< 詩篇 38 >

1 達味紀念歌。 上主,求你不要在你的震怒中責罰我,求你不要在你的氣憤中懲戒我。
Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
2 因為你的箭射中了我,你的手重壓了我。
Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
3 因了你的盛怒,我已體無完膚;因了我的罪行,我已粉身碎骨。
Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
4 因為我的罪過高出我的頭頂,好似重擔把我壓得過分沉重。
Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
5 我的創痍漬爛流膿,完全由於我的愚矇。
Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
6 我悲傷得身已傴僂,終日行動滿懷憂愁。
Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
7 因為我的腰肢焦灼難受,我的肉體已無完膚。
Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
8 我已筋疲力盡,奄奄一息;我已心痛欲絕,嗟嘆不已。
Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
9 我主,我的呻吟常在你的面前,我的悲歎不向你隱瞞;
Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
10 我的心顫慄,我的精力衰退,我眼目的光明也已消逝。
Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
11 我遭難時,我的友朋都袖手旁觀,我的親人都站得很遠。
Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
12 追尋我命的人,張設網羅,設法害我的人,散布惡謨,他們行詭計日夜思索。
Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
13 但我好像是一個有耳聽不見的聾子,我又好像是一個有口不能言的啞巴。
Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
14 我竟成了一個沒有聽覺的人,成了一個口中沒有辯詞的人。
Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
15 因為我唯有仰慕你,上主,你必應允我,我主我天主!
Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
16 我原來說過:「不要讓他們洋洋得意,不要讓他們因我的失足而沾沾自喜。」
Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
17 我生來就易於失足,因此我常心懷痛苦。
Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
18 我的確承認我犯了罪愆,我為了我的過惡而憂慚。
Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
19 無故加害我的人,力強兇暴,無理憎恨我的人,成群結伙;
Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
20 他們都以怨報德而對待我,因我追求正義而惱恨我。
Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
21 上主,求你不要捨棄我,我主,求你不要遠離我。
Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
22 我的上主,我的救助,求你速來給我護祐。
Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

< 詩篇 38 >