< 2 Kraljevima 15 >
1 Dvadeset i sedme godine kraljevanja Jeroboama, kralja izraelskog, postade judejskim kraljem Azarja, sin Amasjin.
Mʼchaka cha 27 cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Azariya mwana wa Amaziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Bilo mu je šesnaest godina kad se zakraljio, a kraljevao je pedeset i dvije godine u Jeruzalemu. Mati mu se zvala Jekolija, a bila je iz Jeruzalema.
Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 16 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 52. Amayi ake anali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
3 Činio je što je pravo u Jahvinim očima, sasvim kao i njegov otac Amasja.
Iyeyo anachita zabwino pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
4 Samo uzvišica nije srušio i narod je svejednako prinosio žrtve i kad na uzvišicama.
Komabe malo opembedzerako mafano sanawachotse ndipo anthu anapitirizabe kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 Ali Jahve udari kralja i ostade on gubav do smrti. Stanovao je u odvojenoj kući. Kraljev sin Jotam bio upravitelj dvora i sudio je puku zemlje.
Ndipo Yehova analanga mfumu ndi nthenda ya khate mpaka tsiku limene inamwalira. Tsono mfumuyo inkakhala mʼnyumba yakeyake yapadera. Mwana wake Yotamu ndiye amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu ndiponso ndiye amene ankalamulira anthu mʼdzikomo.
6 Ostala povijest Azarjina i sve što je učinio, zar sve to nije zapisano u knjizi Ljetopisa kraljeva judejskih?
Ntchito zina za Azariya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
7 Azarja je počinuo i sahraniše ga kraj njegovih otaca u Davidovu gradu. A na njegovo se mjesto zakralji sin mu Jotam.
Azariya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
8 Trideset i osme godine Azarjina kraljevanja u Judeji postade izraelskim kraljem u Samariji za šest mjeseci Zaharija, sin Jeroboamov.
Mʼchaka cha 38 cha Azariya mfumu ya Yuda, Zekariya mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira miyezi isanu ndi umodzi.
9 On je činio što je zlo u očima Jahvinim, kao što su činili njegovi oci; nije odstupao od grijeha Jeroboama, sina Nebatova, koji je na grijeh naveo Izraela.
Ndipo iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira makolo ake. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
10 Šalum, sin Jabešov, uroti se protiv njega; udario ga je i usmrtio u Jibleamu te se zakraljio mjesto njega.
Salumu mwana wa Yabesi anachitira chiwembu Zekariya. Anamukantha anthu akuona, namupha, ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
11 Ostala povijest Zaharijina zapisana je u knjizi Ljetopisa izraelskih kraljeva.
Ntchito zina za Zekariya, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
12 Ispunila se riječ koju je Jahve rekao Jehuu: “Tvoji će sinovi sjediti na prijestolju Izraela sve do četvrtog koljena.” I tako je bilo.
Awa ndiwo mawu a Yehova amene anayankhula kwa Yehu kuti, “Ana ako adzalamulira Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
13 Šalum, sin Jabešov, postade kraljem trideset i devete godine kraljevanja Uzije, judejskog kralja, i kraljevao je mjesec dana u Samariji.
Salumu mwana wa Yabesi anakhala mfumu mʼchaka cha 39 cha ulamuliro wa Uziya mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Samariya mwezi umodzi.
14 Menahem, sin Gadijev, ode iz Tirse, uđe u Samariju te udari Šaluma, sina Jabešova, usmrti ga i zakralji se mjesto njega.
Ndipo Menahemu mwana wa Gadi anachoka ku Tiriza napita ku Samariya nakantha Salumu mwana wa Yabesi ku Samariya, namupha ndipo iye analowa ufumu mʼmalo mwake.
15 Ostala povijest Šalumova i urota koju je skovao, sve je zapisano u knjizi Ljetopisa kraljeva izraelskih.
Ntchito zina za Salumu ndiponso za chiwembu chimene anachita, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
16 Tada je Menahem razorio Tifnah i sve što je u njem bilo i njegovo područje od Tirse jer mu nisu otvorili vrata. Razorio ga je i rasporio sve trudnice u njemu.
Nthawi imeneyo Menahemu, kuchokera ku Tiriza, anakathira nkhondo mzinda wa Tipisa ndi anthu onse amene anali mʼmenemo ndi dera lonse lozungulira chifukwa iwo anakana kutsekula zipata zawo. Iye anatenga katundu yense mu mzinda wa Tipisa ndi kutumbula akazi onse oyembekezera.
17 Trideset i devete godine kraljevanja Azarje u Judeji postade Menahem, sin Gadijev, kraljem Izraela. Kraljevao je deset godina u Samariji.
Mʼchaka cha 39 cha Azariya mfumu ya Yuda, Menahemu mwana wa Gadi anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira mu Samariya zaka khumi.
18 Činio je što je zlo u očima Jahvinim; nije odstupao od grijeha Jeroboama, sina Nebatova, koji je zaveo Izraela. U njegovo vrijeme
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Nthawi yonse ya ulamuliro wake sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
19 Pul, kralj Asirije, osvoji zemlju. Menahem dade Pulu tisuću talenata srebra da mu pomogne učvrstiti kraljevsku vlast u njegovim rukama.
Tsono Puli mfumu ya ku Asiriya inadzathira nkhondo dzikolo ndipo Menahemu anapatsa Puliyo makilogalamu 34,000 a siliva kuti amuthandize ndi kulimbikitsa ufumu wake.
