< 詩篇 72 >
1 天主,求您給君王傳授您的權柄,求您給太子傳授您的公正。
Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2 使他照正義統治您的百姓,使他按公道管理您的平民。
Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4 他必衛護百姓中的窮人,救助窮苦人的子孫,蹂躪欺壓人的暴民。
Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6 祂降臨如落在草原上的喜雨,又如潤澤田地的甘露。
Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7 在祂的歲月中,正義必要興盛,到處國泰民安,直至月亮失明。
Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
8 祂將統治大地,從這海到那海,由大河的流域,至地極的邊界。
Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
9 祂的仇敵將向他屈膝跪拜,和祂作對的人要舌舔塵埃。
Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10 塔爾史士和群島的眾王要獻上禮品,舍巴和色巴的君王,也都要前來進貢。
Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13 祂將憐恤不幸和貧乏的群眾,祂要救護窮苦貧病者的生命。
Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14 祂要救他們脫離殘暴與壓迫,他們的血在祂眼中珍貴無比。
Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
15 願祂常存!願眾人向祂奉獻舍巴黃金,願眾人時常向祂祈禱,不斷向祂求恩!
Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16 田地裏所出產的五穀百果必將豐盈,山嶺上的收成也要富饒有如黎巴嫩,城市的人必要昌盛有如地上的草茵。
Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
17 祂的名號常存,永受讚揚;祂的名號永留,與日爭光。萬邦要因祂而得福,萬民要稱祂為有福。
Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
18 願上主天主,以色列的天主享受讚頌,因為只有上主作出了奇妙的化工。
Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 願上主光榮的名號永受讚美,願上主的榮耀充滿整個大地!阿們!阿們!
Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.