< 箴言 13 >

1 智慧子聽父親的教訓; 褻慢人不聽責備。
Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
2 人因口所結的果子,必享美福; 奸詐人必遭強暴。
Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
3 謹守口的,得保生命; 大張嘴的,必致敗亡。
Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
4 懶惰人羨慕,卻無所得; 殷勤人必得豐裕。
Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
5 義人恨惡謊言; 惡人有臭名,且致慚愧。
Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
6 行為正直的,有公義保守; 犯罪的,被邪惡傾覆。
Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
7 假作富足的,卻一無所有; 裝作窮乏的,卻廣有財物。
Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
8 人的資財是他生命的贖價; 窮乏人卻聽不見威嚇的話。
Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
9 義人的光明亮; 惡人的燈要熄滅。
Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
10 驕傲只啟爭競; 聽勸言的,卻有智慧。
Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
11 不勞而得之財必然消耗; 勤勞積蓄的,必見加增。
Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
12 所盼望的遲延未得,令人心憂; 所願意的臨到,卻是生命樹。
Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
13 藐視訓言的,自取滅亡; 敬畏誡命的,必得善報。
Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
14 智慧人的法則是生命的泉源, 可以使人離開死亡的網羅。
Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
15 美好的聰明使人蒙恩; 奸詐人的道路崎嶇難行。
Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
16 凡通達人都憑知識行事; 愚昧人張揚自己的愚昧。
Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
17 奸惡的使者必陷在禍患裏; 忠信的使臣乃醫人的良藥。
Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
18 棄絕管教的,必致貧受辱; 領受責備的,必得尊榮。
Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
19 所欲的成就,心覺甘甜; 遠離惡事,為愚昧人所憎惡。
Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
20 與智慧人同行的,必得智慧; 和愚昧人作伴的,必受虧損。
Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
21 禍患追趕罪人; 義人必得善報。
Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
22 善人給子孫遺留產業; 罪人為義人積存資財。
Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
23 窮人耕種多得糧食, 但因不義,有消滅的。
Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
24 不忍用杖打兒子的,是恨惡他; 疼愛兒子的,隨時管教。
Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
25 義人吃得飽足; 惡人肚腹缺糧。
Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.

< 箴言 13 >