riječ koju je Jahve objavio preko svoga sluge Ilije Tišbijca: 'U polju jizreelskom psi će proždrijeti Izebelino tijelo.
Choncho iwo anabwerera kwa Yehu ndi kukamufotokozera kuti, “Mawu amene Yehova anayankhula kudzera mwa mtumiki wake Eliya wa ku Tisibe ndi awa: Pa munda wa ku Yezireeli agalu adzadya mtembo wa Yezebeli.
37 Izebelino truplo bit će kao gnoj u polju, da se neće moći kazati: Ovo je Izebela.'”
Mtembo wa Yezebeli udzakhala ngati zinyalala pa munda wa ku Yezireeli, kotero kuti palibe amene adzathe kunena kuti, ‘Uyu ndi Yezebeli.’”

< 2 Kraljevima 9 >