< 約拿書 2 >

1 約拿在魚腹中禱告耶和華-他的上帝,
Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
2 說: 我遭遇患難求告耶和華, 你就應允我; 從陰間的深處呼求, 你就俯聽我的聲音。 (Sheol h7585)
Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol h7585)
3 你將我投下深淵, 就是海的深處; 大水環繞我, 你的波浪洪濤都漫過我身。
Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
4 我說:我從你眼前雖被驅逐, 我仍要仰望你的聖殿。
Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
5 諸水環繞我,幾乎淹沒我; 深淵圍住我; 海草纏繞我的頭。
Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
6 我下到山根, 地的門將我永遠關住。 耶和華-我的上帝啊, 你卻將我的性命從坑中救出來。
Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
7 我心在我裏面發昏的時候, 我就想念耶和華。 我的禱告進入你的聖殿, 達到你的面前。
“Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
8 那信奉虛無之神的人, 離棄憐愛他們的主;
“Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
9 但我必用感謝的聲音獻祭與你。 我所許的願,我必償還。 救恩出於耶和華。
Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
10 耶和華吩咐魚,魚就把約拿吐在旱地上。
Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.

< 約拿書 2 >