< 1 Samuelova 6 >
1 Kovčeg Jahvin bijaše sedam mjeseci u zemlji Filistejaca.
Bokosi la Yehova linakhala mʼdziko la Afilisti kwa miyezi isanu ndi iwiri.
2 Tada Filistejci sazvaše svećenike i vrače i zapitaše ih: “Što da radimo s Kovčegom Jahvinim? Poučite nas kako da ga pošaljemo natrag na njegovo mjesto.”
Tsono Afilisti anayitana ansembe ndi amawula ndipo anati, “Tichite nalo chiyani Bokosi la Yehova? Tiwuzeni momwe tidzalitumizira ku malo ake.”
3 Oni odgovoriše: “Ako hoćete vratiti Kovčeg Boga Izraelova, ne šaljite ga natrag prazna nego uza nj pošaljite i naknadnicu. Tada ćete se izliječiti i znat ćete zašto se njegova ruka nije okrenula od vas.”
Iwo anayankha kuti, “Ngati mufuna kubweza Bokosi la Mulungu wa Israeli, musalitumize wopanda kanthu, koma muyesetse kulitumiza pamodzi ndi nsembe yopepesera machimo. Mukatero mudzachiritsidwa, ndipo mudzadziwa chifukwa chiyani chilango cha Yehova sichikukuchokani.”
4 Oni zapitaše: “Kakvu naknadnicu treba da mu pošaljemo?” Oni odgovoriše: “Prema broju filistejskih knezova, pet zlatnih čireva i pet zlatnih štakora, jer je ista nevolja na vama i na vašim knezovima.
Afilisti anafunsanso kuti “Kodi ife tipereke nsembe yanji yopepesera machimo?” Iwo anayankha kuti, “Mupereke zifanizo zagolide za zithupsa zisanu ndi zamakoswe asanu malingana ndi chiwerengero cha akalonga a Afilisti popeza mliri womwewo wagwera inu ndi akalonga anu.
5 Načinite, dakle, likove svojih čireva i likove svojh štakora, koji vam zatiru zemlju, i dajte slavu Bogu Izraelovu. Možda će dignuti ruku svoju od vas, od vaših bogova i od vaše zemlje.
Mupange zifanizo za zithupsa zisanu ndi za makoswe asanu amene akuwononga dziko lanu ndipo mupereke ulemu kwa Israeli. Mwina adzaleka kuzunza inu, milungu yanu ndi dziko lanu.
6 Zašto hoćete da vam srce otvrdne kao što je bilo otvrdnulo Egipćanima i faraonu? Kad ih je Bog pritisnuo, nisu li ih onda pustili da odu?
Nʼchifukwa chiyani mukuwumitsa mitima monga anachita Aigupto ndi Farao? Mulungu atawalanga anthu a ku Igupto aja kodi suja anawalola Aisraeli kuti azipita ndipo anapitadi?
7 Pripremite sada jedna nova kola i uzmite dvije krave dojilice koje još nisu nosile jarma: upregnite krave u kola, a njihovu telad odvedite natrag u staju.
“Tsopano konzani galeta latsopano limodzi ndiponso ngʼombe ziwiri zazikazi zamkaka zimene sizinavalepo goli. Muzimangirire ngʼombezo ku ngoloyo, koma ana awo muwachotse ndi kuwasiya kwanu.
8 Tada ćete uzeti Kovčeg Jahvin i staviti ga na kola. Zlatne predmete koje mu prinosite kao žrtvu naknadnicu stavit ćete u kovčežić kraj njega i tako neka pođe.
Mutenge Bokosi la Yehova ndi kuliyika pa galetapo ndipo pambali pake pakhale Bokosi, mʼmene muyikemonso zinthu zagolide zomwe mukutumiza kwa Iye monga nsembe yopepesera machimo. Kenaka, mulisiye lizipita.
9 Zatim gledajte: ako krene prema svome kraju, put Bet Šemeša, onda je sigurno da nam je on zadao ovo veliko zlo; ako li ne krene tako, znat ćemo da nas nije udarila njegova ruka, nego da nam se to dogodilo slučajno.”
Koma muziliyangʼana. Ngati lilondola njira yopita kwawo kwa Bokosilo mpaka ku Beti-Semesi ndiye kuti amene watichita zoyipa zazikulu zoterezi ndi Mulungu wa Israeli. Koma ngati silitero, ife tidzadziwa kuti sanali Mulungu wa Israeli amene watizunza koma kuti zinangochitika mwatsoka.”
10 Ljudi učiniše tako: uzeše dvije krave dojilice i upregoše ih u kola, a njihovu telad zadržaše u staji.
Anthu aja anachitadi zimenezi. Anatenga ngʼombe zamkaka ziwiri nazimanga ku galeta lija. Koma ana awo anawatsekera mʼkhola.
