< 詩篇 119 >

1 品行完美遵行上主法律的,這樣的人才算是真有福的,
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 遵守上主誡命全心尋求祂的,這樣的人才算是真有福的。
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 他們總不為非作惡,只按祂的道路生活。
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 您頒發了您的命令,叫他們嚴格去遵行。
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 願我的行徑堅定,為遵守您的章程!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 我若重視您的每條誡律,我就絕對不會蒙羞受辱。
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 我一學習您正義的判詞,就以至誠的心靈頌謝您。
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 我要遵守您的規矩,不要將我完全棄去!
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 青年怎樣才能守身如玉?那就只有遵從您的言語。
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 我要用我整個心尋覓您,不要讓我錯行您的諭旨!
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 我將您的話藏在我心裏,免得我犯罪而獲罪於您。
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 上主,您理應受讚頌,教訓我遵守您的誡命。
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 您所傳授的一切法度,我要以我的脣舌敘述。
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 我喜愛您約法的道路,就如喜愛一切的財富。
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 我要默想上主的法度,要沉思您一切的道路。
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 我喜歡您一切的章程,我永遠不忘您的聖言。
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 請恩待您的僕人我得以生存,這樣使我能夠服從您的綸音。
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 求您開明我的眼睛,透視您法律的奇能。
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 我原是寄居塵世的旅客,不要向我隱瞞您的規則。
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 我因常常渴慕您的諭令,我的靈魂便為此而成病。
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 您已經怒責了驕矜橫蠻的人,背棄您誡命的,是可咒詛的人。
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 請除去我所受的淩辱與輕謾,因為我已經遵守了您的規範。
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 判官雖然反對我而開庭,您僕人仍然默思您的章程。
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 因為您的誡命是我的喜樂,您的典章是我的謀士。
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 我的靈魂雖已輾轉於灰塵,求你照你的諾言使我生存。
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 我陳明我的行徑,您便垂聽了我;
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 請指給我您約法的路徑,我要沉思您的奇妙工程。
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 我的靈魂因憂傷而滴滴流淚,請照您的諾言使我奮昂興起。
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 求您不要使我走錯誤的道路,求您賜我常遵守您的法度。
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 我揀定真理的途徑,我矢志服從您的諭令。
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 我時常依戀著您的法度,上主不要叫我蒙受羞辱。
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 我必奔赴您誡命的路程,因為您舒展了我的心靈。
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 上主,給我指出您章程的道路,我要一直到死仔細遵守。
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 求您教訓我遵守您的法律,我要以整個心靈持守不逾。
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 求您引導我走您誡命的捷徑,因為這捷徑使我非常高興。
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 使我的心傾慕您的律例,不要讓我的心貪財好利。
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 求您轉回我的眼目免看虛榮,求您按照您的道路賜我生命。
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 求您向您的僕人實踐您的許諾,即您向敬愛您的人所許的恩賜。
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 求您除去我所怕的羞恥,因為您的約法是我的甘飴。
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 我如何渴慕您的規約,按照您的正義賜我生活。
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 上主,願您的仁慈和救恩,照您的諾言臨於我身!
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 對凌辱我的人,我有所答辯,因為我全寄望於你的聖言。
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 不要由我口撤去真理的訓言,因我一心一意渴望你的判斷。
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 我要常常遵守你的法典,時時不斷,一直要到永遠。
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 我要行走平坦寬闊的途徑,因為我常常追求你的誡命。
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 我要傳述您的規律,在列王前也不畏懼。
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 我非常喜悅您的規誡,因為我對此有所鍾愛。
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 我向您的誡命舉起我的手,對您的一切章程沉思不休。
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 求您莫把您給您的僕人的諾言遺忘,因為您在這諾言裏賜給我希望。
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 在我的憂苦中,這是我的安慰,因為您的聖言,賜給了我生氣。
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 驕傲人雖加給我極度的侮辱,但我卻沒有偏離過您的法律。
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 我一思到您永怚的斷定;上主,我是多麼安慰而高興。
