< 詩篇 73 >

1 阿撒夫的詩歌。
Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
2 天主待正直的人多麼美善,上主對心裏潔淨的人亦然!
Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
3 我的腳幾乎要跌跤,我的腳險些要滑倒,
Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
4 因我看見惡人安寧幸福,就對驕橫的人心生嫉妒。
Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
5 原來他們總沒有受過重創,所以他們的身體健康肥胖;
Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
6 他們沒有別人所受的憂傷,也沒有常人所遭遇的災殃。
Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
7 故此,驕傲纏繞他們相似項鍊,殘暴遮蔽他們有如衣衫。
Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
8 他們的邪惡,出自肥胖的心田,讓他們自己的惡念,肆意氾濫。
Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
9 他們譏諷嘲弄,言惡語狂,他們欺壓恐嚇蠻橫倔強;
Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
10 用自己的口褻瀆上天,以自己的舌詆毀塵寰。
Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
11 因此我的百姓向他們依歸,滿口啜飲由他們供給的水,
Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
12 且說:天主豈能知悉,難道至高者能理會?
Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
13 看,這些人為非作歹,常享平安,積存錢財,
Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
14 的確,我白白清心寡欲,我徒然洗手表白無辜。
Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
15 我時時遭受鞭擊,也天天遇到責斥。
Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
16 我若想:我說話若與他們相同,就等於放棄與您子民為同宗。
Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
17 我愈設法了解這事,我愈覺得神妙莫測。
kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
18 直到我接近天主的奧妙,直到我注意他們的結果。
Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
19 您的確將他們置於坡路,讓他們滑倒於消滅之途。
Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
20 他們瞬息之間變得如此悽涼,他們因受驚過度而從此滅亡。
Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
21 上主,世人睡醒,怎樣了解夢境;您醒時,也怎樣看他們的幻影。
Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
22 幾時我的心靈遭受酸苦,刺痛也會進入我的肺腑。
ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
23 原來是我愚昧毫無理性,在您面前竟燃好像畜牲。
Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
24 但以後,我要常與您同處,您已經握住了我的右手。
Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
25 您要以您的聖訓來領導我,最後引我進入您的榮耀。
Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
26 在天上除您以外,為我還能有誰﹖在地上除您以外,為我一無所喜。
Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
27 我的肉身和我的心靈,雖以憔瘁;天主卻永是我心的福分和磐石。
Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
28 看,遠離您的人必將趨於沉淪。您必消滅一切背棄您的人民。 親近天主對我是多麼的美好:只有上主天主是我的避難所。我要在熙雍女子門前,把您一切的工程宣傳。
Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.

< 詩篇 73 >