< 約伯記 26 >

1 約伯回答說:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 無能的人蒙你何等的幫助! 膀臂無力的人蒙你何等的拯救!
“Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
3 無智慧的人蒙你何等的指教! 你向他多顯大知識!
Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
4 你向誰發出言語來? 誰的靈從你而出?
Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
5 在大水和水族以下的陰魂戰兢。
“Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
6 在上帝面前,陰間顯露; 滅亡也不得遮掩。 (Sheol h7585)
Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
7 上帝將北極鋪在空中, 將大地懸在虛空;
Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
8 將水包在密雲中, 雲卻不破裂;
Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
9 遮蔽他的寶座, 將雲鋪在其上;
Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
10 在水面的周圍劃出界限, 直到光明黑暗的交界。
Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
11 天的柱子因他的斥責震動驚奇。
Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
12 他以能力攪動大海; 他藉知識打傷拉哈伯,
Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
13 藉他的靈使天有妝飾; 他的手刺殺快蛇。
Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
14 看哪,這不過是上帝工作的些微; 我們所聽於他的是何等細微的聲音! 他大能的雷聲誰能明透呢?
Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”

< 約伯記 26 >