< 诗篇 66 >
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 歌颂他名的荣耀! 用赞美的言语将他的荣耀发明!
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 当对 神说:你的作为何等可畏! 因你的大能,仇敌要投降你。
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 全地要敬拜你,歌颂你, 要歌颂你的名。 (细拉)
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 你们来看 神所行的, 他向世人所做之事是可畏的。
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 他将海变成干地,众民步行过河; 我们在那里因他欢喜。
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 他用权能治理万民,直到永远。 他的眼睛鉴察列邦; 悖逆的人不可自高。 (细拉)
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 万民哪,你们当称颂我们的 神, 使人得听赞美他的声音。
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 神啊,你曾试验我们, 熬炼我们,如熬炼银子一样。
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 你使人坐车轧我们的头; 我们经过水火, 你却使我们到丰富之地。
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 我要把肥牛作燔祭, 将公羊的香祭献给你, 又把公牛和山羊献上。 (细拉)
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 凡敬畏 神的人,你们都来听! 我要述说他为我所行的事。
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 但 神实在听见了; 他侧耳听了我祷告的声音。
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 神是应当称颂的! 他并没有推却我的祷告, 也没有叫他的慈爱离开我。
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!