< 诗篇 35 >
1 大卫的诗。 耶和华啊,与我相争的,求你与他们相争! 与我相战的,求你与他们相战!
Salimo la Davide. Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane; mumenyane nawo amene akumenyana nane.
Tengani chishango ndi lihawo; dzukani ndipo bwerani mundithandize.
3 抽出枪来,挡住那追赶我的; 求你对我的灵魂说:我是拯救你的。
Tengani mkondo ndi nthungo, kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa. Uzani moyo wanga kuti, “Ine ndine chipulumutso chako.”
4 愿那寻索我命的,蒙羞受辱! 愿那谋害我的,退后羞愧!
Iwo amene akufunafuna moyo wanga anyozedwe ndi kuchita manyazi; iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.
Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.
6 愿他们的道路又暗又滑, 有耶和华的使者追赶他们。
Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.
7 因他们无故地为我暗设网罗, 无故地挖坑,要害我的性命。
Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,
8 愿灾祸忽然临到他身上! 愿他暗设的网缠住自己! 愿他落在其中遭灾祸!
chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa ukonde umene iwo abisa uwakole, agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.
Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.
10 我的骨头都要说: 耶和华啊,谁能像你 救护困苦人脱离那比他强壮的, 救护困苦穷乏人脱离那抢夺他的?
Thupi langa lidzafuwula mokondwera, “Ndani angafanane nanu Yehova? Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri, osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”
Mboni zopanda chisoni zinayimirira, zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.
Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.
13 至于我,当他们有病的时候, 我便穿麻衣,禁食,刻苦己心; 我所求的都归到自己的怀中。
Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya. Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,
14 我这样行,好像他是我的朋友,我的弟兄; 我屈身悲哀,如同人为母亲哀痛。
ndinayendayenda ndi kulira maliro, kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga. Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima kukhala ngati ndikulira amayi anga.
15 我在患难中,他们却欢喜,大家聚集。 我所不认识的那些下流人聚集攻击我; 他们不住地把我撕裂。
Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala; ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa. Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.
Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe; anandikukutira mano awo.
17 主啊,你看着不理要到几时呢? 求你救我的灵魂脱离他们的残害! 救我的生命脱离少壮狮子!
Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana? Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo, moyo wanga wopambana ku mikango.
Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu; pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.
19 求你不容那无理与我为仇的向我夸耀! 不容那无故恨我的向我挤眼!
Musalole adani anga onyenga akondwere chifukwa cha masautso anga; musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.
20 因为他们不说和平话, 倒想出诡诈的言语害地上的安静人。
Iwowo sayankhula mwamtendere, koma amaganizira zonamizira iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.
21 他们大大张口攻击我,说: 阿哈,阿哈,我们的眼已经看见了!
Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa! Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”
22 耶和华啊,你已经看见了,求你不要闭口! 主啊,求你不要远离我!
Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete. Ambuye musakhale kutali ndi ine.
23 我的 神我的主啊,求你奋兴醒起, 判清我的事,伸明我的冤!
Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza! Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.
24 耶和华—我的 神啊,求你按你的公义判断我, 不容他们向我夸耀!
Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga. Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.
25 不容他们心里说:阿哈,遂我们的心愿了! 不容他们说:我们已经把他吞了!
Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!” Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”
26 愿那喜欢我遭难的一同抱愧蒙羞! 愿那向我妄自尊大的披惭愧,蒙羞辱!
Onse amene amakondwera ndi masautso anga achite manyazi ndi kusokonezeka. Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana, avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.
27 愿那喜悦我冤屈得伸的欢呼快乐; 愿他们常说:当尊耶和华为大! 耶和华喜悦他的仆人平安。
Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa, afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo. Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke, Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”
Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu ndi za matamando anu tsiku lonse.