< 诗篇 19 >

1 大卫的诗,交与伶长。 诸天述说 神的荣耀; 穹苍传扬他的手段。
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
2 这日到那日发出言语; 这夜到那夜传出知识。
Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
3 无言无语, 也无声音可听。
Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
4 它的量带通遍天下, 它的言语传到地极。 神在其间为太阳安设帐幕;
Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
5 太阳如同新郎出洞房, 又如勇士欢然奔路。
Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
6 它从天这边出来,绕到天那边, 没有一物被隐藏不得它的热气。
Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
7 耶和华的律法全备,能苏醒人心; 耶和华的法度确定,能使愚人有智慧。
Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
8 耶和华的训词正直,能快活人的心; 耶和华的命令清洁,能明亮人的眼目。
Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
9 耶和华的道理洁净,存到永远; 耶和华的典章真实,全然公义—
Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
10 都比金子可羡慕,且比极多的精金可羡慕; 比蜜甘甜,且比蜂房下滴的蜜甘甜。
ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
11 况且你的仆人因此受警戒, 守着这些便有大赏。
Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
12 谁能知道自己的错失呢? 愿你赦免我隐而未现的过错。
Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
13 求你拦阻仆人不犯任意妄为的罪, 不容这罪辖制我, 我便完全,免犯大罪。
Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
14 耶和华—我的磐石,我的救赎主啊, 愿我口中的言语、心里的意念在你面前蒙悦纳。
Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.

< 诗篇 19 >