< ⲚⲒⲢⲰⳘⲈⲞⲤ 3 >
1 ⲁ̅ ⲟⲩ ϭⲉ ⲡⲉ ⲡⲉϩⲟⲩⲟ ⲙⲡⲓⲟⲩⲇⲁⲓ ⲏ ⲟⲩ ⲡⲉ ⲡϩⲏⲩ ⲙⲡⲥⲃⲃⲉ
Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe?
2 ⲃ̅ ⲛⲁϣⲱⲥ ⲕⲁⲧⲁⲥⲙⲟⲧ ⲛⲓⲙ ⲛϣⲟⲣⲡ ⲅⲁⲣ ⲛⲉⲛⲧⲁⲛϩⲟⲩⲧⲟⲩ ⲉⲛϣⲁϫⲉ ⲙⲡⲛⲟⲩⲧⲉ
Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.
3 ⲅ̅ ⲉϣⲁⲣⲉ ⲟⲩ ⲅⲁⲣ ϣⲱⲡⲉ ⲉϣϫⲉ ⲁϩⲟⲓⲛⲉ ⲣⲁⲧⲛⲁϩⲧⲉ ⲙⲏ ⲉⲣⲉⲧⲉⲩⲙⲛⲧⲁⲧⲛⲁϩⲧⲉ ⲛⲁⲕⲁⲧⲁⲣⲅⲓ ⲛⲧⲡⲓⲥⲧⲓⲥ ⲙⲡⲛⲟⲩⲧⲉ
Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu?
4 ⲇ̅ ⲛⲛⲉⲥϣⲱⲡⲉ ⲙⲁⲣⲉ ⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲇⲉ ϣⲱⲡⲉ ⲙⲙⲉ ⲛⲧⲉ ⲣⲱⲙⲉ ⲛⲓⲙ ϣⲱⲡⲉ ⲛϭⲟⲗ ⲕⲁⲧⲁ ⲑⲉ ⲉⲧⲥⲏϩ ϫⲉ ϫⲉⲕⲁⲥ ⲉⲕⲉⲧⲙⲁⲓⲟ ϩⲛ ⲛⲉⲕϣⲁϫⲉ ⲛⲅϫⲣⲟ ϩⲙ ⲡⲧⲣⲉⲕϯ ϩⲁⲡ ⲉⲣⲟⲓ
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti, “Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi kupambana pamene muweruza.”
5 ⲉ̅ ⲉϣϫⲉ ⲡⲉⲛϫⲓ ⲛϭⲟⲛⲥ ⲇⲉ ⲡⲉⲧⲛⲁⲥⲩⲛϩⲓⲥⲧⲁ ⲛⲧⲇⲓⲕⲁⲓⲟⲥⲩⲛⲏ ⲙⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲟⲩ ⲡⲉⲧⲛⲛⲁϫⲟⲟϥ ⲙⲏ ⲉⲓϫⲱ ⲙⲙⲟⲥ ϫⲉ ⲟⲩⲁⲇⲓⲕⲟⲥ ⲡⲉ ⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲉⲧⲉⲓⲛⲉ ⲛⲧⲉϥⲟⲣⲅⲏ ⲉϫⲛ ⲛⲣⲱⲙⲉ
Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira).
6 ⲋ̅ ⲛⲛⲉⲥϣⲱⲡⲉ ⲉⲙⲙⲟⲛ ⲉⲣⲉⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲛⲁⲕⲣⲓⲛⲉ ⲙⲡⲕⲟⲥⲙⲟⲥ ⲛⲁϣ ⲛϩⲉ
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi?
7 ⲍ̅ ⲉϣϫⲉ ⲛⲧⲁⲧⲙⲉ ⲅⲁⲣ ⲙⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲣϩⲟⲩⲟ ϩⲛ ⲧⲁϭⲟⲗ ⲉⲡⲉϥⲉⲟⲟⲩ ⲁϩⲣⲟⲓ ϭⲉ ⲥⲉⲕⲣⲓⲛⲉ ⲙⲙⲟⲓ ϩⲱⲥ ⲣⲉϥⲣⲛⲟⲃⲉ
Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?”
