< 詩篇 2 >
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 世上的君王一齊起來, 臣宰一同商議, 要敵擋耶和華並他的受膏者,
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 那時,他要在怒中責備他們, 在烈怒中驚嚇他們,
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 受膏者說:我要傳聖旨。 耶和華曾對我說:你是我的兒子, 我今日生你。
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 你求我,我就將列國賜你為基業, 將地極賜你為田產。
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 你必用鐵杖打破他們; 你必將他們如同窯匠的瓦器摔碎。
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 現在,你們君王應當省悟! 你們世上的審判官該受管教!
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 當以嘴親子,恐怕他發怒, 你們便在道中滅亡, 因為他的怒氣快要發作。 凡投靠他的,都是有福的。
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.