< 詩篇 66 >

1 普世大地,請向天主歡呼!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 請歌頌天主聖名的光榮,請獻給天主輝煌的讚頌。
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 請您們向天主說:您的作為是何等驚人!您威赫的大能,您的仇敵都向您奉承。
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 天主,普世都要朝拜您,全球都要歌頌您的聖名。
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 請您們前來觀看天主的作為,他對世人作的事實在可奇。
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 他曾使海洋乾涸,使人徒步走過江河,叫我們因他而喜樂。
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 他以自己的大能,永遠統治列國萬邦,他的眼睛鑒察萬民,不使叛逆者狂妄。
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 萬民,請您們讚美我們的天主,請傳揚天主應受的榮耀。
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
9 他曾使我們的性命存活,沒有讓我們的腳步滑倒。
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 天主,因為您曾考驗我們,像鍊銀子一般,也鍊我們;
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
11 您曾引領我們墜入了網羅,曾將鐵索繫在我們的身腰;
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 您曾使異民騎在我們頭上,使我們經過水深火熱中央,最後您使我們獲得解放。
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
13 我帶著全燔祭進入您的聖殿,我要向您償還我的各種誓願:
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 就是我從前在困厄中間,我口所許,我唇所發的願。
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 我要以肥大牲畜作全燔祭,要把公羊的馨香獻與您,要將牛犢和山羊祭奠您。
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 凡敬愛天主的人,請您們前來靜聽,我要敘述祂為我所作所行。
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 我親口呼號過他,我舌頭稱揚過他。
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
18 如果我真存心作惡,上主決不會俯聽我;
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 然而天主終於俯聽了我,也傾聽了我哀號的祈禱,
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 天主應受讚美:因祂從未拒絕我的懇求,從未在我身上撤回祂的仁慈。
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!

< 詩篇 66 >