8 ⲏ̅ ⲁⲩⲱ ⲉⲛⲕⲁⲧⲁ ⲑⲉ ⲁⲛ ⲉⲧⲟⲩϫⲓⲟⲩⲁ ⲉⲣⲟⲛ ⲛⲑⲉ ⲉⲧⲉⲣⲉϩⲟⲓⲛⲉ ϫⲱ ⲙⲙⲟⲥ ϫⲉ ϣⲁⲛϫⲟⲟⲥ ϫⲉ ⲙⲁⲣⲛⲉⲓⲣⲉ ⲛⲙ ⲡⲉⲑⲟⲟⲩ ϫⲉ ⲉⲣⲉⲙⲡⲉⲧⲛⲁⲛⲟⲩϥ ⲧⲁϩⲟⲛ ⲛⲁⲓ ⲉⲩⲙⲉ ⲡⲉ ⲡⲉⲩϩⲁⲡ
Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.
9 ⲑ̅ ⲟⲩ ϭⲉ ⲡⲉ ⲉⲩⲟ ⲛϣⲟⲣⲡ ⲉⲣⲟⲛ ⲙⲙⲟⲛ ϫⲓⲛ ⲛϣⲟⲣⲡ ⲅⲁⲣ ⲁⲛϭⲛⲁⲣⲓⲕⲉ ⲉⲛⲓⲟⲩⲇⲁⲓ ⲙⲛ ⲛⲟⲩⲉⲓⲉⲛⲓⲛ ϫⲉ ⲥⲉϩⲁⲡ ⲛⲟⲃⲉ ⲧⲏⲣⲟⲩ
Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa.
10 ⲓ̅ ⲕⲁⲧⲁ ⲑⲉ ⲉⲧⲥⲏϩ ϫⲉ ⲙⲛ ⲇⲓⲕⲁⲓⲟⲥ ⲗⲁⲁⲩ ⲙⲛ ⲟⲩⲁ
Monga kwalembedwa kuti, “Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.
11 ⲓ̅ⲁ̅ ⲙⲛ ⲣⲙⲛϩⲏⲧ ⲙⲛ ⲡⲉⲧϣⲓⲛⲉ ⲛⲥⲁ ⲡⲛⲟⲩⲧⲉ
Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira, palibe amene amafunafuna Mulungu.
12 ⲓ̅ⲃ̅ ⲁⲩⲣⲓⲕⲉ ⲉⲃⲟⲗ ⲧⲏⲣⲟⲩ ⲁⲩⲣⲁⲧϣⲁⲩ ϩⲓⲟⲩⲥⲟⲡ ⲙⲛ ⲡⲉⲧⲉⲓⲣⲉ ⲛⲟⲩⲙⲛⲧⲭⲣⲏⲥⲧⲟⲥ ⲙⲛ ⲟⲩⲟⲛ ϣⲁϩⲣⲁⲓ ⲉⲟⲩⲁ
Onse apatukira kumbali, onse pamodzi asanduka opandapake. Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino, palibe ngakhale mmodzi.”
13 ⲓ̅ⲅ̅ ⲟⲩⲧⲁⲫⲟⲥ ⲉϥⲟⲩⲏⲛ ⲧⲉ ⲧⲉⲩϣⲟⲩⲱⲃⲉ ⲁⲩⲣⲕⲣⲟϥ ϩⲛ ⲛⲉⲩⲗⲁⲥ ⲟⲩⲙⲁⲧⲟⲩ ⲛϩⲟϥ ⲧⲉⲧϩⲁⲛⲉⲩⲥⲡⲟⲧⲟⲩ
“Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.” “Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”
14 ⲓ̅ⲇ̅ ⲛⲁⲓ ⲉⲣⲉⲧⲉⲩⲧⲁⲡⲣⲟ ⲙⲉϩ ⲛⲥⲁϩⲟⲩ ϩⲓ ⲥⲓϣⲉ
“Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”
15 ⲓ̅ⲉ̅ ⲛⲉⲩⲟⲩⲉⲣⲏⲧⲉ ϭⲉⲡⲏ ⲉⲡⲛⲥⲛⲟϥ ⲉⲃⲟⲗ
“Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.
