< 詩篇 38 >
1 達味紀念歌。 上主,求你不要在你的震怒中責罰我,求你不要在你的氣憤中懲戒我。
Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
3 因了你的盛怒,我已體無完膚;因了我的罪行,我已粉身碎骨。
Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
4 因為我的罪過高出我的頭頂,好似重擔把我壓得過分沉重。
Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
8 我已筋疲力盡,奄奄一息;我已心痛欲絕,嗟嘆不已。
Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
9 我主,我的呻吟常在你的面前,我的悲歎不向你隱瞞;
Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
10 我的心顫慄,我的精力衰退,我眼目的光明也已消逝。
Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
11 我遭難時,我的友朋都袖手旁觀,我的親人都站得很遠。
Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
12 追尋我命的人,張設網羅,設法害我的人,散布惡謨,他們行詭計日夜思索。
Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
13 但我好像是一個有耳聽不見的聾子,我又好像是一個有口不能言的啞巴。
Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
14 我竟成了一個沒有聽覺的人,成了一個口中沒有辯詞的人。
Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
15 因為我唯有仰慕你,上主,你必應允我,我主我天主!
Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
16 我原來說過:「不要讓他們洋洋得意,不要讓他們因我的失足而沾沾自喜。」
Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
18 我的確承認我犯了罪愆,我為了我的過惡而憂慚。
Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
19 無故加害我的人,力強兇暴,無理憎恨我的人,成群結伙;
Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
20 他們都以怨報德而對待我,因我追求正義而惱恨我。
Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
21 上主,求你不要捨棄我,我主,求你不要遠離我。
Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.