< 诗篇 21 >
1 大卫的诗,交与伶长。 耶和华啊,王必因你的能力欢喜; 因你的救恩,他的快乐何其大!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mfumu ikusangalala mu mphamvu yanu, chimwemwe chake nʼchachikuludi pa kupambana kumene mumapereka!
2 他心里所愿的,你已经赐给他; 他嘴唇所求的,你未尝不应允。 (细拉)
Inu mwayipatsa zokhumba za mtima wake ndipo simunayimane zopempha za pa milomo yake. (Sela)
Inu munayilandira ndi madalitso ochuluka ndipo munayiveka chipewa chaufumu chagolide weniweni pa mutu wake.
4 他向你求寿,你便赐给他, 就是日子长久,直到永远。
Iye anakupemphani moyo, ndipo munamupatsa masiku ochuluka kwamuyaya.
5 他因你的救恩大有荣耀; 你又将尊荣威严加在他身上。
Kudzera mʼzigonjetso zimene munapereka, ulemerero wake ndi waukulu; Inu mwapereka pa iyo ulemerero ndi ufumu.
6 你使他有洪福,直到永远, 又使他在你面前欢喜快乐。
Zoonadi Inu mwayipatsa madalitso amuyaya, Inu mwayipatsa chisangalalo ndi chimwemwe chimene chili pamaso panu.
Pakuti mfumu imadalira Yehova; kudzera mʼchikondi chake chosatha cha Wammwambamwamba, iyo sidzagwedezeka.
8 你的手要搜出你的一切仇敌; 你的右手要搜出那些恨你的人。
Dzanja lanu lidzayimitsa adani anu onse; dzanja lanu lamanja lidzagwira adani anu.
9 你发怒的时候,要使他们如在炎热的火炉中。 耶和华要在他的震怒中吞灭他们; 那火要把他们烧尽了。
Pa nthawi ya kuonekera kwanu mudzawasandutsa ngʼanjo yamoto yotentha. Mu ukali wake Yehova adzawameza, ndipo moto wake udzawatha.
10 你必从世上灭绝他们的子孙, 从人间灭绝他们的后裔。
Inu mudzawononga ana awo pa dziko lapansi, zidzukulu zawo pakati pa anthu.
11 因为他们有意加害于你; 他们想出计谋,却不能作成。
Ngakhale iwo akukonzereni chiwembu mwa kuchenjera kwawo sadzapambana;
pakuti mudzawapirikitsa ndipo adzaonetsa misana yawo pamene mudzawaloza ndi mivi yanu.
13 耶和华啊,愿你因自己的能力显为至高! 这样,我们就唱诗,歌颂你的大能。
Mukwezeke Inu Yehova mʼmphamvu yanu, ife tidzayimba nyimbo ndi kutamanda mphamvu yanu.