< 诗篇 98 >

1 一篇诗。 你们要向耶和华唱新歌! 因为他行过奇妙的事; 他的右手和圣臂施行救恩。
Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
2 耶和华发明了他的救恩, 在列邦人眼前显出公义;
Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
3 记念他向以色列家所发的慈爱,所凭的信实。 地的四极都看见我们 神的救恩。
Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
4 全地都要向耶和华欢乐; 要发起大声,欢呼歌颂!
Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
5 要用琴歌颂耶和华, 用琴和诗歌的声音歌颂他!
Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
6 用号和角声, 在大君王耶和华面前欢呼!
ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
7 愿海和其中所充满的澎湃; 世界和住在其间的也要发声。
Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
8 愿大水拍手; 愿诸山在耶和华面前一同欢呼;
Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
9 因为他来要审判遍地。 他要按公义审判世界, 按公正审判万民。
izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.

< 诗篇 98 >