< 箴言 16 >

1 心中的谋算在乎人; 舌头的应对由于耶和华。
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 人一切所行的,在自己眼中看为清洁; 惟有耶和华衡量人心。
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 你所做的,要交托耶和华, 你所谋的,就必成立。
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 耶和华所造的,各适其用; 就是恶人也为祸患的日子所造。
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 凡心里骄傲的,为耶和华所憎恶; 虽然连手,他必不免受罚。
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 因怜悯诚实,罪孽得赎; 敬畏耶和华的,远离恶事。
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 人所行的,若蒙耶和华喜悦, 耶和华也使他的仇敌与他和好。
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 多有财利,行事不义, 不如少有财利,行事公义。
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 人心筹算自己的道路; 惟耶和华指引他的脚步。
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 王的嘴中有神语, 审判之时,他的口必不差错。
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 公道的天平和秤都属耶和华; 囊中一切法码都为他所定。
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 作恶,为王所憎恶, 因国位是靠公义坚立。
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 公义的嘴为王所喜悦; 说正直话的,为王所喜爱。
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 王的震怒如杀人的使者; 但智慧人能止息王怒。
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 王的脸光使人有生命; 王的恩典好像春云时雨。
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 得智慧胜似得金子; 选聪明强如选银子。
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 正直人的道是远离恶事; 谨守己路的,是保全性命。
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 骄傲在败坏以先; 狂心在跌倒之前。
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 心里谦卑与穷乏人来往, 强如将掳物与骄傲人同分。
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 谨守训言的,必得好处; 倚靠耶和华的,便为有福。
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 心中有智慧,必称为通达人; 嘴中的甜言,加增人的学问。
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 人有智慧就有生命的泉源; 愚昧人必被愚昧惩治。
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 智慧人的心教训他的口, 又使他的嘴增长学问。
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 良言如同蜂房, 使心觉甘甜,使骨得医治。
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 有一条路,人以为正, 至终成为死亡之路。
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 劳力人的胃口使他劳力, 因为他的口腹催逼他。
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 匪徒图谋奸恶, 嘴上仿佛有烧焦的火。
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 乖僻人播散纷争; 传舌的,离间密友。
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 强暴人诱惑邻舍, 领他走不善之道。
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 眼目紧合的,图谋乖僻; 嘴唇紧闭的,成就邪恶。
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 白发是荣耀的冠冕, 在公义的道上必能得着。
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 不轻易发怒的,胜过勇士; 治服己心的,强如取城。
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 签放在怀里, 定事由耶和华。
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< 箴言 16 >