< 詩篇 44 >

1 科辣黑後裔的訓誨歌,交與樂官。 天主,我們親耳聽見過,祖先也給我們述說過:昔日在他們那一時代,你手所行的偉業。
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 你為栽培他們,手驅散外人,你為發展他們,曾親自磨難異民。
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 的確,他們佔領了那地,並非靠著自己的刀劍,他們獲得了勝利,並非靠著自己的臂腕;完全是賴著你的右手和你的腕能,並你儀容的光輝,因為你喜愛他們。
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 你是我的天主,我的君王,是你使雅各伯打了勝仗。
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 仰仗著你,我們克勝了我們的對頭,因你的名,我們踐踏了我們的仇讎。
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 因我從未依恃過我的弓箭,拯救我的,也不是我的刀劍,
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 而是你救我們脫離我們的對頭,是你使痛恨我們的人都蒙羞受辱。
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 我們時時以天主而自豪,永永遠遠歌頌你的名號。
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 然而現今你拋棄我們,使我們蒙羞受辱,你也不再與我們的軍隊,一同出征為伍;
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 反而使我們在敵人,前轉身敗走,讓那些恨我們的人,劫奪俘虜。
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 你使我們有如待宰的羔羊,你使我們漂流而逃亡異邦;
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 你將你的子民賤價出售,你由售價並未獲財。
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 你使我們遭受鄰邦的侮辱,四周人民對我們諷刺咒詛;
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 你使我們成了異族的話柄,外邦人都向我們搖頭熱諷。
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 我的恥辱終日擺在我的眼前,羞愧也常籠罩著我的臉面:
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 因我聽到侮慢與欺凌者的聲音,又面臨仇敵和尋隙報復的人民。
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 我們雖然從未把你忘記,從來沒有違背過你的盟約,但我們身受了這一切災禍。
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 我們的心志從來沒有萎靡退縮,我們的腳步也未偏離你的正道;
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 但你竟將我們拋棄在野犬的邊界,以死亡的陰影把我們遮蓋。
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 如果我們忘卻了我們天主的聖名,並舉起我們的手朝向外邦的神明:
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 難道天主究查不出這事?因為祂洞悉人心的隱密。
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 我們卻是為了你,時常受傷受戕,他們竟將我們視作待宰的群羊。
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 醒來!我主,你為什麼依舊沉睡?起來!你不要永遠把我們拋棄。
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 你為什麼掩起你的慈顏,不顧我們的痛苦和辛酸?
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 請看,我們的靈魂已俯伏在灰間,我們的身體已緊貼於地面。
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 求你站起來,援助我們,因你的慈愛,拯救我們。
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

< 詩篇 44 >