11 Kovčeg Jahvin staviše na kola i kovčežić sa zlatnim štakorima i s likovima svojih čireva.
Tsono anayika Bokosi la Yehova pa galeta pamodzi ndi bokosi limene munali makoswe agolide ndi zifanizo zawo za zithupsa.
12 Krave udariše ravno cestom prema Bet Šemešu i jednako su išle istim putem, mukale su idući, a nisu skretale ni desno ni lijevo. Filistejski knezovi pratili su ih do granice Bet Šemeša.
Ngʼombe zija zinapita molunjika kutsata msewu wopita ku Beti Semesi zikulira njira yonse. Sizinakhotere kumanja kapena kumanzere. Akalonga a Afilisti anazitsatira mpaka mʼmalire a Beti-Semesi.
13 Stanovnici Bet Šemeša upravo su bili zabavljeni žetvom pšenice u dolini. Digavši oči, ugledaše Kovčeg i potrčaše mu s veseljem u susret.
Nthawi imeneyi anthu a ku Beti-Semesi amakolola tirigu mʼchigwa ndipo pamene anayangʼana ndi kuona Bokosi la Chipangano likubwera anakondwa.
14 Kad su kola stigla na polje Jošue iz Bet Šemeša, zaustaviše se. Ondje bijaše velik kamen. Tada iscijepaše drvo od kola i prinesoše krave kao žrtvu paljenicu Jahvi.
Galeta lija linafika ku munda wa Yoswa ku Beti-Semesi ndipo linayima. Kumeneko kunali mwala waukulu. Tsono anthu anawaza nkhuni galetalo, ndipo anapha ngʼombe zija ndi kuzipereka ngati nsembe zopsereza kwa Yehova.
15 Leviti bijahu skinuli Kovčeg Jahvin i kovčežić što je bio kraj njega i u kojem su bili zlatni predmeti i sve bijahu stavili na onaj veliki kamen. Stanovnici Bet Šemeša prinosili su toga dana žrtve paljenice i klali žrtve klanice Jahvi.
Alevi nʼkuti atatsitsa Bokosi la Yehova, pamodzi ndi bokosi mmene munali zinthu zagolide, ndipo anawayika pa mwala uja waukulu. Tsiku limenelo anthu a ku Beti-Semesi anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Yehova.
16 Kad je to vidjelo pet filistejskih knezova, vratiše se u Ekron isti dan.
Atsogoleri asanu a Afilisti ataona izi anabwerera ku Ekroni tsiku lomwelo.
17 A ovo je pet zlatnih čireva što su ih Filistejci poslali kao žrtvu naknadnicu Jahvi: za Ašdod jedan, za Gazu jedan, za Aškelon jedan, za Gat jedan, za Ekron jedan.
Zifanizo zagolide za zithupsa zimene Afilisti anatumiza ngati nsembe zopepesera machimo kwa Yehova zinkayimirira mizinda isanu iyi motere: chimodzi cha ku Asidodi, china cha ku Gaza ndi zina za ku Asikeloni, Gati ndi Ekroni.
18 A zlatnih je štakora bilo toliko koliko svih gradova filistejskih, u svih pet kneževina, od utvrđenih gradova do otvorenih sela. Svjedok je veliki kamen na koji su položili Kovčeg Jahvin i koji još i danas stoji na polju Jošue iz Bet Šemeša.
Ndipo chiwerengero cha zifanizo za makoswe chinali chofanana ndi chiwerengero cha mizinda ya akalonga asanu a Afilisti. Mizindayi inali yotetezedwa bwino ndi ina yapamtetete. Mwala waukulu umene anayikapo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼmunda mwa Yoswa ku Beti-Semesi uli ngati mboni mpaka lero.
19 Sinovi Jekonijini nisu se radovali sa stanovnicima Bet Šemeša kad su vidjeli Kovčeg Jahvin. Zato je Jahve pobio sedamdeset ljudi među njima. Narod je tugovao zbog toga što ga je Jahve tako teško iskušao.
Yehova anakantha amuna a ku Beti-Semesi 70 chifukwa anasuzumira mʼBokosi la Chipangano cha Yehova. Ndipo anzawo analira chifukwa Yehova anawalanga kwambiri.
20 Tada ljudi u Bet Šemešu rekoše: “Tko bi mogao opstati pred Jahvom, ovim Svetim Bogom? Kome će otići sada od nas?”
Tsono anthu a ku Beti-Semesi anafunsa, “Ndani angathe kuyima pamaso pa Yehova Mulungu Woyera? Bokosi la Chipanganoli lipita kuti likachoka pano?”
21 I poslaše poslanike stanovnicima Kirjat Jearima i poručiše im: “Filistejci su vratili Kovčeg Jahvin. Dođite i odnesite ga sebi.”
Tsono iwo anatumiza a mithenga kwa anthu a ku Kiriati-Yearimu kuti, “Afilisti atibwezera Bokosi la Yehova. Bwerani kuno mudzalitenge, mupite nalo kwanuko.”