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 為了背棄您法律的罪人,我不知不覺地恕火焚心。
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 在我這客居不定的寓所,您的法令成了我的詩歌。
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 上主,夜間我想起您的聖名,我就決意遵守您的法令。
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 我之所以如此這般,因我遵守您的規範。
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 上主,我說:我的福分,就是遵守您的教訓。
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 我全心仰膽著您的容貌,求您按您的諾言憐憫我。
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 我一默想到我所走的道路,就把我的腳轉您的法度。
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 爽爽快快,毫不躊躇,我常遵守您的法度。
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 惡人的繩索雖將我纏起,我郤未將您的法律忘記。
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 為了您正義的判語,我半夜起身讚美您。
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 我常向敬愛您的人為友,與遵守您誡命的人為侶。
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 上主,您的慈愛充滿大地,求您教我遵守您的律例。
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 上主,您依照您的言詞,善待了您的僕役。
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 您以知識和聰慧教訓我,我要一心信賴您的誡條。
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 我在受苦以前徘徊岐途,但我現今順從您的訓語。
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 您是慈善的,好施仁惠,求您給我教授您的規矩。
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 驕傲人捏造謊言陷害我,我要全心遵守您的規約。
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 他們的心遲純如蒙脂肪,然而我卻喜歡您的典章。
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 為叫我能學習您的法度,受若遭難於我確有好處。
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 您頒的法律對我的利益,連千萬的金銀也不能比。
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 您的雙手創造了我,形成了我;求您賜我智力,為學您的誡條。
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 敬愛您的人,見我就喜歡;因為我常仰望您的聖言。
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 上主,我知道您的審判是公正無私的,您叫我遭受磨難是理所當然的。
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 照您給您僕人的許諾,按您的仁慈來安慰我。
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 願您的仁愛臨於我,使我生活,因為您的法律就是我的喜樂。
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 願無端難為我的驕傲人蒙羞!但是我要默想沉思您的法律。
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 願那些敬愛您的人歸向我,願關心您的人依附我!
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 願我全心遵守您的法典,這樣我便不致自覺羞赧。
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 我靈渴慕您的救援而衰弱,我熱切地盻望著您的許諾。
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 我對您的諾言望眼欲穿,究竟您何時才賜我慰安?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 我雖然相似煙熏的皮囊,我仍然不忘卻您的典章。
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 您僕人的歲月還能有多久?您何時處罰迫害我的惡徒?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 不按您法律生活的驕傲人,暗中給我挖掘了陷阱深坑。
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 您所有的一切誡命全是真道;他們無理迫害我,求您協助我。
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 我們幾乎將我由地上滅絕,但我卻沒有背棄您的規誡。
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 您按照您的仁慈使我生活,這樣我必遵守您口中的條約。
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 上主您的聖言,永遠存留,它堅固而不移,好似蒼天。
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 您所有的忠誠,代代流傳,您所造的大地,屹立不變。
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 天地時常遵守您的旨意,因為萬物都是您的僕役。
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 我如果不喜愛您的法令,我早已在我苦患中喪命。
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 我永遠不忘卻您的法令,因為您藉此賜給我生命。
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 我全屬於您,求您救拔我,因為我尋求了您的法約。
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 惡人窺視我,忌把我殺害,然而我仍細想您的規誡。
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 我看任何齊全的都有界限,唯您的誡命卻廣闊無邊。
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 上主,我是多麼愛慕您的法律,它是我終日對默想的題目。
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 您的誡命永遠存在於我心,它使我比我的仇敵聰明。
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 我比我所有的教師更聰明,因為我常默想您的法令。
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 我比老年的人更有智慧,因為我恪守您的律例。
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 我使我的腳迴避一切惡路,為叫我能夠遵守您的言語。
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 我不偏離您的約法,因為是您教訓了我。
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 您的教言對我上顎多麼甘美!在我的口中比蜂蜜更要甘美!
