< 約伯記 33 >
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 我的言語要發明心中所存的正直; 我所知道的,我嘴唇要誠實地說出。
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 我是清潔無過的,我是無辜的; 在我裏面也沒有罪孽。
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 我要回答你說:你這話無理, 因上帝比世人更大。
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 人躺在床上沉睡的時候, 上帝就用夢和夜間的異象,
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 開通他們的耳朵, 將當受的教訓印在他們心上,
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 他的肉消瘦,不得再見; 先前不見的骨頭都凸出來。
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 一千天使中, 若有一個作傳話的與上帝同在, 指示人所當行的事,
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 上帝就給他開恩, 說:救贖他免得下坑; 我已經得了贖價。
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 他禱告上帝, 上帝就喜悅他, 使他歡呼朝見上帝的面; 上帝又看他為義。
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 他在人前歌唱說: 我犯了罪,顛倒是非, 這竟與我無益。
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 上帝救贖我的靈魂免入深坑; 我的生命也必見光。
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 為要從深坑救回人的靈魂, 使他被光照耀,與活人一樣。
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 約伯啊,你當側耳聽我的話, 不要作聲,等我講說。
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 你若有話說,就可以回答我; 你只管說,因我願以你為是。
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 若不然,你就聽我說; 你不要作聲,我便將智慧教訓你。
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”