< 詩篇 132 >

1 上主,求您以慈愛懷念達味,和他所有的一切焦思勞瘁:
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Inu Yehova, kumbukirani Davide ndi mavuto onse anapirira.
2 因為他曾向上主立過了誓言,向雅各伯的全能者許過願:
Iye analumbira kwa Yehova ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,
3 我決不進入我住家中的帳幔,也決不登上我躺臥的床沿,
“Sindidzalowa mʼnyumba mwanga kapena kugona pa bedi langa:
4 不容許我的眼睛睡眠,也不讓我的眼臉安閑,
sindidzalola kuti maso anga agone, kapena zikope zanga ziwodzere,
5 直到我給上主尋找到一個處所,給雅各伯的全能者將居地覓妥。
mpaka nditamupezera malo Yehova, malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”
6 看,我們聽說約櫃在厄弗辣大,我們在雅阿爾的平原找到了它。
Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata, tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:
7 大家一同進祂的居所,並在祂的腳凳下崇拜說:
“Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo; tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.
8 上主,請您和您威嚴的約櫃,起來駕臨到您安息的住宅,
‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira, Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.
9 願您的司祭身披正義,願您的信徒踴躍歡喜。
Ansembe anu avekedwe chilungamo; anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’”
10 為了您僕人達味的情面,不要將您的受傅者輕看!
Chifukwa cha Davide mtumiki wanu, musakane wodzozedwa wanu.
11 上主既然向達味起了誓,真理的約言決不再收回:我要使您的親生兒子,榮登上您自己的王位;
Yehova analumbira kwa Davide, lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha: “Mmodzi wa ana ako ndidzamuyika pa mpando waufumu;
12 若您的子孫遵守我的誓言,也遵守我教訓他們的法典,連他們的子孫代代世世,也必定要坐上您的王位。
ngati ana ako azisunga pangano langa ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa, pamenepo ana awo adzakhala pa mpando wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”
13 的確上主特別揀選了熙雍,希望熙雍作為自己的王宮:
Pakuti Yehova wasankha Ziyoni, Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:
14 就是我的永遠安息之處,我希望的是常在這裏居住。
“Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi; ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.
15 我要祝福這裏的食糧充裕,窮人都無憂並且吃得飽飫,
Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri; anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.
16 使這裏的司祭得蒙救助,使這裏的信徒踴躍歡愉。
Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso, ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.
17 在這裏我要使達味的頭角高聳,我要給我的受傅者備妥明燈,
“Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.
18 我要使他的敵人個個恥辱備嘗,我要使他的王冠在頭上發光。
Ndidzaveka adani ake manyazi, koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”

< 詩篇 132 >