< 尼希米记 7 >

1 城墙修完,我安了门扇,守门的、歌唱的,和利未人都已派定。
Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
2 我就派我的弟兄哈拿尼和营楼的宰官哈拿尼雅管理耶路撒冷;因为哈拿尼雅是忠信的,又敬畏 神过于众人。
Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
3 我吩咐他们说:“等到太阳上升才可开耶路撒冷的城门;人尚看守的时候就要关门上闩;也当派耶路撒冷的居民各按班次看守自己房屋对面之处。”
Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
4 城是广大,其中的民却稀少,房屋还没有建造。
Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
5 我的 神感动我心,招聚贵胄、官长,和百姓,要照家谱计算。我找着第一次上来之人的家谱,其上写着:
Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
6 巴比伦王尼布甲尼撒从前掳去犹大省的人,现在他们的子孙从被掳到之地回耶路撒冷和犹大,各归本城。
Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
7 他们是同着所罗巴伯、耶书亚、尼希米、亚撒利雅、拉米、拿哈玛尼、末底改、必珊、米斯毗列、比革瓦伊、尼宏、巴拿回来的。
Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
8 以色列人民的数目记在下面:巴录的子孙二千一百七十二名;
Zidzukulu za Parosi 2,172
9 示法提雅的子孙三百七十二名;
Zidzukulu za Sefatiya 372
10 亚拉的子孙六百五十二名;
Zidzukulu za Ara 652
11 巴哈·摩押的后裔,就是耶书亚和约押的子孙二千八百一十八名;
Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
12 以拦的子孙一千二百五十四名;
Zidzukulu za Elamu 1,254
13 萨土的子孙八百四十五名;
Zidzukulu za Zatu 845
14 萨改的子孙七百六十名;
Zidzukulu za Zakai 760
15 宾内的子孙六百四十八名;
Zidzukulu za Binuyi 648
16 比拜的子孙六百二十八名;
Zidzukulu za Bebai 628
17 押甲的子孙二千三百二十二名;
Zidzukulu za Azigadi 2,322
18 亚多尼干的子孙六百六十七名;
Zidzukulu za Adonikamu 667
19 比革瓦伊的子孙二千零六十七名;
Zidzukulu za Abigivai 2,067
20 亚丁的子孙六百五十五名;
Zidzukulu za Adini 655
21 亚特的后裔,就是希西家的子孙九十八名;
Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
22 哈顺的子孙三百二十八名;
Zidzukulu za Hasumu 328
23 比赛的子孙三百二十四名;
Zidzukulu za Bezayi 324
24 哈拉的子孙一百一十二名;
Zidzukulu za Harifu 112
25 基遍人九十五名;
Zidzukulu za Gibiyoni 95.
26 伯利恒人和尼陀法人共一百八十八名;
Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
27 亚拿突人一百二十八名;
Anthu a ku Anatoti 128
28 伯·亚斯玛弗人四十二名;
Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
29 基列·耶琳人、基非拉人、比录人共七百四十三名;
Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
30 拉玛人和迦巴人共六百二十一名;
Anthu a ku Rama ndi Geba 621
31 默玛人一百二十二名;
Anthu a ku Mikimasi 122
32 伯特利人和艾人共一百二十三名;
Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
33 别的尼波人五十二名;
Anthu a ku Nebo winayo 52
34 别的以拦子孙一千二百五十四名;
Ana a Elamu wina 1,254
35 哈琳的子孙三百二十名;
Zidzukulu za Harimu 320
36 耶利哥人三百四十五名;
Zidzukulu za Yeriko 345
37 罗德人、哈第人、阿挪人共七百二十一名;
Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
38 西拿人三千九百三十名。
Zidzukulu za Senaya 3,930.
39 祭司:耶书亚家,耶大雅的子孙九百七十三名;
Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
40 音麦的子孙一千零五十二名;
Zidzukulu za Imeri 1,052
41 巴施户珥的子孙一千二百四十七名;
Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
42 哈琳的子孙一千零一十七名。
Zidzukulu za Harimu 1,017.
43 利未人:何达威的后裔,就是耶书亚和甲篾的子孙七十四名。
Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
44 歌唱的:亚萨的子孙一百四十八名。
Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
45 守门的:沙龙的子孙、亚特的子孙、达们的子孙、亚谷的子孙、哈底大的子孙、朔拜的子孙,共一百三十八名。
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
46 尼提宁:西哈的子孙、哈苏巴的子孙、答巴俄的子孙、
Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
47 基绿的子孙、西亚的子孙、巴顿的子孙、
Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
48 利巴拿的子孙、哈迦巴的子孙、萨买的子孙、
Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
49 哈难的子孙、吉德的子孙、迦哈的子孙、
Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
50 利亚雅的子孙、利汛的子孙、尼哥大的子孙、
Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
51 迦散的子孙、乌撒的子孙、巴西亚的子孙、
Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
52 比赛的子孙、米乌宁的子孙、尼普心的子孙、
Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
53 巴卜的子孙、哈古巴的子孙、哈忽的子孙、
Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
54 巴洗律的子孙、米希大的子孙、哈沙的子孙、
Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
55 巴柯的子孙、西西拉的子孙、答玛的子孙、
Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
56 尼细亚的子孙、哈提法的子孙。
Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
57 所罗门仆人的后裔,就是琐太的子孙、琐斐列的子孙、比路大的子孙、
Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
58 雅拉的子孙、达昆的子孙、吉德的子孙、
zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
59 示法提雅的子孙、哈替的子孙、玻黑列·哈斯巴音的子孙、亚们的子孙。
zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
60 尼提宁和所罗门仆人的后裔共三百九十二名。
Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
61 从特米拉、特哈萨、基绿、亚顿、音麦上来的,不能指明他们的宗族谱系是以色列人不是;
Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
62 他们是第莱雅的子孙、多比雅的子孙、尼哥大的子孙,共六百四十二名。
Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
63 祭司中,哈巴雅的子孙、哈哥斯的子孙、巴西莱的子孙;因为他们的先祖娶了基列人巴西莱的女儿为妻,所以起名叫巴西莱。
Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
64 这三家的人在族谱之中寻查自己的谱系,却寻不着,因此算为不洁,不准供祭司的职任。
Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
65 省长对他们说:“不可吃至圣的物,直到有用乌陵和土明决疑的祭司兴起来。”
Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
66 会众共有四万二千三百六十名。
Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
67 此外,还有他们的仆婢七千三百三十七名,又有歌唱的男女二百四十五名。
Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
68 他们有马七百三十六匹,骡子二百四十五匹,
Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
69 骆驼四百三十五只,驴六千七百二十匹。
Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
70 有些族长为工程捐助。省长捐入库中的金子一千达利克,碗五十个,祭司的礼服五百三十件。
Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
71 又有族长捐入工程库的金子二万达利克,银子二千二百弥拿。
Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
72 其余百姓所捐的金子二万达利克,银子二千弥拿,祭司的礼服六十七件。
Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
73 于是祭司、利未人、守门的、歌唱的、民中的一些人、尼提宁,并以色列众人,各住在自己的城里。
Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.

< 尼希米记 7 >