< 何西阿书 13 >
1 从前以法莲说话,人都战兢, 他在以色列中居处高位; 但他在事奉巴力的事上犯罪就死了。
Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
2 现今他们罪上加罪, 用银子为自己铸造偶像, 就是照自己的聪明制造, 都是匠人的工作。 有人论说, 献祭的人可以向牛犊亲嘴。
Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
3 因此,他们必如早晨的云雾, 又如速散的甘露, 像场上的糠秕被狂风吹去, 又像烟气腾于窗外。
Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
4 自从你出埃及地以来, 我就是耶和华—你的 神。 在我以外,你不可认识别神; 除我以外并没有救主。
Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
6 这些民照我所赐的食物得了饱足; 既得饱足,心就高傲, 忘记了我。
Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
8 我遇见他们必像丢崽子的母熊, 撕裂他们的胸膛。 在那里,我必像母狮吞吃他们; 野兽必撕裂他们。
Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
9 以色列啊,你与我反对, 就是反对帮助你的,自取败坏。
“Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
10 你曾求我说: 给我立王和首领。 现在你的王在哪里呢? 治理你的在哪里呢? 让他在你所有的城中拯救你吧!
Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
13 产妇的疼痛必临到他身上; 他是无智慧之子, 到了产期不当迟延。
Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
14 我必救赎他们脱离阴间, 救赎他们脱离死亡。 死亡啊,你的灾害在哪里呢? 阴间哪,你的毁灭在哪里呢? 在我眼前绝无后悔之事。 (Sheol )
“Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol )
15 他在弟兄中虽然茂盛, 必有东风刮来, 就是耶和华的风从旷野上来。 他的泉源必干; 他的源头必竭; 仇敌必掳掠他所积蓄的一切宝器。
ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
16 撒马利亚必担当自己的罪, 因为悖逆她的 神。 她必倒在刀下; 婴孩必被摔死; 孕妇必被剖开。
Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”