20 Menahem ubra taj novac od Izraela, od svih imućnih ljudi, da bi ga mogao dati asirskom kralju. Po osobi je bilo pedeset šekela srebra. Tako se asirski kralj vratio i nije ondje ostao u zemlji.
Menahemu anapeza ndalamazo kudzera mu msonkho umene ankakhometsa Aisraeli. Munthu aliyense wachuma ankapereka masekeli a siliva makumi asanu kwa mfumu ya ku Asiriya. Choncho mfumu ya ku Asiriya inabwerera ndipo sinakhalenso mʼdzikomo.
21 Ostala povijest Menahema i sve što je učinio, zar sve to nije zapisano u knjizi Ljetopisa kraljeva izraelskih?
Ntchito zina za Menahemu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
22 Menahem je počinuo sa svojim ocima, a sin njegov Pekahja zakralji se na njegovo mjesto.
Menahemu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Pekahiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
23 Pedesete godine kraljevanja judejskog kralja Azarje postade kraljem izraelskim u Samariji Pekahja, sin Menahemov. Kraljevao je dvije godine.
Mʼchaka cha makumi asanu a Azariya mfumu ya Yuda, Pekahiya mwana wa Menahemu anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka ziwiri.
24 On je činio što je zlo u očima Jahvinim; nije odstupao od grijeha Jeroboama, sina Nebatova, koji je zaveo Izraela.
Pekahiya anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, omwe anachimwitsa nawo Israeli.
25 Njegov dvoranin Pekah, sin Remalijin, uroti se protiv njega i ubi ga u Samariji, u kuli kraljevskog dvora, s Argobom i Arjeom. Imao je sa sobom pedeset ljudi iz Gileada. Ubio je kralja i zakraljio se mjesto njega.
Ndipo Peka mwana wa Remaliya, mtsogoleri wake wa ankhondo, anamuchita chiwembu. Iye pamodzi ndi anthu makumi asanu a ku Giliyadi anapha Pekahiya pamodzi ndi Arigobu ndi Ariyeli mʼchipinda choteteza nyumba ya mfumu mu Samariya. Kotero Peka anapha Pekahiya ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
26 Ostala povijest Pekahje i sve što je učinio, sve je to zapisano u knjizi Ljetopisa izraelskih kraljeva.
Ntchito zina za Pekahiya ndi zonse zimene anachita zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
27 Pedeset i druge godine kraljevanja Azarje, judejskoga kralja, postade kraljem u Samariji Pekah, sin Remalijin. Kraljevao je dvadeset godina.
Mʼchaka cha 52 cha Azariya mfumu ya Yuda, Peka mwana wa Remaliya anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira zaka makumi awiri.
28 On je činio što je zlo u očima Jahvinim; nije odstupao od grijeha Jeroboama, sina Nebatova, koji je zaveo Izraela.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
29 U vrijeme izraelskog kralja Pekaha došao je asirski kralj Tiglat Pileser i zauzeo Ijon, Abel Bet Maaku, Janoah, Kedeš, Hasor, Gilead, Galileju i svu zemlju Naftalijevu. I odveo je stanovništvo u Asiriju.
Nthawi ya Peka mfumu ya Israeli, Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kudzalanda Iyoni, Abeli-Beti-Maaka, Yanowa, Kedesi ndi Hazori. Mfumu ya ku Asiriya inatenga Giliyadi ndi Galileya, kuphatikizanso madera onse a Nafutali ndipo anatumiza Aisraeli ku Asiriya.
30 Hošea, sin Elin, uroti se protiv Pekaha, sina Remalijina, ubi ga i zakralji mjesto njega dvadesete godine Jotama, sina Uzijina.
Kenaka Hoseya mwana wa Ela anachitira chiwembu Peka mwana wa Remaliya. Anamukantha ndi kumupha ndipo anakhala mfumu mʼmalo mwake mʼchaka makumi awiri cha Yotamu mwana wa Uziya.
31 Ostala povijest Pekahova, sve što je učinio, sve je to zapisano u knjizi Ljetopisa izraelskih kraljeva.
Ntchito zina za Peka ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
32 Druge godine kraljevanja Pekaha, sina Remalijina, nad Izraelom, postade judejskim kraljem Jotam, sin Uzijin.
Mʼchaka chachiwiri cha Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli, Yotamu mwana wa Uziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
33 Bilo mu je dvadeset i pet godina kad se zakraljio, a kraljevao je šesnaest godina u Jeruzalemu. Materi mu bješe ime Jeruša, Sadokova kći.
Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Amayi ake anali Yerusa mwana wa Zadoki.
34 Činio je što je pravo u Jahvinim očima, sasvim kao i otac mu Uzija.
Iye anachita zabwino pamaso pa Yehova monga anachitira Uziya abambo ake.
35 Ali ni on nije srušio uzvišica; narod je svejednako prinosio žrtve i kad na uzvišicama. On je sagradio Gornja vrata na Domu Jahvinu.
Komabe malo opembedzera mafano sanawachotse ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
36 Ostala povijest Jotama i sve što je učinio, zar to nije sve zapisano u knjizi Ljetopisa judejskih kraljeva?
Ntchito zina za Yotamu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
37 U njegove je dane Jahve počeo slati protiv Judeje aramejskog kralja Resina i Pekaha, sina Remalijina.
(Nthawi imeneyo, Yehova anayamba kumatuma Rezini mfumu ya Aaramu ndi Peka mwana wa Remaliya kudzamenyana ndi Yuda).
38 Tada Jotam počinu kod otaca i sahraniše ga u gradu njegova praoca Davida. A na njegovo se mjesto zakralji sin mu Ahaz.
Yotamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Ahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.