16 ⲓ̅ⲋ̅ ⲟⲩⲟⲩⲱϣϥ ⲙⲛ ⲟⲩⲧⲁⲗⲁⲓⲡⲱⲣⲓⲁ ⲛⲉⲧϣⲟⲟⲡ ϩⲛ ⲛⲉⲩϩⲓⲟⲟⲩⲉ
Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,
17 ⲓ̅ⲍ̅ ⲧⲉϩⲓⲏ ⲛϯⲣⲏⲛⲏ ⲙⲡⲟⲩⲥⲟⲩⲱⲛⲥ
ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”
18 ⲓ̅ⲏ̅ ⲛⲑⲟ ⲧⲉ ⲙⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲙⲡⲉⲙⲧⲟ ⲛⲛⲉⲩⲃⲁⲗ ⲉⲃⲟⲗ ⲁⲛ
“Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”
19 ⲓ̅ⲑ̅ ⲧⲛⲥⲟⲟⲩⲛ ⲇⲉ ϫⲉ ⲛⲉⲧⲉⲣⲉ ⲡⲛⲟⲙⲟⲥ ϫⲱ ⲙⲙⲟⲟⲩ ⲉϥϫⲱ ⲙⲙⲟⲟⲩ ⲛⲛⲉⲧϩⲙ ⲡⲛⲟⲙⲟⲥ ϫⲉⲕⲁⲥ ⲉⲣⲉⲧⲁⲡⲣⲟ ⲛⲓⲙ ⲧⲱⲙ ⲛⲧⲉ ⲡⲕⲟⲥⲙⲟⲥ ⲧⲏⲣϥ ϣⲱⲡⲉ ϩⲁⲡϩⲁⲡ ⲙⲡⲛⲟⲩⲧⲉ
Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu.
20 ⲕ̅ ϫⲉ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲛ ⲛⲉϩⲃⲏⲩⲉ ⲙⲡⲛⲟⲙⲟⲥ ⲙⲛ ⲗⲁⲁⲩ ⲛⲥⲁⲣⲝ ⲛⲁⲧⲙⲁⲉⲓⲟ ⲙⲡⲉϥⲙⲧⲟ ⲉⲃⲟⲗ ⲛⲧⲁⲛⲥⲟⲩⲛ ⲡⲛⲟⲃⲉ ⲅⲁⲣ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲓⲧⲙ ⲡⲛⲟⲙⲟⲥ
Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.
21 ⲕ̅ⲁ̅ ⲧⲉⲛⲟⲩ ⲇⲉ ⲁϫⲙ ⲡⲛⲟⲙⲟⲥ ⲁⲧⲇⲓⲕⲁⲓⲟⲥⲩⲛⲏ ⲙⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲟⲩⲱⲛϩ ⲉⲃⲟⲗ ⲉⲩⲣⲙⲛⲧⲣⲉ ϩⲁⲣⲟⲥ ϩⲓⲧⲙ ⲡⲛⲟⲙⲟⲥ ⲙⲛ ⲛⲉⲡⲣⲟⲫⲏⲧⲏⲥ
Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni.
22 ⲕ̅ⲃ̅ ⲧⲇⲓⲕⲁⲓⲟⲥⲩⲛⲏ ⲇⲉ ⲙⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲓⲧⲛ ⲧⲡⲓⲥⲧⲓⲥ ⲛⲓⲏⲥ ⲡⲉⲭⲥ ⲉϩⲟⲩⲛ ⲉⲟⲩⲟⲛ ⲛⲓⲙ ⲉⲧⲡⲓⲥⲧⲉⲩⲉ ⲙⲛ ⲡⲱⲣϫ ⲅⲁⲣ ϣⲟⲟⲡ
Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina,
23 ⲕ̅ⲅ̅ ⲁⲩⲣⲛⲟⲃⲉ ⲅⲁⲣ ⲧⲏⲣⲟⲩ ⲁⲩⲱ ⲥⲉϣⲁⲁⲧ ⲙⲡⲉⲟⲟⲩ ⲙⲡⲛⲟⲩⲧⲉ
pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu
24 ⲕ̅ⲇ̅ ⲉⲩⲧⲙⲁⲉⲓⲟ ⲙⲙⲟⲟⲩ ⲛϫⲓⲛϫⲏ ϩⲛ ⲧⲉϥⲭⲁⲣⲓⲥ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲓⲧⲙ ⲡⲥⲱⲧⲉ ⲙⲡⲉⲭⲥ ⲓⲏⲥ
ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola.
