< 詩篇 76 >

1 阿撒夫的詩歌。交與樂官,樂用絃樂。 天主在猶大地顯示了自己,在以色列廣揚了自己的名。
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
2 他在撒冷支搭了自己的帳幕,他在熙雍建豎了自己的住處。
Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
3 在那裏他打斷了弓上的火箭,他也打斷了槍柄、盾牌與刀劍。
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
4 大能者,您大發光明,是來自遠古的山陵。
Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
5 膽大的人,全被剝奪,一睡不醒,那勇敢的將領,手臂麻木失靈。
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
6 雅各伯的天主,因您的恐嚇,戰車戰馬都驚得麻木僵直。
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
7 您尊嚴可畏;您盛怒時,何人能在您面前站立?
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
8 您由天上宣佈判案,大地戰慄默默無言。
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
9 因為天主起來施行審判,是要救世上的一切貧賤。
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
10 人 的狂怒成全您的光榮,幸免憤怒的人,向您祝頌。
Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
11 您們許願要向上主您們的天主還願;他四周的人都要向可敬者供奉祭獻。
Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
12 他抑壓首領們的氣燄,他使地上的眾王抖顫。
Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.

< 詩篇 76 >