< 詩篇 98 >

1 請眾向上主歌唱新歌,因為祂行了奇事。祂的右手和祂的聖臂為祂獲得了勝利。
Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
2 上主已經宣佈了自己的救恩,將自己的正義已啟示給萬民。
Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
3 上主記起自己的良善和忠誠,即向以色列家族廣施的寬仁。全球看見了我們天主的救恩。
Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
4 普世大地,請向上主歌舞,請踴躍,請歡樂,彈琴演奏:
Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
5 彈著豎琴,向上主讚頌,彈著豎琴,伴隨著絃韻。
Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
6 吹起喇叭,伴奏著號角,在上主面前謳歌。
ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
7 海洋及其中的一切澎湃,寰宇的居民驚駭!
Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
8 江河拍手鼓掌,山岳舞蹈歌唱。
Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
9 都在上主面前歡樂,因為祂已駕臨是要統治大地乾坤;祂以正義審判普世人群,祂要以公平治理天下萬民。
izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.

< 詩篇 98 >