< 创世记 32 >
Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
2 雅各看见他们就说:“这是 神的军兵”,于是给那地方起名叫玛哈念。
Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
3 雅各打发人先往西珥地去,就是以东地,见他哥哥以扫,
Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
4 吩咐他们说:“你们对我主以扫说:‘你的仆人雅各这样说:我在拉班那里寄居,直到如今。
Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
5 我有牛、驴、羊群、仆婢,现在打发人来报告我主,为要在你眼前蒙恩。’”
Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
6 所打发的人回到雅各那里,说:“我们到了你哥哥以扫那里,他带着四百人,正迎着你来。”
Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
7 雅各就甚惧怕,而且愁烦,便把那与他同在的人口和羊群、牛群、骆驼分做两队,
Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
8 说:“以扫若来击杀这一队,剩下的那一队还可以逃避。”
Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
9 雅各说:“耶和华—我祖亚伯拉罕的 神,我父亲以撒的 神啊,你曾对我说:‘回你本地本族去,我要厚待你。’
Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
10 你向仆人所施的一切慈爱和诚实,我一点也不配得;我先前只拿着我的杖过这约旦河,如今我却成了两队了。
Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
11 求你救我脱离我哥哥以扫的手;因为我怕他来杀我,连妻子带儿女一同杀了。
Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
12 你曾说:‘我必定厚待你,使你的后裔如同海边的沙,多得不可胜数。’”
Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
13 当夜,雅各在那里住宿,就从他所有的物中拿礼物要送给他哥哥以扫:
Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
14 母山羊二百只,公山羊二十只,母绵羊二百只,公绵羊二十只,
Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
15 奶崽子的骆驼三十只—各带着崽子,母牛四十只,公牛十只,母驴二十匹,驴驹十匹;
ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
16 每样各分一群,交在仆人手下,就对仆人说:“你们要在我前头过去,使群群相离,有空闲的地方”;
Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
17 又吩咐尽先走的说:“我哥哥以扫遇见你的时候,问你说:‘你是哪家的人?要往哪里去?你前头这些是谁的?’
Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
18 你就说:‘是你仆人雅各的,是送给我主以扫的礼物;他自己也在我们后边。’”
Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
19 又吩咐第二、第三,和一切赶群畜的人说:“你们遇见以扫的时候也要这样对他说;
Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
20 并且你们要说:‘你仆人雅各在我们后边。’”因雅各心里说:“我借着在我前头去的礼物解他的恨,然后再见他的面,或者他容纳我。”
Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
22 他夜间起来,带着两个妻子,两个使女,并十一个儿子,都过了雅博渡口,
Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
24 只剩下雅各一人。有一个人来和他摔跤,直到黎明。
Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
25 那人见自己胜不过他,就将他的大腿窝摸了一把,雅各的大腿窝正在摔跤的时候就扭了。
Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
26 那人说:“天黎明了,容我去吧!”雅各说:“你不给我祝福,我就不容你去。”
Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
27 那人说:“你名叫什么?”他说:“我名叫雅各。”
Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
28 那人说:“你的名不要再叫雅各,要叫以色列;因为你与 神与人较力,都得了胜。”
Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
29 雅各问他说:“请将你的名告诉我。”那人说:“何必问我的名?”于是在那里给雅各祝福。
Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
30 雅各便给那地方起名叫毗努伊勒,意思说:“我面对面见了 神,我的性命仍得保全。”
Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
31 日头刚出来的时候,雅各经过毗努伊勒,他的大腿就瘸了。
Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
32 故此,以色列人不吃大腿窝的筋,直到今日,因为那人摸了雅各大腿窝的筋。
Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.