< 詩篇 76 >
1 阿撒夫的詩歌。交與樂官,樂用絃樂。 天主在猶大地顯示了自己,在以色列廣揚了自己的名。
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
2 他在撒冷支搭了自己的帳幕,他在熙雍建豎了自己的住處。
Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
3 在那裏他打斷了弓上的火箭,他也打斷了槍柄、盾牌與刀劍。
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
5 膽大的人,全被剝奪,一睡不醒,那勇敢的將領,手臂麻木失靈。
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
6 雅各伯的天主,因您的恐嚇,戰車戰馬都驚得麻木僵直。
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
10 人 的狂怒成全您的光榮,幸免憤怒的人,向您祝頌。
Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
11 您們許願要向上主您們的天主還願;他四周的人都要向可敬者供奉祭獻。
Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.