< 箴言 19 >
Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
2 心无知识的,乃为不善; 脚步急快的,难免犯罪。
Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
5 作假见证的,必不免受罚; 吐出谎言的,终不能逃脱。
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
6 好施散的,有多人求他的恩情; 爱送礼的,人都为他的朋友。
Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
7 贫穷人,弟兄都恨他; 何况他的朋友,更远离他! 他用言语追随,他们却走了。
Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
8 得着智慧的,爱惜生命; 保守聪明的,必得好处。
Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
9 作假见证的,不免受罚; 吐出谎言的,也必灭亡。
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
10 愚昧人宴乐度日是不合宜的; 何况仆人管辖王子呢?
Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
11 人有见识就不轻易发怒; 宽恕人的过失便是自己的荣耀。
Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
12 王的忿怒好像狮子吼叫; 他的恩典却如草上的甘露。
Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
13 愚昧的儿子是父亲的祸患; 妻子的争吵如雨连连滴漏。
Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
14 房屋钱财是祖宗所遗留的; 惟有贤慧的妻是耶和华所赐的。
Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
16 谨守诫命的,保全生命; 轻忽己路的,必致死亡。
Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
17 怜悯贫穷的,就是借给耶和华; 他的善行,耶和华必偿还。
Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
18 趁有指望,管教你的儿子; 你的心不可任他死亡。
Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
23 敬畏耶和华的,得着生命; 他必恒久知足,不遭祸患。
Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
24 懒惰人放手在盘子里, 就是向口撤回,他也不肯。
Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
25 鞭打亵慢人,愚蒙人必长见识; 责备明哲人,他就明白知识。
Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
29 刑罚是为亵慢人预备的; 鞭打是为愚昧人的背预备的。
Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.