< 诗篇 37 >

1 大卫的诗。 不要为作恶的心怀不平, 也不要向那行不义的生出嫉妒。
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 因为他们如草快被割下, 又如青菜快要枯干。
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 你当倚靠耶和华而行善, 住在地上,以他的信实为粮;
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 又要以耶和华为乐, 他就将你心里所求的赐给你。
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 当将你的事交托耶和华, 并倚靠他,他就必成全。
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 他要使你的公义如光发出, 使你的公平明如正午。
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 你当默然倚靠耶和华,耐性等候他; 不要因那道路通达的和那恶谋成就的心怀不平。
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 当止住怒气,离弃忿怒; 不要心怀不平,以致作恶。
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 因为作恶的必被剪除; 惟有等候耶和华的必承受地土。
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 还有片时,恶人要归于无有; 你就是细察他的住处也要归于无有。
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 但谦卑人必承受地土, 以丰盛的平安为乐。
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 恶人设谋害义人, 又向他咬牙。
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
13 主要笑他, 因见他受罚的日子将要来到。
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 恶人已经弓上弦,刀出鞘, 要打倒困苦穷乏的人, 要杀害行动正直的人。
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 他们的刀必刺入自己的心; 他们的弓必被折断。
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
16 一个义人所有的虽少, 强过许多恶人的富余。
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 因为恶人的膀臂必被折断; 但耶和华是扶持义人。
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
18 耶和华知道完全人的日子; 他们的产业要存到永远。
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 他们在急难的时候不致羞愧, 在饥荒的日子必得饱足。
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 恶人却要灭亡。 耶和华的仇敌要像羊羔的脂油; 他们要消灭,要如烟消灭。
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
21 恶人借贷而不偿还; 义人却恩待人,并且施舍。
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 蒙耶和华赐福的必承受地土; 被他咒诅的必被剪除。
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
23 义人的脚步被耶和华立定; 他的道路,耶和华也喜爱。
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 他虽失脚也不至全身仆倒, 因为耶和华用手搀扶他。
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
25 我从前年幼,现在年老, 却未见过义人被弃, 也未见过他的后裔讨饭。
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
26 他终日恩待人,借给人; 他的后裔也蒙福!
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
27 你当离恶行善, 就可永远安居。
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 因为,耶和华喜爱公平, 不撇弃他的圣民; 他们永蒙保佑, 但恶人的后裔必被剪除。
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 义人必承受地土, 永居其上。
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
30 义人的口谈论智慧; 他的舌头讲说公平。
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 神的律法在他心里; 他的脚总不滑跌。
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
32 恶人窥探义人, 想要杀他。
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 耶和华必不撇他在恶人手中; 当审判的时候,也不定他的罪。
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
34 你当等候耶和华,遵守他的道, 他就抬举你,使你承受地土; 恶人被剪除的时候,你必看见。
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
35 我见过恶人大有势力, 好像一棵青翠树在本土生发。
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 有人从那里经过,不料,他没有了; 我也寻找他,却寻不着。
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
37 你要细察那完全人,观看那正直人, 因为和平人有好结局。
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 至于犯法的人,必一同灭绝; 恶人终必剪除。
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
39 但义人得救是由于耶和华; 他在患难时作他们的营寨。
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 耶和华帮助他们,解救他们; 他解救他们脱离恶人,把他们救出来, 因为他们投靠他。
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.

< 诗篇 37 >