< 1 Solunjanima 5 >
1 A o vremenima i trenucima nije, braćo, potrebno pisati vam.
Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni,
2 Ta i sami dobro znate da Dan Gospodnji dolazi baš kao kradljivac u noći.
chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku.
3 Dok još budu govorili: “Mir i sigurnost”, zadesit će ih iznenadna propast kao trudovi trudnicu i neće umaći.
Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.
4 Ali vi, braćo, niste u tami, da bi vas Dan mogao zaskočiti kao kradljivac:
Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala.
5 ta svi ste vi sinovi svjetlosti i sinovi dana. Nismo doista od noći ni od tame.
Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima.
6 Onda i ne spavajmo kao ostali, nego bdijmo i trijezni budimo.
Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga.
7 Jer koji spavaju, noću spavaju; i koji se opijaju, noću se opijaju.
Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku.
8 A mi koji smo od dana, budimo trijezni, obucimo oklop vjere i ljubavi i stavimo kacigu, nadu spasenja!
Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa.
9 Ta Bog nas nije odredio za gnjev, nego da imamo spasenje po Gospodinu našem Isusu Kristu,
Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
10 koji je za nas umro da - bdjeli ili spavali - zajedno s njime živimo.
Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi.
11 Zato, tješite se uzajamno i izgrađujte jedan drugoga, kako i činite.
Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.
12 Molimo vas, braćo: priznajte one koji se trude među vama, koji su vam predstojnici u Gospodinu i opominju vas;
Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani.
13 s ljubavlju ih nadasve cijenite poradi njihova djela! Gajite mir među sobom!
Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.
14 Potičemo vas, braćo: opominjite neuredne, sokolite malodušne, podržavajte slabe, budite velikodušni prema svima!
Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense.
15 Pazite da tko komu zlo zlom ne uzvrati, nego uvijek promičite dobro jedni prema drugima i prema svima.
Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.
17 Bez prestanka se molite!
Pempherani kosalekeza.
18 U svemu zahvaljujte! Jer to je za vas volja Božja u Kristu Isusu.
Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.
Musazimitse moto wa Mzimu Woyera.
20 proroštava ne prezirite!
Musanyoze mawu a uneneri.
21 Sve provjeravajte: dobro zadržite,
Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino.
22 svake se sjene zla klonite!
Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.
23 A sam Bog mira neka vas posvema posveti i cijelo vaše biće - duh vaš i duša i tijelo - neka se besprijekornim, savršenim sačuva za Dolazak Gospodina našega Isusa Krista.
Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu.
24 Vjeran je Onaj tko vas poziva: on će to i učiniti.
Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.
25 Braćo, molite i za nas!
Abale, mutipempherere.
26 Pozdravite svu braću cjelovom svetim.
Perekani moni wachikondi kwa onse.
27 Zaklinjem vas u Gospodinu: neka se ova poslanica pročita svoj braći.
Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.
28 Milost Gospodina našega Isusa Krista s vama!
Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.