< 2 Ljetopisa 10 >

1 Tada Roboam ode u Šekem, jer su u Šekem došli svi Izraelci da ga zakralje.
Rehobowamu anapita ku Sekemu, pakuti Aisraeli onse anapita kumeneko kuti akamulonge ufumu.
2 Čim to ču Nebatov sin Jeroboam - koji je bio u Egiptu kamo bijaše pobjegao pred kraljem Salomonom - vrati se iz Egipta,
Yeroboamu mwana wa Nebati atamva zimenezi (Iye anali ku Igupto, kumene anapita pothawa mfumu Solomoni) anabwerako kuchokera ku Igupto.
3 jer bijahu poslali po nj i dozvali ga. Kad dođoše Jeroboam i sav zbor Izraelov, rekoše Roboamu:
Kotero anthu anakayitana Yeroboamu ndipo iye ndi Aisraeli onse anapita kwa Rehobowamu ndi kumuwuza kuti,
4 “Tvoj nam je otac nametnuo težak jaram, ti nam sada olakšaj tešku službu svoga oca i teški jaram koji metnu na nas, pa ćemo ti služiti.”
“Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma tsopano mutipeputsire ntchito yolemetsayi ndi goli lolemerali limene analiyika pa ife ndipo ifeyo tidzakutumikirani.”
5 On im odgovori: “Za tri dana dođite opet k meni.” I narod ode.
Rehobowamu anayankha kuti, “Mukabwerenso pakapita masiku atatu.” Choncho anthuwo anachoka.
6 Tada se kralj Roboam posavjetova sa starcima koji su služili njegovu ocu Salomonu dok je bio živ i upita ih: “Što savjetujete da odgovorim ovome narodu?”
Kenaka mfumu Rehobowamu anafunsira nzeru kwa akuluakulu amene ankatumikira abambo ake, Solomoni, pamene anali moyo. Iye anafunsa kuti, “Kodi inu mungandilangize zotani kuti ndiwayankhe anthu awa?”
7 A oni mu odgovoriše: “Ako udovoljiš tim ljudima, budeš im blagonaklon i odgovoriš im lijepim riječima, oni će ti uvijek biti sluge.”
Iwo anayankha kuti, “Ngati inu muwakomera mtima anthu awa ndi kuwasangalatsa ndiponso kuwayankha mawu abwino, iwo adzakutumikirani nthawi zonse.”
8 Ali on odbaci savjet što mu ga dadoše starci i posavjetova se s mladićima koji su odrasli s njim i bili mu u službi.
Koma Rehobowamu anakana malangizo amene akuluakulu anamupatsa ndipo anakafunsira nzeru kwa anyamata amene anakula naye pamodzi komanso amamutumikira.
9 Upita ih: “Što savjetujete da odgovorim ovomu narodu koji mi reče: 'Olakšaj jaram što nam ga nametnu tvoj otac!'”
Iye anawafunsa kuti, “Kodi malangizo anu ndi otani? Kodi tiwayankhe chiyani anthu amene akunena kuti, ‘Peputsani goli limene abambo anu anayika pa ife?’”
10 Odgovoriše mu mladići koji bijahu s njim odrasli: “Narodu koji ti je rekao 'Tvoj nam je otac nametnuo jaram, a ti nam ga olakšaj', odvrati ovako: 'Moj je mali prst deblji od bedara moga oca!
Anyamata amene anakula pamodzi naye anamuyankha kuti, “Anthu amene anena kwa inu kuti, ‘Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma inu mupeputse goli lathu,’ muwawuze kuti, ‘Chala changa chachingʼono ndi chachikulu kuposa chiwuno cha abambo anga.
11 Dakle, moj vam je otac nametnuo težak jaram, a ja ću još otežati vaš jaram; moj vas je otac šibao bičevima, a ja ću vas šibati bičevima sa željeznim štipavcima.'”
Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.’”
12 Trećega dana dođe Jeroboam i sav narod k Roboamu, jer im kralj bijaše naredio: “Vratite se k meni trećega dana.”
Tsiku lachitatu Yeroboamu ndi anthu onse anabwerera kwa Rehobowamu monga ananenera mfumu kuti, “Mukabwerenso kwa ine pakapita masiku atatu.”
13 Kralj im oštro odgovori; odbacivši savjet starijih,
Mfumu inawayankha mwankhanza, pokana malangizo a akuluakulu aja.
14 odvrati po savjetu mladih: “Moj je otac otežao vaš jaram, a ja ću još dometnuti na nj; moj vas je otac šibao bičevima, a ja ću vas šibati bičevima sa željeznim štipavcima.”
Iye anatsatira malangizo a anyamata ndipo anati, “Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.”
15 Kralj, dakle, ne htjede poslušati naroda, jer tako upriliči Bog da se ispuni riječ što je preko Šilonjanina Ahije kaza Nabatovu sinu Jeroboamu.
Kotero mfumu sinamvere anthuwo, pakuti zinthu izi zinali zochokera kwa Mulungu, kukwaniritsa mawu amene Yehova ananena kwa Yeroboamu mwana wa Nebati kudzera mwa Ahiya wa ku Silo.
16 Kad Izraelci vidješe gdje se kralj oglušio, odgovori mu narod: “Kakav dio mi imamo s Davidom? Mi nemamo baštine s Jišajevim sinom! U šatore, Izraele! Sad se, Davide, brini za svoj dom!” I sav Izrael ode pod svoje šatore.
Aisraeli onse ataona kuti mfumu yakana kuwamvera, iwo anayankha mfumu kuti, “Kodi ife tili ndi gawo lanji mwa Davide, gawo lanji mwa mwana wa Yese? Inu Aisraeli! Pitani kwanu. Iwe Davide! Yangʼana banja lako.” Kotero Aisraeli onse anapita kwawo.
17 Roboam zavlada samo nad Izraelovim sinovima koji su živjeli po judejskim gradovima.
Koma Rehobowamu anakhala akulamulirabe Aisraeli amene amakhala mʼmizinda ya Yuda.
18 Potom kralj Roboam posla Adorama, nadstojnika za tlaku, ali ga Izraelci kamenovaše i on umrije; a kralj se Roboam brže-bolje pope na kola te pobježe u Jeruzalem.
Mfumu Rehobowamu inatuma Hadoramu amene ankayangʼanira ntchito yathangata, koma Aisraeli anamugenda miyala ndi kumupha. Koma mfumu Rehobowamu anakwera galeta lake ndi kuthawira ku Yerusalemu.
19 Tako se Izrael odijelio od doma Davidova sve do danas.
Motero Israeli wakhala akuwukira banja la Davide mpaka lero lino.

< 2 Ljetopisa 10 >