< 詩篇 33 >

1 義人,你們要向上主踴躍歡呼,正直的人,理當讚美上主。
Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
2 我們要彈琴,稱謝上主,彈奏十絃琴,讚頌上主。
Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
3 我們應向上主高唱新歌,在歡呼之聲中奏琴吟詠,
Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
4 因為上主聖言是正直的,上主一切作為都忠實的;
Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
5 上主愛護正義和公理,上主的慈愛瀰漫大地。
Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
6 因上主的一句話,諸天造成;因上主的一口氣,萬象生成。
Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
7 上主把海水好像裝在皮囊,上主將汪洋好像貯在池塘。
Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
8 願整個大地敬愛上主,願普世居民敬愛上主,
Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
9 因為祂一發言,萬有造成,祂一出命,各物生成。
Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
10 上主使異邦的計畫無緒,使萬民的策略廢去。
Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
11 上主的計畫卻永恒不變,祂心中的謀挌萬世常傳。
Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
12 尊上主為自天主的民族,真是有福!上主選為自己產業的百姓,真是有福!
Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
13 上主由高天監臨,注視亞當的子孫;
Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
14 上主由自己居處,視察大地的眾庶:
kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
15 上主創造眾人的心靈,上主知曉人的一切言行。
Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
16 帝王不是因兵多而取勝,勇士不是因力大而保命。
Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
17 為獲勝利,駿馬乃是徒然,氣力雖大,依舊難獲安全。
Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
18 請看上主的眼睛常關注敬愛祂的人,祂的雙目常眷顧靠祂仁慈的人,
Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
19 為使他們的性命,脫免死亡,為使他們在饑饉時,生活如常。
kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
20 我們的靈魂仰望上主,祂是我們的保障和扶助;
Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
21 我們的心靈要因祂而喜樂歡暢,在祂的聖名內寄托我們的希望。
Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
22 上主,求你向我們廣施慈愛,有如我們對你所存的期待。
Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.

< 詩篇 33 >