< 詩篇 2 >

1 【默西亞必勝】萬邦為什麼囂張,眾民為什麼妄想?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 世上列民群集一堂,諸侯畢至聚首相商,反抗上主,反抗他的受傅者:
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 來!我們掙斷他們的綑綁,我們擺脫他們的繩韁!
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 坐於天上者在冷笑,我主對他們在熱嘲。
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 在震怒中對他們發言,在氣焰中對他們喝道:
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 我已祝聖我的君王,在熙雍我的聖山上。
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 我要傳報上主的聖旨:上主對我說:你是我的兒子,我今日生了你。
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 你向我請求,我必將萬民賜你作產業,我必將八極賜你作領地。
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 你必以鐵杖將他們粉碎,就如打破陶匠的瓦器。
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 眾王!你們現在應當自覺,大地掌權者!你們應受教:
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 應以敬愛之情事奉上主,戰戰兢兢向祂跪拜叩首;
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 以免祂發怒將你們滅於中途,因為祂的怒火發怒非常快速。凡一切投奔祂的人真是有福。
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

< 詩篇 2 >