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 由您的誡命,我獲得了聰明,因我憎惡一切欺詐的途徑。
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 上主,您的言語是我腳步的明燈,是我路途上的光明。
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 我今起誓,我要定志,堅守您正義的諭令。
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 上主,我已經受苦很重,照您的諾言,保我生命。
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 上主,請悅納我口中的祭獻,請教訓我明白您的審斷。
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 我的生命常處於危險中,但我仍不忘記您的法典。
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 惡人雖然給我設下陷阱,我仍然不偏離您的章程。
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 您的誡命永做我的家產,因為這是我心中的喜歡。
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 我要傾心遵守您的法典,千秋萬世,一直到永遠。
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 我惱恨心懷二意的人,對您的法律,我喜愛萬分。
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 您是我的庇護我的盾牌,因此我唯您的聖言是賴。
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 作惡的人,您們應離我遠去!因為我要遵守天主的法度。
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 照您的諾言,扶持我的生命,不要讓我的希望成成為泡影。
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 求您扶持我得蒙拯救,能時常留意您的制度。
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 凡背棄您法令的,您都鄙棄,因為他們的思念全是詐欺。
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 地上的惡人您都看作渣滓,因此我非常喜愛您的法制。
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 我的肉身因敬愛您而戢戰憟,對您的諭令失也知所敬愛。
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 我行正義及合法律的事情,別把我交於壓迫我的壞人。
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 求您保證您僕人的安全,沒有驕傲心將我磨難。
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 對您的救助和正義的諾言,我熱切渴盻已經望眼欲穿。
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 求您照您的仁慈恩待您的僕人,也求您教訓我能明白您的章程。
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 我是您的僕人,求賜我明達,為使我能夠通曉您的約法。
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 現今是上主行動的時候,因他們違反了您的法度。
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 所以我愛慕您的誡律,遠勝各種黃金和寶玉。
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 我尊重您的一切誡命,憎惡所有的欺詐途徑。
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 您的約法誠然是美妙神奇,因此我的靈魂要遵守不離。
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 您的言語經過解釋必會發亮光照,連知識淺薄的人也可以通達知曉。
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 我張開我的口嗟嘆唏嚧,因為我極渴慕您的誡律。
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 求您回身向我,垂憐我,如素常對待愛您名者然。
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 引導我的腳步履行您的訓誥,不要允許任何邪惡來主宰我。
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 求您救我擺挩人的欺壓,為使我能遵守您的律法。
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 求您給您的僕人顯示您的慈顏,同時也您們給我教導您的規範。
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 我的眼淚滴滴下流有如溪水,因為他們全不遵守您的法規。
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 上主,您原是公義的,您的判決是正直的。
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 您以正義和至誠,立定了您的誡命。
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 我的熱火快要將我消耗殆盡,因為我的敵人忘了您的聖訓。
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 您的教言經過千捶百鍊,您的僕人對它愛不知倦。
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 我雖然年記幼小,被人輕看,可是我總不忘卻您的法範。
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 您的正義永遠公正,您的法律永遠堅定。
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 困苦和壓迫雖然來臨我身,但您的誡命仍是我的歡欣。
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 您的約法永遠公允,賜我智慧,使我生存。
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 我全心呼號,並求您俯聽,上主,我要遵守您的法令。
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 我呼號您,求您救護,我必遵守您的法度。
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 天還未亮,我就起來求助,熱切期待您的訓語,
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 夜裏每更,我都睜開眼睛,全是為了您的聖訓。
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 上主,請照您的仁慈俯聽我的呼聲,上主,請照您的正義使我得以重生。
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 非法迫害我的人已經臨近,他們都遠離了您的法令。
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 上主,願您時常與我親近,您一切的誡命全屬忠信。
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 我早就已由您的約法得知,那都是您從永遠所立定。
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 求您垂視我的苦難而救拔我、因為我媲沒有忘記您的約法。
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 求您辯護我的案件而拯救我,並請依照您的諾言,使我生活。
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 恨不得救恩達達離開惡徒,因為他們不理睬您的法度。
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 上主,您的仁愛何其廣闊,按照您的諭旨,賜我生命。
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 迫害與磨難我的人確實眾多,然而我卻不曾偏離您的法約。
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 奸黨惡輩我一看見就會生厭,因為他們都不遵守您的規範。
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 上主,請您看我如何愛您的訓令,上主,照您的仁慈保全我的生命。
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 您聖言的總綱確是真實無欺,您正義的一切判斷永遠不移。
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 王侯雖然無緣無故加我苦難,我的心靈仍舊敬愛您的教言。
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 我對您的諾言實在歡喜若狂,像得到許多勝利品的人一像。
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 奸詐邪惡是我所恨所愛的,您的法令是我所喜所愛的。
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 為了您那正義的判詞,我一要讚美您七次。
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 愛慕您法律的必飽享平安,沒有一點失足跌倒的危險。
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 上主,我期待您的助佑,上主,我遵守您的法度。
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 我的靈魂恪守您的規誡,因為我對規誡十分喜愛。
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 我必要遵守您的規誡和勸言,因我的一切道路在您的面前。
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 上主,願我呼聲上達於您,求您照您的約言使我明理。
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 願我的祈求到達您的面前,求您照您的諾言救我脫險。
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 願我的雙脣湧溢讚美歌曲!因為您給我教授您的法律。
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 願我的舌頭歌詠您的訓令!因您的一切誡命盡屬公正。
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 願您伸出您的手救助我!因為我揀選您的法約。
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 上主,我渴望您的救援,您的法律是我的喜樂。
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 願我的靈魂活著讚美您,願您的斷語來支持我!
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 我像迷路的亡羊,請尋回您的僕人,因為我總沒有忘記您任何的誡命。
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< 詩篇 119 >