< 诗篇 34 >

1 大卫在亚比米勒面前装疯,被他赶出去,就作这诗。 我要时时称颂耶和华; 赞美他的话必常在我口中。
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 我的心必因耶和华夸耀; 谦卑人听见就要喜乐。
Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 你们和我当称耶和华为大, 一同高举他的名。
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 我曾寻求耶和华,他就应允我, 救我脱离了一切的恐惧。
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 凡仰望他的,便有光荣; 他们的脸必不蒙羞。
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 我这困苦人呼求,耶和华便垂听, 救我脱离一切患难。
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 耶和华的使者在敬畏他的人四围安营, 搭救他们。
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
8 你们要尝尝主恩的滋味,便知道他是美善; 投靠他的人有福了!
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 耶和华的圣民哪,你们当敬畏他, 因敬畏他的一无所缺。
Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 少壮狮子还缺食忍饿, 但寻求耶和华的什么好处都不缺。
Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 众弟子啊,你们当来听我的话! 我要将敬畏耶和华的道教训你们。
Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 有何人喜好存活, 爱慕长寿,得享美福,
Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 就要禁止舌头不出恶言, 嘴唇不说诡诈的话。
asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 要离恶行善, 寻求和睦,一心追赶。
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 耶和华的眼目看顾义人; 他的耳朵听他们的呼求。
Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 耶和华向行恶的人变脸, 要从世上除灭他们的名号。
nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 义人呼求,耶和华听见了, 便救他们脱离一切患难。
Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 耶和华靠近伤心的人, 拯救灵性痛悔的人。
Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 义人多有苦难, 但耶和华救他脱离这一切,
Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 又保全他一身的骨头, 连一根也不折断。
Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 恶必害死恶人; 恨恶义人的,必被定罪。
Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 耶和华救赎他仆人的灵魂; 凡投靠他的,必不致定罪。
Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.

< 诗篇 34 >