< 诗篇 55 >

1 大卫的训诲诗,交与伶长。用丝弦的乐器。 神啊,求你留心听我的祷告, 不要隐藏不听我的恳求!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
2 求你侧耳听我,应允我。 我哀叹不安,发声唉哼,
mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
3 都因仇敌的声音,恶人的欺压; 因为他们将罪孽加在我身上,发怒气逼迫我。
chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
4 我心在我里面甚是疼痛; 死的惊惶临到我身。
Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
5 恐惧战兢归到我身; 惊恐漫过了我。
Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
6 我说:但愿我有翅膀像鸽子, 我就飞去,得享安息。
Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
7 我必远游, 宿在旷野。 (细拉)
Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
8 我必速速逃到避所, 脱离狂风暴雨。
Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
9 主啊,求你吞灭他们,变乱他们的舌头! 因为我在城中见了强暴争竞的事。
Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
10 他们在城墙上昼夜绕行; 在城内也有罪孽和奸恶。
Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
11 邪恶在其中; 欺压和诡诈不离街市。
Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
12 原来不是仇敌辱骂我, 若是仇敌,还可忍耐; 也不是恨我的人向我狂大, 若是恨我的人就必躲避他。
Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
13 不料是你;你原与我平等, 是我的同伴,是我知己的朋友!
Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
14 我们素常彼此谈论,以为甘甜; 我们与群众在 神的殿中同行。
Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
15 愿死亡忽然临到他们! 愿他们活活地下入阴间! 因为他们的住处,他们的心中,都是邪恶。 (Sheol h7585)
Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol h7585)
16 至于我,我要求告 神; 耶和华必拯救我。
Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
17 我要晚上、早晨、晌午哀声悲叹; 他也必听我的声音。
Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
18 他救赎我命脱离攻击我的人, 使我得享平安, 因为与我相争的人甚多。
Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
19 那没有更变、不敬畏 神的人, 从太古常存的 神必听见而苦待他。
Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
20 他背了约, 伸手攻击与他和好的人。
Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
21 他的口如奶油光滑, 他的心却怀着争战; 他的话比油柔和, 其实是拔出来的刀。
Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
22 你要把你的重担卸给耶和华, 他必抚养你; 他永不叫义人动摇。
Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
23 神啊,你必使恶人下入灭亡的坑; 流人血、行诡诈的人必活不到半世, 但我要倚靠你。
Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.

< 诗篇 55 >