25 ⲕ̅ⲉ̅ ⲡⲁⲓ ⲉⲛⲧⲁ ⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲕⲁⲁϥ ϫⲓⲛ ⲛϣⲟⲣⲡ ⲛⲕⲱ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲓⲧⲛ ⲧⲡⲓⲥⲧⲓⲥ ⲙⲡⲉϥⲥⲛⲟϥ ⲉⲡⲟⲩⲱⲛϩ ⲉⲃⲟⲗ ⲛⲧⲉϥⲇⲓⲕⲁⲓⲟⲥⲩⲛⲏ ⲉⲧⲃⲉ ⲡⲕⲱ ⲉⲃⲟⲗ ⲛⲛⲛⲟⲃⲉ ⲉⲛⲧⲁⲛⲛⲁⲁⲩ ⲛϣⲟⲣⲡ
Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale.
26 ⲕ̅ⲋ̅ ϩⲛ ⲧⲁⲛⲟⲭⲏ ⲙⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲉⲡⲟⲩⲱⲛϩ ⲉⲃⲟⲗ ⲛⲧⲉϥⲇⲓⲕⲁⲓⲟⲥⲩⲛⲏ ϩⲙ ⲡⲉⲉⲓⲟⲩⲟⲓϣ ⲧⲉⲛⲟⲩ ⲉⲧⲣⲉϥϣⲱⲡⲉ ⲛⲇⲓⲕⲁⲓⲟⲥ ⲁⲩⲱ ⲉϥⲧⲙⲁⲉⲓⲟ ⲙⲡⲉⲃⲟⲗ ϩⲛ ⲧⲡⲓⲥⲧⲓⲥ ⲛⲓⲏⲥ
Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.
27 ⲕ̅ⲍ̅ ⲉϥⲧⲱⲛ ϭⲉ ⲡϣⲟⲩϣⲟⲩ ⲁⲩϣⲧⲁⲙ ⲉⲣⲱϥ ϩⲓⲧⲛ ⲁϣ ⲛⲛⲟⲙⲟⲥ ⲡⲁ ⲛⲉϩⲃⲏⲩⲉ ⲙⲙⲟⲛ ⲁⲗⲗⲁ ϩⲓⲧⲙ ⲡⲛⲟⲙⲟⲥ ⲛⲧⲡⲓⲥⲧⲓⲥ ⲛⲓⲏⲥ
Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro.
28 ⲕ̅ⲏ̅ ⲧⲛϫⲱ ⲅⲁⲣ ⲙⲙⲟⲥ ϫⲉ ⲡⲣⲱⲙⲉ ⲛⲁⲧⲙⲁⲉⲓⲟ ϩⲛ ⲧⲡⲓⲥⲧⲓⲥ ⲛⲟⲩⲉϣ ⲛⲛⲉϩⲃⲏⲩⲉ ⲙⲡⲛⲟⲙⲟⲥ
Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo.
29 ⲕ̅ⲑ̅ ⲏ ⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲡⲁ ⲛⲓⲟⲩⲇⲁⲓ ⲙⲁⲩⲁⲁⲩ ⲡⲉ ⲙⲡⲁ ⲛⲕⲉϩⲉⲑⲛⲟⲥ ⲛⲧⲟⲟⲩ ⲁⲛ ⲡⲉ ⲉϩⲉ ⲡⲁ ⲛⲕⲉϩⲉⲑⲛⲟⲥ ⲡⲉ
Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso,
30 ⲗ̅ ⲉⲧⲃⲉ ϫⲉ ⲟⲩⲁ ⲡⲉ ⲡⲛⲟⲩⲧⲉ ⲡⲁⲓ ⲉⲧⲛⲁⲧⲙⲁⲓ ⲉⲡⲥⲃⲃⲉ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲛ ⲧⲡⲓⲥⲧⲓⲥ ⲁⲩⲱ ⲧⲙⲛⲧⲁⲅⲥⲃⲃⲉ ⲉⲃⲟⲗ ϩⲓⲧⲛ ⲧⲡⲓⲥⲧⲓⲥ
popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho.
31 ⲗ̅ⲁ̅ ⲉⲛⲛⲁⲕⲁⲧⲁⲣⲅⲉⲓ ϭⲉ ⲙⲡⲛⲟⲙⲟⲥ ϩⲓⲧⲛ ⲧⲡⲓⲥⲧⲓⲥ ⲛⲛⲉⲥϣⲱⲡⲉ ⲁⲗⲗⲁ ⲉⲛⲛⲁⲥⲩⲛϩⲓⲥⲧⲁ ⲙⲡⲛⲟⲙⲟⲥ
Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.